路加福音 22 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

路加福音 22:1-71

犹大出卖耶稣

1除酵节,又名逾越节,快到了。 2祭司长和律法教师因为害怕百姓,便密谋如何杀害耶稣。 3这时,撒旦进入加略犹大的心,这人原是十二使徒之一。 4他去见祭司长和圣殿护卫长,商议如何把耶稣出卖给他们, 5他们喜出望外,答应给犹大一笔酬金。 6犹大同意了,便伺机找百姓不在的场合将耶稣交给他们。

最后的晚餐

7除酵节到了,那天要宰杀逾越羊羔。 8耶稣差派彼得约翰出去,说:“你们为我们准备逾越节吃的晚餐。”

9他们问:“你要我们到哪里去预备呢?”

10耶稣回答说:“你们进城的时候,一个男子会扛着一瓶水迎面走来,你们要跟着他,他进哪所房子,你们也进去, 11对房子的主人说,‘老师问你客房在哪里,祂要和门徒在里面吃逾越节的晚餐。’ 12那主人会带你们到楼上一间布置整齐的大房间,你们就在那里预备吧。”

13他们进了城,所遇见的果然和耶稣所说的一样。他们便在那里预备逾越节的晚餐。

设立圣餐

14晚餐时,耶稣和使徒们一同坐席。 15耶稣对他们说:“我一直盼望在受难之前和你们同吃这个逾越节的宴席。 16我告诉你们,在这宴席成就在上帝的国度之前,我不会再吃这宴席了。”

17祂接过杯来,祝谢后,说:“你们拿去分着喝吧。 18我告诉你们,在上帝的国降临之前,我不会再喝这葡萄酒了。”

19接着,祂拿起饼来,祝谢后,掰开递给他们,说:“这是我为你们牺牲的身体,你们今后也要这样做,以纪念我。”

20饭后,祂又举起杯来,说:“这杯是用我的血立的新约,这血是为你们流的。

21“但是看啊,那出卖我之人的手和我的手都在桌子上。 22按照所定的,人子要死去,但那出卖人子的人有祸了!” 23他们开始彼此追问谁会出卖耶稣。

谁最伟大

24门徒又开始争论他们当中谁最伟大。 25耶稣对他们说:“外族人有君王统治他们,那些统治者被称为恩主, 26但你们不可这样。相反,你们中间地位最高的,要像最卑微的;做首领的,要像服侍人的。 27坐着吃饭的和伺候的哪个地位高呢?难道不是坐着的那个吗?然而,我在你们当中是服侍人的。

28“在我患难之时,你们一直在我身边, 29所以,我父怎样将国赐给我,我也照样将国赐给你们, 30使你们在我的国中和我一同坐席,并且坐在宝座上审判以色列的十二个支派。”

预言彼得不认主

31耶稣说:“西门西门!撒旦已经要求像筛麦子一样筛你们, 32但我已经为你祷告了,叫你不至于失去信心。你回头以后,要让你的弟兄刚强。”

33西门·彼得说:“主啊,我愿意和你一起坐牢,一起受死!”

34耶稣说:“彼得,我告诉你,明早鸡叫之前,你会三次不认我。”

35耶稣又问门徒:“我派你们出去的时候,无钱袋、背包和鞋子,你们有任何缺乏吗?”

他们答道:“没有。”

36耶稣说:“但现在如果有钱袋或背包,都要带着;如果没有刀剑,要卖掉衣服买刀剑。 37我告诉你们,‘祂要被列在罪犯中’这句经文必在我身上应验,因为圣经上有关我的事情快要实现了。”

38他们说:“主啊,请看,这里有两把刀。”耶稣说:“够了。”

橄榄山上的祷告

39耶稣离开,像往常一样前往橄榄山,门徒也跟去了。 40到了山上,祂对门徒说:“你们要祷告,以免陷入诱惑!”

41然后,祂独自走到离门徒约有扔一块石头那么远的地方跪下祷告: 42“父啊,若你愿意,求你撤去此杯。然而,愿你的旨意成就,而非我的意愿。” 43有一位从天上来的天使向祂显现,给祂加添力量。

44祂心中极其悲痛,祷告更恳切,汗珠如血滴在地上。

45祂祷告完后,便起身回到门徒那里,看见他们因忧愁而疲惫地睡着了, 46就说:“你们为什么睡觉呢?要起来祷告,以免陷入诱惑!”

