那鸿书 2 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

那鸿书 2:1-13

尼尼微的覆灭

1尼尼微啊,

攻击者已经向你扑来。

你要进驻堡垒,

把守道路,

集中全力,

准备上阵!

2虽然掳掠者曾掳掠雅各

掳掠以色列

毁坏他们的葡萄树枝,

但耶和华必恢复雅各的荣耀,

恢复以色列的荣耀。

3他的勇士手持红色盾牌,

他的士兵身穿朱红战衣。

整装待发之日,

战车铁光闪闪,

松木矛枪在空中挥舞。

4战车在街道上狂奔,

在广场上横冲直撞,

亮如火炬,疾似闪电。

5亚述王召集将领,

他们一路跌跌撞撞,

奔上城墙,架起防御盾牌。

6河闸大开,王宫坍塌。

7王后赤身被掳;

宫女捶胸悲泣,

像鸽子一样哀鸣。

8尼尼微城自古以来就像聚水的池子,

如今居民却像泄漏的池水四散奔逃。

虽有人喊:“站住!站住!”

却无人回头。

9抢银子吧!抢金子吧!

城里有无尽的财富和数不清的宝物。

10尼尼微被洗劫一空!

被洗劫一空!

一片荒凉!

人们胆战心惊,双膝哆嗦,

浑身发抖,面色苍白。

11如今那狮子的洞穴,

那喂养壮狮的地方在哪里呢?

从前,雄狮、母狮和幼狮曾在那里出入,

无人惊扰。

12雄狮为幼狮撕碎充足的食物,

为母狮掐死猎物,

洞穴里堆满猎物,

堆满撕碎的肉。

13万军之耶和华说:

“我要与你为敌,

烧毁你的战车,

使刀剑吞噬你的壮狮;

我要使你无法再掳掠他国,

你使者的声音将从此消逝。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nahumu 2:1-13

Kugwa kwa Ninive

1Wodzathira nkhondo akubwera

kudzalimbana nawe, Ninive.

Tetezani malinga anu,

dziyangʼanani ku msewu,

konzekerani nkhondo,

valani dzilimbe.

2Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo

ngati ulemerero wa Israeli,

ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu

ndipo anawononganso mpesa wawo.

3Zishango za ankhondo ake ndi zofiira;

asilikali ake avala zovala zofiirira.

Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira

tsiku la kukonzekera kwake.

Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.

4Magaleta akuthamanga mʼmisewu

akungothamangathamanga pa mabwalo.

Akuoneka ngati miyuni yoyaka;

akuthamanga ngati chingʼaningʼani.

5Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka,

koma iwo akubwera napunthwa.

Akuthamangira ku linga la mzinda;

akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.

6Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje

ndipo nyumba yaufumu yagwa.

7Zatsimikizika kuti mzinda

utengedwa ndi kupita ku ukapolo.

Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda

ndipo akudziguguda pachifuwa.

8Ninive ali ngati dziwe,

ndipo madzi ake akutayika.

Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!”

Koma palibe amene akubwerera.

9Funkhani siliva!

Funkhani golide!

Katundu wake ndi wochuluka kwambiri,

chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!

10Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa!

Mitima yasweka, mawondo akuwombana,

anthu akunjenjemera ndipo

nkhope zasandulika ndi mantha.

11Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti,

malo amene mikango inkadyetserako ana ake,

kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako,

ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?

12Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake

ndiponso kuphera nyama mkango waukazi,

kudzaza phanga lake ndi zimene wapha

ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.

13Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Ine ndikutsutsana nawe.

Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo,

ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono;

sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi.

Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”