诗篇 90 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 90:1-17

卷四:诗篇90—106

第 90 篇

上帝与世人

上帝的仆人摩西的祈祷。

1主啊,

你是我们世世代代的居所。

2群山尚未诞生,

大地和世界还未形成,

从亘古到永远,你是上帝。

3你叫人归回尘土,

说:“世人啊,归回尘土吧。”

4在你眼中,

千年如一日,又如夜里的一更。

5你像急流一般把世人冲走,

叫他们如梦消逝。

他们像清晨的嫩草,

6清晨还生机盎然,

傍晚就凋谢枯萎。

7你的怒气使我们灭亡,

你的愤怒使我们战抖。

8你知道我们的罪恶,

对我们隐秘的罪了如指掌。

9我们活在你的烈怒之下,

一生就像一声叹息飞逝而去。

10我们一生七十岁,

强壮的可活八十岁,

但人生最美好的时光也充满劳苦和愁烦,

生命转瞬即逝,

我们便如飞而去。

11谁明白你愤怒的威力?

有谁因为明白你的烈怒而对你心存敬畏呢?

12求你教导我们明白人生有限,

使我们做有智慧的人。

13耶和华啊,我还要苦候多久呢?

求你怜悯你的仆人。

14求你在清晨以慈爱来满足我们,

使我们一生欢喜歌唱。

15你使我们先前经历了多少苦难和不幸的岁月,

求你也赐给我们多少欢乐的岁月。

16求你让仆人们看见你的作为,

让我们的后代看见你的威荣。

17愿主——我们的上帝恩待我们,

使我们所做的亨通,

使我们所做的亨通。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 90:1-17

BUKU LACHINAYI

Masalimo 90–106

Salimo 90

Pemphero la Mose munthu wa Mulungu.

1Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo

pa mibado yonse.

2Mapiri asanabadwe,

musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse,

kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.

3Inu mumabwezera anthu ku fumbi,

mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”

4Pakuti zaka 1,000 pamaso panu

zili ngati tsiku limene lapita

kapena ngati kamphindi ka usiku.

5Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa,

iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,

6ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano,

pofika madzulo wauma ndi kufota.

7Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu;

ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.

8Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu,

machimo athu obisika poonekera pamaso panu.

9Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu;

timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.

10Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70,

kapena 80 ngati tili ndi mphamvu;

komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa,

zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.

11Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu?

Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.

12Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola,

kuti tikhale ndi mtima wanzeru.

13Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?

Achitireni chifundo atumiki anu.

14Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha,

kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.

15Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa,

kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.

16Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu,

kukongola kwanu kwa ana awo.

17Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife;

tikhazikitsireni ntchito ya manja athu;

inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.