耶稣被捕

47耶稣还在说话的时候,十二使徒中的犹大已带着一群人赶到,他上前亲吻耶稣。 48耶稣对他说:“犹大,你用亲吻的暗号来出卖人子吗?”

49跟随耶稣的人见他们来势汹汹,就说:“主啊,我们该拔刀抵抗吗?” 50其中一人拔刀朝大祭司的奴仆砍过去,削掉了他的右耳。

51耶稣却说:“住手!够了!”于是祂摸那奴仆的耳朵,治好了他, 52然后对前来抓祂的祭司长、圣殿护卫长和长老说:“你们像对付强盗一样拿着刀棍来抓我吗? 53我天天和你们一起在圣殿里,你们没有抓我。但现在正是黑暗当权、你们得势的时候了!”

彼得不认主

54他们把耶稣押到大祭司的府第。彼得远远地跟在后面。

55他们在庭院当中生起了火,围坐取暖,彼得也坐在他们中间。 56有个婢女看见彼得坐在火堆边,打量他一番后,说:“这人是与耶稣一伙的!”

57彼得却否认说:“你这女子,我不认识祂。”

58过了一会儿,又有个人看见了彼得,就说:“你也是跟他们一伙的!”

彼得说:“你这人,我不是!”

59大约一小时之后,又有人指着彼得肯定地说:“这人确实是和耶稣一伙的,因为他也是加利利人。”

60彼得说:“你这人,我不知道你在说什么!”话才出口,鸡就叫了。

61这时,主转过头来望着彼得彼得想起主对他说的话:“明早鸡叫之前,你会三次不认我。” 62他就到外面,痛哭起来。

在公会受审

63看守耶稣的人嘲弄祂,殴打祂, 64蒙住祂的眼睛,对祂说:“说预言吧!是谁在打你?” 65还说了许多侮辱祂的话。

66天亮后,民间的长老、祭司长和律法教师聚在一起,把耶稣押到他们的公会, 67对祂说:“如果你是基督,就告诉我们。”

耶稣说:“即使我告诉你们,你们也不会相信。 68如果我问你们,你们也不会回答。 69但从今以后,人子要坐在全能上帝的右边。”

70他们都问:“那么,你是上帝的儿子吗?”耶稣回答说:“你们说我是。”

71他们说:“我们还需要什么见证呢?我们已经听见祂自己说的了。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 22:1-71

Yudasi Avomera Kumupereka Yesu

1Phwando la buledi wopanda yisiti lotchedwa Paska litayandikira, 2akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo amafunafuna mpata woti amuphere Yesu, pakuti ankachita mantha ndi anthu. 3Kenaka Satana analowa mwa Yudasi, wotchedwa Isikarioti, mmodzi wa khumi ndi a iwiriwo. 4Ndipo Yudasi anapita kwa akulu a ansembe ndi akulu oyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndi kukambirana nawo za mmene iye angaperekere Yesu. 5Iwo anakondwa ndipo anagwirizana zomupatsa ndalama. 6Iye anavomera, ndipo anayamba kufunafuna mpata wabwino wakuti amupereke Yesu kwa iwo pamene panalibe gulu la anthu pafupi.

Paska Womaliza

7Kenaka linafika tsiku la buledi wopanda yisiti pamene mwana wankhosa wa Paska amaperekedwa nsembe. 8Yesu anatuma Petro ndi Yohane nati, “Pitani kukatikonzera Paska kuti tikadye.”

9Iwo anafunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonzere kuti?”

10Iye anayankha kuti, “Taonani, mukamalowa mu mzinda, mudzakumana ndi mwamuna atanyamula mtsuko wamadzi. Mulondoleni ku nyumba imene akalowe, 11ndipo mukamuwuze mwini nyumbayo kuti, ‘Aphunzitsi kufunsa kuti, chili kuti chipinda cha alendo, kumene Ine ndi ophunzira anga tikadyere Paska?’ 12Iyeyo adzakuonetsani chipinda chachikulu chapamwamba, chokhala ndi zonse. Kachiteni zokonzekera mʼmenemo.”

13Iwo anapita nakapeza zinthu monga mmene Yesu anawawuzira. Tsono anakonza Paska.

Za Mgonero wa Ambuye

14Ora litakwana, Yesu ndi ophunzira ake anakhala pa tebulo. 15Ndipo Iye anawawuza kuti, “Ine ndakhala ndikuyembekezera kudya Paska uyu ndi inu ndisanamve zowawa. 16Pakuti Ine ndikukuwuzani kuti sindidzadyanso Paska wina mpaka Paskayi itakwaniritsidwa mu ufumu wa Mulungu.”

