路加福音 17 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

路加福音 17:1-37

论罪、信心和本分

1耶稣教导门徒说:“引人犯罪的事是免不了的,但引人犯罪的人有祸了。 2谁使一个卑微的弟兄失足犯罪,他的下场比把大磨石拴在他脖子上扔到海里还要惨。 3你们要小心谨慎!你的弟兄若犯了罪,要责备他。他若悔改,要饶恕他。 4就算他一天得罪你七次,每次都对你说,‘我悔改’,你都要饶恕他。”

5使徒对主说:“请你加添我们的信心。”

6主说:“如果你们的信心像一粒芥菜种那么大,便可对这棵桑树说,‘连根拔起,栽在大海里!’它必服从你们。

7“你们谁会对种田或放羊回来的奴仆说,‘请赶快坐下来吃饭’? 8不都是吩咐他‘给我准备晚饭,束上腰带伺候我用餐,等我吃完,你才可以吃’吗? 9奴仆照着吩咐去做,主人会谢他吗? 10同样,你们照着吩咐把事情办妥后,也该这样说,‘我们是无用的奴仆,所做的不过是分内的事。’”

十个麻风病人

11耶稣继续前往耶路撒冷,途经撒玛利亚加利利的交界处。 12祂进入一个村庄时,十个麻风病人迎面而来。他们远远地站着, 13高声呼喊道:“耶稣,老师啊,求你可怜我们吧!”

14耶稣看见他们,就说:“去让祭司察看你们的身体。”

他们去的时候,就洁净了。 15其中一个发现自己痊愈了,就跑回来,高声赞美上帝, 16又俯伏在耶稣的脚前连连称谢。这人是撒玛利亚人。

17耶稣说:“被医好的不是有十个人吗?其他九个呢? 18回来赞美称颂上帝的只有这个外族人吗?” 19于是祂对那人说:“起来回去吧!你的信心救了你。”

上帝国的降临

20法利赛人问耶稣:“上帝的国什么时候降临?”

耶稣回答说:“上帝国的降临并没有看得见的征兆。 21所以没有人能说,‘上帝的国在这里’,或说,‘在那里’,因为上帝的国就在你们心里17:21 在你们心里”或作“在你们当中”。。”

22祂又对门徒说:“时候将到,你们将渴望见到人子降临的日子,可是你们却见不到。 23有人将对你们说,‘看啊,祂在这里!’或说,‘看啊,祂在那里!’你们不要出去,也不要追随他们。 24因为人子降临的时候必如划过长空的闪电,从天这边一直照亮到天那边。 25但祂必须先受苦,被这个世代弃绝。

26“人子降临时的情形将像挪亚的时代, 27人们吃喝嫁娶,一直到挪亚进入方舟那天,洪水来了,毁灭了他们; 28又像罗得的时代,人们吃喝、做买卖、耕地、盖房。 29罗得离开所多玛那天,烈火和硫磺从天而降,把他们全毁灭了。

30“人子显现之日的情形也是如此。 31那天,在自己屋顶上的,不要下来收拾行李;在田里工作的,也不要回家。 32你们要记住罗得妻子的事。 33想保全生命的,必丧失生命;丧失生命的,必保全生命。 34我告诉你们,那天晚上,两个人睡在一张床上,一个将被接去,一个将被撇下; 35两个女人一起推磨,一个将被接去,一个将被撇下; 36两个人在田间,一个将被接去,一个将被撇下。17:36 有古卷无36节。

37门徒问:“主啊,在哪里有这事呢?”

耶稣回答说:“尸体在哪里,秃鹰就会聚集在哪里。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 17:1-37

Za Uchimo, Chikhulupiriro ndi Ntchito

1Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zinthu zimene zimachimwitsa sizingalephere kubwera, koma tsoka kwa munthu wozibweretsayo. 2Kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala wamphero mʼkhosi mwake kusiyana kuti achimwitse mmodzi mwa ana aangʼonowa. 3Nʼchifukwa chake dziyangʼanireni nokha.

“Ngati mʼbale wanu achimwa, mudzudzuleni, ndipo ngati alapa, mukhululukireni. 4Ngati iye akulakwira kasanu ndi kawiri pa tsiku, ndipo ngati nʼkubweranso kwa iwe kasanu ndi kawiri nati, ‘Ndalapa,’ umukhululukire.”

5Atumwiwo anati kwa Ambuye, “Kulitsani chikhulupiriro chathu!”

6Yesu anayankha kuti, “Ngati muli ndi chikhulupiriro chachingʼono ngati kambewu kampiru, mukhoza kulamula mtengo wamkuyu uwu kuti, ‘Zulidwa ndi kukadzalidwa mʼnyanja,’ ndipo udzakumverani.

