路加福音 24 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

路加福音 24:1-53

耶稣死里复活

1周日黎明时分,几位妇女带着预备好的香料来到坟前, 2发现墓口的大石头已经滚到旁边, 3便进去,却没有看见主耶稣的遗体。 4正在猜疑之间,突然有两个衣服发光的人站在旁边, 5她们吓得俯伏在地。那两个人对她们说:“你们为什么在死人中找活人呢? 6祂不在这里,已经复活了!记住祂在加利利对你们说的话, 7‘人子必须被交在罪人的手中,被钉在十字架上,在第三天复活。’”

8她们想起耶稣的话来, 9便离开墓地回去把事情的经过告诉十一个使徒和其他人。 10这些妇女就是抹大拉玛丽亚约亚娜雅各的母亲玛丽亚及其他人。

11大家听了都不相信,认为是无稽之谈。 12彼得却起身跑到墓地,屈身往墓里张望,只见细麻布在那里,他便离开了,对发生的事大惑不解。

耶稣的显现

13同一天,有两个门徒前往离耶路撒冷十一公里的以马忤斯村, 14一路谈论着最近发生的一切事。 15正谈论的时候,耶稣走过来和他们同行。 16可是,他们认不出耶稣。

17耶稣问他们:“你们一路上在谈论什么?”

他们停下脚步,满面愁容, 18其中一个叫革流巴的说:“难道在耶路撒冷作客的人中,只有你不知道近日发生的大事吗?”

19耶稣问:“什么事?”

他们说:“就是拿撒勒人耶稣的事。祂本来是个先知,在上帝和百姓面前言谈举止充满力量。 20我们的祭司长和官长却把祂押去判了死刑,钉在十字架上。

21“我们一直希望祂就是要拯救以色列的那位。还有,今天是事发后的第三天, 22我们当中有几位妇女一早到耶稣的坟墓, 23发现耶稣的遗体不见了,回来说天使曾向她们显现并告诉她们耶稣已经复活了。

24“后来我们有几个人亲自去坟墓察看,果然像她们所说的,耶稣的遗体不见了。”

25耶稣对他们说:“无知的人啊!为什么迟迟不肯相信先知的话呢? 26基督岂不是要先这样受害,然后进入祂的荣耀吗?”

27耶稣接着从摩西和众先知的记载开始,把有关自己的经文都向他们讲解明白。

28快到以马忤斯村时,耶稣好像还要继续前行。 29他们极力挽留祂,说:“天快黑了,时候不早了,跟我们一同住宿吧。”耶稣就和他们一起进村住下。

30吃饭的时候,耶稣拿起饼来,祝谢后,掰开递给他们。 31忽然他们眼睛明亮了,认出是耶稣。耶稣很快从他们眼前消失了。

32二人彼此议论说:“一路上祂和我们说话、为我们解释圣经的时候,我们心里不是很火热吗?” 33二人马上赶回耶路撒冷,看到十一位使徒及其同伴正聚在一起谈论: 34“主真的复活了,祂向西门显现了。”

35二人也把路上发生的事以及掰饼时认出主的经过述说了一遍。

36正说的时候,耶稣出现在他们中间,说:“愿你们平安!” 37他们又惊又怕,以为是看见了鬼魂。

38耶稣说:“你们为什么忧心忡忡?为什么心存疑惑呢? 39你们看我的手和脚,就知道真的是我。来摸摸看,鬼魂没有骨和肉,你们看!我有。” 40说完,便伸出手和脚给他们看。

41门徒又惊又喜,半信半疑。耶稣问:“你们这里有吃的吗?” 42他们便给祂一片烤鱼, 43祂接过鱼来在他们面前吃了。

44耶稣对他们说:“我跟你们在一起的时候曾经说过,摩西的律法书、先知的书以及诗篇里有关我的记载都要应验。” 45于是,耶稣开启了他们的心窍,使他们明白这些经文, 46又对他们说:“圣经上说,基督必受害,然后在第三天从死里复活, 47人们要奉祂的名传扬悔改、赦罪的福音,从耶路撒冷一直传遍万国。