17Atanyamula chikho, Iye anayamika ndipo anati, “Tengani ndipo patsiranani pakati panu. 18Pakuti ndikukuwuzani kuti, Ine sindidzamwanso zochokera ku chipatso cha mphesa mpaka ufumu wa Mulungu utabwera.”

19Ndipo Iye anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema, nagawira iwo nati, “Ili ndi thupi langa lomwe laperekedwa kwa inu; muzichita zimenezi pokumbukira Ine.”

20Chimodzimodzinso, utatha mgonero, anatenga chikho nati, “Chikho ichi ndi pangano latsopano la magazi anga, amene akhetsedwa chifukwa cha inu. 21Koma dzanja la amene akundipereka Ine lili pamodzi ndi langa pa chakudya pano. 22Mwana wa Munthu apita monga mmene zinalembedwera, koma tsoka kwa munthu amene amupereka Iye.” 23Iwo anayamba kufunsana pakati pawo kuti ndi ndani wa iwo amene akanachita ichi.

Mkangano Pakati pa Ophunzira

24Komanso mkangano unabuka pakati pawo kuti ndani mwa iwo amene amaganiziridwa kukhala wamkulu. 25Yesu anawawuza kuti, “Mafumu a anthu a mitundu ina amaonetsa mphamvu za ufumu wawo pa anthuwo; ndipo amene ali ndi ulamuliro, amapatsidwa dzina la kuti ‘Opindula.’ 26Koma inu simuyenera kukhala choncho. Mʼmalo mwake, wamkulu pakati panu akhale ngati wamngʼono pa onse, ndipo iye amene alamulira akhale ngati wotumikira. 27Pakuti wamkulu ndani, iye amene ali pa tebulo kapena iye amene akutumikira? Kodi si iye amene ali pa tebulo? Koma ndili pakati panu ngati mmodzi wokutumikirani. 28Inu ndinu amene mwayima nane mʼmayesero. 29Ndipo Ine ndikupatsani inu ufumu, monga momwe Atate anga anandipatsiranso Ine, 30kuti inu muthe kudya ndi kumwa pa tebulo langa mu ufumu wanga ndi kukhala pa mipando yaufumu kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israeli.”

Yesu Aneneratu kuti Petro Adzamukana

31“Simoni, Simoni, Satana wapempha kuti akupete ngati tirigu. 32Koma Ine ndakupempherera Simoni, kuti chikhulupiriro chako chisafowoke ndipo pamene udzabwerera kwa Ine, udzalimbikitse abale ako.”

33Koma iye anayankha kuti, “Ambuye, ndine wokonzeka kupita nanu ku ndende ndi kufa komwe.”

34Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuza Petro, tambala asanalire lero lino, udzandikana katatu kuti sukundidziwa Ine.”

35Kenaka Yesu anawafunsa iwo kuti, “Ine nditakutumizani wopanda chikwama cha ndalama, thumba kapena nsapato, kodi inu munasowa kanthu?”

Iwo anayankha kuti, “Palibe chimene tinasowa.”

36Iye anawawuza kuti, “Koma tsopano ngati muli ndi chikwama cha ndalama, chitengeni, ndiponso thumba. Ndipo ngati mulibe lupanga, gulitsani mkanjo wanu ndi kugula. 37Zalembedwa kuti, ‘Ndipo Iye anawerengedwa pamodzi ndi anthu ochimwa,’ ndipo Ine ndikuwuzani kuti izi ziyenera kukwaniritsidwa mwa Ine. Inde, zimene zinalembedwa za Ine, zikukwaniritsidwa.”

38Ophunzira anati, “Taonani Ambuye, awa malupanga awiri.”

Iye anayankha kuti, “Amenewa akwanira.”

Yesu Apemphera ku Phiri la Olivi

39Yesu anapitanso monga mwa masiku onse ku Phiri la Olivi, ndipo ophunzira ake anamutsatira Iye. 40Atafika pamalopo, Iye anawawuza kuti, “Pempherani kuti musagwe mʼmayesero.” 41Iye anapita patsogolo pangʼono patali ngati kuponya mwala, anagwada napephera kuti, 42“Atate ngati mukufuna chotsereni chikho ichi. Komatu muchite zimene mukufuna osati zimene ndikufuna ine.” 43Mngelo wochokera kumwamba anafika namulimbikitsa. 44Ndipo mopsinjika mtima, anapemphera moona mtima, ndipo thukuta lake linali ngati madontho a magazi akugwera pansi.