7“Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu anali ndi wantchito wolima kapena woweta nkhosa, kodi angawuze wantchitoyo atabwera ku munda kuti, ‘Tsopano bwera kuno khala pansi kuti udye?’ 8Kodi sangamuwuze kuti, ‘Konzere chakudya cha madzulo, iweyo ukonzeke ndipo undidikirire pamene ndikudya ndi kumwa; kenaka ukhoza kudya ndi kumwa?’ 9Kodi iye angathokoze wantchitoyo chifukwa chochita chimene anawuzidwa kuchita? 10Chimodzimodzi inunso, mukachita zonse zimene munawuzidwa, muzinena kuti, ‘Ndife antchito osayenera; tangogwira ntchito yathu basi.’ ”

Yesu Achiritsa Akhate Khumi

11Tsopano Yesu anayenda mʼmalire a pakati pa Samariya ndi Galileya pa ulendo wake wa ku Yerusalemu. 12Akulowa mʼmudzi wina, amuna khumi amene anali ndi khate anakumana naye. Iwo anayima patali 13ndipo anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Yesu, Ambuye, tichitireni chifundo!”

14Iye atawaona, anati, “Pitani kadzionetseni nokha kwa ansembe.” Ndipo pamene iwo ankapita, anachiritsidwa.

15Mmodzi wa iwo, ataona kuti wachiritsidwa, anabwerera, nayamika Mulungu ndi mawu okweza. 16Anagwetsa nkhope yake nagwa pa mapazi a Yesu ndi kumuthokoza. Ndipo iye anali Msamariya.

17Yesu anafunsa kuti, “Kodi amene anachiritsidwa sanalipo khumi? Nanga asanu ndi anayi ena ali kuti? 18Kodi palibe mmodzi mwa iwo amene anabwerera kudzalemekeza Mulungu kupatula mlendoyu?” 19Pamenepo anati kwa iye, “Imirira ndipo pita; chikhulupiriro chako chakuchiritsa iwe.”

Za Ufumu wa Mulungu

20Ndipo Afarisi atamufunsa Iye kuti, ufumu wa Mulungu udzabwera liti, Yesu anayankha kuti, “Mulungu sakhazikitsa ufumu wake mooneka ndi maso, 21kapenanso kuti anthu adzati, ‘Uwu uli apa,’ kapena ‘Uwo uli apo,’ Pakuti taonani ufumu wa Mulungu uli pakati panu.”

22Kenaka Iye anati kwa ophunzira ake, “Masiku akubwera pamene inu mudzalakalaka mutaona tsiku limodzi la masiku a Mwana wa Munthu, koma simudzaliona. 23Anthu adzakuwuzani kuti, ‘Uyo ali apoyo!’ kapena ‘Uyu ali apa!’ Musawathamangire iwo. 24Pakuti monga mphenzi ingʼanima ndi kuwala kuchokera mbali ina ya thambo kufikira inzake, koteronso adzakhala ali Mwana wa Munthu pa tsiku lake. 25Koma poyamba ayenera kuzunzika mu zambiri ndi kukanidwa ndi mʼbado uno.

26“Monga mmene zinkachitikira nthawi ya Nowa, momwemonso zidzachitikanso nthawi ya Mwana wa Munthu. 27Anthu ankadya, kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo. Pomwepo chigumula chinafika ndi kuwawononga onsewo.

28“Zinalinso chimodzimodzi nthawi ya Loti. Anthu ankadya ndi kumwa, kugula ndi kugulitsa, kudzala ndi kumanga. 29Koma tsiku limene Loti anachoka ku Sodomu, moto ndi sulufule zinavumbwa kuchokera kumwamba ndi kuwawononga onsewo.

30“Zidzakhalanso choncho Mwana wa Munthu akadzaonekera. 31Tsiku limenelo munthu amene ali pa denga la nyumba yake, ndi katundu wake ali mʼnyumbamo, asadzatsike kukatenga. Chimodzimodzinso, munthu amene adzakhale ali ku munda asadzabwerere kukatenga chilichonse. 32Kumbukirani mkazi wa Loti! 33Aliyense amene ayesetsa kusunga moyo wake adzawutaya, ndipo aliyense amene ataya moyo wake adzawusunga. 34Ine ndikukuwuzani inu, usiku umenewo anthu awiri adzagona pa mphasa imodzi; wina adzatengedwa ndipo wina adzasiyidwa. 35Amayi awiri adzakhala pamodzi akusinja; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa. 36Amuna awiri adzakhala akulima mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.”

37Iwo anafunsa kuti, “Ambuye, kodi zimenezi zidzachitikira kuti?”

Iye anayankha kuti, “Kumene kuli mtembo, nʼkumene makwangwala amasonkhanako.”