诗篇 94 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 94:1-23

第 94 篇

上帝是审判者

1耶和华啊,你是申冤的上帝;

申冤的上帝啊,

求你彰显你的荣光。

2审判世界的主啊,

求你起来使骄傲人受到应得的报应。

3耶和华啊,

恶人洋洋得意,要到何时呢?

要到何时呢?

4他们大放厥词,狂妄自大。

5耶和华啊,他们压迫你的子民,

苦害你的产业。

6他们谋害寡妇、外族人和孤儿,

7并说:“耶和华看不见,

雅各的上帝不会知道。”

8愚昧的人啊,你们要思想;

无知的人啊,你们何时才能明白呢?

9难道创造耳朵的上帝听不见吗?

难道创造眼睛的上帝看不见吗?

10管教列国的上帝难道不惩罚你们吗?

赐知识的上帝难道不知道吗?

11耶和华洞悉人的思想,

祂知道人的思想虚妄,

12耶和华啊,蒙你管教并用律法训诲的人有福了!

13你使他们在患难中有平安,

恶人终必灭亡。

14耶和华不会丢弃祂的子民,

也不会遗弃祂的产业。

15公正的审判必重现,

心地正直的人都必拥护。

16谁肯为我奋起攻击恶人?

谁肯为我起来抵挡作恶的人?

17耶和华若不帮助我,

我早已归入死亡的沉寂中了。

18我说:“我要倒下了!”

耶和华啊,你便以慈爱扶助我。

19当我忧心忡忡的时候,

你的抚慰带给我欢乐。

20借律例制造不幸的首领,

岂能与你联盟?

21他们结党攻击义人,

残害无辜。

22但耶和华是我的堡垒,

我的上帝是保护我的磐石。

23祂必使恶人自食恶果,

因他们的罪恶而毁灭他们。

我们的上帝耶和华必毁灭他们。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 94:1-23

Salimo 94

1Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango,

Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.

2Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi;

bwezerani kwa odzikuza zowayenera.

3Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova,

mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?

4Amakhuthula mawu onyada;

onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.

5Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova;

amapondereza cholowa chanu.

6Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko;

amapha ana amasiye.

7Iwo amati, “Yehova sakuona;

Mulungu wa Yakobo salabadirako.”

8Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu;

zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?

9Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva?

Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?

10Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga?

Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?

11Yehova amadziwa maganizo a munthu;

Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.

12Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza,

munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;

13mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto,

mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.

14Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake;

Iye sadzasiya cholowa chake.

15Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo,

ndipo onse olungama mtima adzachitsata.

16Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa?

Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?

17Yehova akanapanda kundithandiza,

bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.

18Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,”

chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.

19Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga,

chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.

20Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu

umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?

21Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama

ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.

22Koma Yehova wakhala linga langa,

ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.

23Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo

ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo;

Yehova Mulungu wathu adzawawononga.