45Iye atamaliza kupemphera, ndi kubwerera kwa ophunzira ake, anawapeza atagona atafowoka ndi chisoni. 46Iye anafunsa kuti, Nʼchifukwa chiyani mukugona? “Dzukani ndipo pempherani kuti inu musagwe mʼmayesero.”

Amugwira Yesu

47Pamene Iye ankayankhulabe, gulu la anthu linabwera, ndipo munthu wotchedwa Yudasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo analitsogolera. Iye anamuyandikira Yesu kuti amupsompsone. 48Koma Yesu anamufunsa kuti, “Yudasi, kodi ukupereka Mwana wa Munthu ndi mpsopsono?”

49Otsatira Yesu ataona zimene zimati zichitike, anati, “Ambuye, kodi timenyane ndi malupanga athu?” 50Ndipo mmodzi wa iwo anatema wantchito wamkulu wa ansembe, nadula khutu lake lamanja.

51Koma Yesu anayankha kuti, “Zisachitikenso zimenezi!” Ndipo Iye anakhudza khutu la munthuyo ndi kumuchiritsa.

52Kenaka Yesu anafunsa akulu a ansembe, akuluakulu oyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndi akuluakulu ena amene anabwerawo kuti, “Kodi Ine ndikutsogolera gulu lowukira kuti mubwere ndi malupanga ndi zibonga? 53Tsiku lililonse ndinali nanu mʼmabwalo a mʼNyumba ya Mulungu ndipo inu simunandigwire. Koma iyi ndi nthawi yanu pamene mdima ukulamulira.”

Petro Akana Yesu

54Pamenepo anamugwira Iye, napita naye ndipo anamutengera ku nyumba ya mkulu wa ansembe. Petro anamutsatira patali. 55Koma pamene anasonkha moto pakati pa bwalo la milandu, anakhala onse pansi ndipo Petro anakhalanso pansi. 56Mtsikana wantchito anamuona atakhala nawo pafupi ndi moto. Iye anamuyangʼanitsitsa ndipo anati, “Munthu uyu anali ndi Yesu.”

57Koma Petro anakana nati, “Mtsikana, ine sindimudziwa ameneyu.”

58Patatha kanthawi pangʼono, wina wake anamuona ndipo anati, “Iwenso ndiwe mmodzi mwa iwo.”

Petro anayankha kuti, “Munthu iwe, ayi sindine.”

59Patatha pafupifupi ora limodzi, munthu winanso anati, “Zoonadi, munthu uyu anali ndi Iye, pakuti ndi mu Galileya.”

60Petro anayankha kuti, “Munthu iwe, sindikudziwa zimene ukunena apa.” Pamene iye ankayankhula, tambala analira. 61Ambuye anachewuka namuyangʼanitsitsa Petro. Pamenepo Petro anakumbukira mawu amene Ambuye anayankhula kwa iye kuti, “Asanalire tambala lero lino, udzandikana Ine katatu.” 62Ndipo iye anapita panja nakalira kwambiri.

Asilikali Amuchita Chipongwe Yesu

63Anthu amene ankalonda Yesu anayamba kumuchita chipongwe ndi kumumenya. 64Anamumanga mʼmaso ndi kumufunsa kuti, “Tanenera! Wakumenya iwe ndi ndani?” 65Ndipo iwo anamunena zachipongwe zambiri.

Yesu Pamaso pa Pilato ndi Herode

66Kutacha, bungwe la akuluakulu, pamodzi ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anakumana pamodzi, ndipo anamuyika Yesu patsogolo pawo. 67Iwo anati, “Tiwuze, ngati ndiwe Khristu.”

Yesu anayankha kuti, “Ine nditakuwuzani simungandikhulupirire. 68Ine nditakufunsani inu, simungandiyankhe. 69Koma kuyambira tsopano, Mwana wa Munthu adzakhala ku dzanja lamanja la Mulungu wamphamvu.”

70Onse anafunsa kuti, “Ndiye kuti ndiwe Mwana wa Mulungu?”

Iye anayankha kuti, “Mwanena ndinu kuti Ndine.”

71Pamenepo iwo anati, “Nanga tikufuniranjinso umboni wina? Ife tamva kuchokera pa milomo yake.”