48“你们是这些事的见证人, 49我要把我父所应许的赐给你们。不过,你们要留在城里,直到你们得到天上来的能力。”

耶稣升天

50耶稣带着门徒来到伯大尼附近,举起双手为他们祝福。 51正祝福的时候,祂就离开了他们,被接到天上去了。 52门徒都敬拜祂,然后欢欢喜喜地回到耶路撒冷53他们常在圣殿里赞美上帝。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 24:1-53

Yesu Auka kwa Akufa

1Pa tsiku loyamba la Sabata, mmamawa kwambiri, amayi anatenga zonunkhira napita ku manda. 2Anaona mwala wa pa manda utagubuduzika 3ndipo atalowamo sanapeze mtembo wa Ambuye Yesu. 4Pamene iwo ankadabwa za zimenezi, mwadzidzidzi, amuna awiri ovala zovala zonyezimira kwambiri anayimirira pambali pawo. 5Ndi mantha, amayiwo anaweramitsa nkhope zawo pansi, koma amunawo anawawuza kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufuna wamoyo pakati pa akufa? 6Iye sali muno ayi. Wauka! Kumbukirani zimene anakuwuzani pamene anali nanu ku Galileya: 7‘Mwana wa Munthu ayenera kuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa, napachikidwa ndipo tsiku lachitatu adzaukitsidwanso.’ ” 8Ndipo anakumbukira mawu ake.

9Atabwerera kuchokera ku mandako, anafotokoza zinthu zonse kwa khumi ndi mmodziwo ndi kwa ena onse. 10Amayi anali Mariya Magadalena, Yohana, Mariya amayi a Yakobo, ndi ena anali nawo amene anawuza atumwi. 11Koma iwo sanawakhulupirire amayiwa, chifukwa mawu awo amaoneka kwa iwo ngati opanda nzeru. 12Komabe Petro anayimirira ndi kuthamangira ku manda. Atasuzumira, anaona nsalu zimene anamukulungira zija zili pa zokha, ndipo iye anachoka, akudabwa ndi zimene zinachitikazo.

Zochitika pa Njira ya ku Emau

13Ndipo tsiku lomwelo, awiri a iwo ankapita ku mudzi wotchedwa Emau, pafupifupi makilomita khumi ndi imodzi kuchokera ku Yerusalemu. 14Iwo ankayankhulana za zonse zimene zinachitikazo. 15Pamenepo Yesu mwini wake anabwera ndi kuyenda nawo pamodzi; 16koma iwo sanamuzindikire.

17Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukukambirana zotani mʼnjira muno?”

Iwo anayima ndi nkhope zakugwa. 18Mmodzi wa iwo wotchedwa Kaliyopa anamufunsa kuti, “Kodi ndiwe wekha wokhala mu Yerusalemu amene sukudziwa zinthu zimene zachitika mʼmasiku awa?”

19Iye anafunsa kuti, “Zinthu zotani?”

Iwo anayankha nati, “Za Yesu wa ku Nazareti, Iye anali mneneri, wamphamvu mʼmawu ndi mu zochita pamaso pa Mulungu ndi anthu onse. 20Akulu a ansembe ndi oweruza anamupereka Iye kuti aphedwe, ndipo anamupachika Iye; 21koma ife tinkayembekezera kuti Iye ndiye amene akanawombola Israeli. Ndipo kuwonjeza apo, lero ndi tsiku lachitatu chichitikireni izi. 22Kuwonjezanso apo, ena mwa amayi athu atidabwitsa ife. Iwo anapita ku manda mmamawa 23koma sanakapeze mtembo wake. Iwo anabwera ndi kudzatiwuza ife kuti anaona masomphenya a angelo amene anati Yesu ali moyo. 24Kenaka ena mwa anzathu anapita ku manda ndipo anakapeza monga momwe amayiwo ananenera, koma Iye sanamuone.”

25Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu anthu opusa, osafuna kukhulupirira msanga zonse zimene aneneri ananena! 26Kodi Khristu sanayenera kumva zowawa izi ndipo kenaka ndi kulowa mu ulemerero wake?” 27Ndipo kuyambira ndi Mose ndi aneneri onse Iye anawafotokozera zimene zinalembedwa mʼmalemba wonse zokhudzana ndi Iye mwini.

28Atayandikira mudzi omwe amapitako, Yesu anachita ngati akupitirira. 29Koma iwo anamupempha Iye kwambiri kuti, “Mukhale ndi ife, popeza kwatsala pangʼono kuda, ndipo dzuwa lili pafupi kulowa.” Ndipo Iye anapita kukakhala nawo.

30Iye ali pa tebulo pamodzi nawo, anatenga buledi ndipo anayamika, nanyema nayamba kuwagawira. 31Kenaka maso awo anatsekuka ndipo anamuzindikira Iye, ndipo anachoka pakati pawo. 32Iwo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi mitima yathu sinali kutentha mʼkati mwathu pamene Iye ankayankhulana nafe pa njira ndi mmene anatitsekulira malemba?”

33Nthawi yomweyo iwo anayimirira ndi kubwerera ku Yerusalemu. Iwo anapeza khumi ndi mmodziwo ndi ena anali nawo nasonkhana pamodzi 34ndipo anati, “Ndi zoonadi! Ambuye auka ndipo anaonekera kwa Simoni.” 35Kenaka awiriwo anawawuza zimene zinachitika pa njira, ndi mmene iwo anamudziwira Yesu, Iye atanyema buledi.

Yesu Aonekera kwa Ophunzira

36Akufotokoza zimenezi, Yesu mwini wake anayimirira pakati pawo ndipo anati, “Mukhale ndi mtendere.”

37Koma chifukwa choti anathedwa nzeru ndi kuchita mantha, ankaganiza kuti akuona mzukwa. 38Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuvutika? Nʼchifukwa chiyani mukukayika mu mtima mwanu? 39Taonani manja anga ndi mapazi anga. Ine ndine amene! Khudzeni kuti muone. Mzukwa ulibe mnofu ndi mafupa monga mukuonera ndili nazo.”

40Iye atanena izi anawaonetsa manja ake ndi mapazi ake. 41Ndipo pamene iwo samakhulupirirabe, chifukwa cha chimwemwe ndi kudabwa, Iye anawafunsa kuti, “Kodi muli ndi chakudya chilichonse pano?” 42Iwo anamupatsa Iye kachidutswa ka nsomba yophika. 43Iye anakatenga ndi kukadya iwo akuona.

44Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene ndinakuwuzani pamene ndinali nanu: chilichonse chiyenera kukwaniritsidwa chimene chinalembedwa cha Ine mʼbuku la Malamulo a Mose, Aneneri ndi Masalimo.”

45Kenaka anawatsekula maganizo kuti azindikire Malemba. 46Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene zinalembedwa: Khristu adzazunzika ndipo adzauka kwa akufa tsiku lachitatu. 47Ndipo kutembenuka mtima ndi kukhululukidwa kwa machimo zidzalalikidwa mu dzina lake kwa anthu amitundu yonse kuyambira mu Yerusalemu. 48Inu ndinu mboni za zimenezi. 49Ine ndidzakutumizirani chimene Atate anga analonjeza. Koma khalani mu mzinda muno mpaka mutavekedwa mphamvu yochokera kumwamba.”

Kupita Kumwamba

50Iye atawatengera kunja kwa mzindawo mpaka ku Betaniya, anakweza manja ake ndi kuwadalitsa. 51Iye akuwadalitsa, anawasiya ndipo anatengedwa kupita kumwamba. 52Pamenepo anamulambira Iye ndipo anabwerera ku Yerusalemu ndi chimwemwe chachikulu. 53Ndipo iwo anakhalabe ku Nyumba ya Mulungu, akulemekeza Mulungu.