诗篇 78 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 78:1-72

第 78 篇

上帝引导祂的子民

亚萨的训诲诗。

1我的百姓啊!

你们要听我的教导,

侧耳倾听我的话。

2我要开口讲比喻,

道出古时的奥秘,

3是我们所闻所知、世代流传下来的事。

4我们不要在子孙面前隐瞒事实,

要把耶和华当受称颂的作为、

祂的权能和所行的奇事告诉下一代。

5因为祂为雅各制定法度,

以色列设立律法,

又吩咐我们的祖先把这些律法传给儿女,

6好让他们也照样教导自己的子孙后代,

世代相传。

7这样,他们就会信靠上帝,

遵行祂的命令,

不忘记祂的作为;

8也不会像自己的祖先那样顽梗叛逆,

对上帝不忠,心怀二意。

9以法莲人备上了弓箭,

却临阵逃命。

10他们不遵守上帝的约,

拒绝遵行祂的律法。

11他们忘记了祂的作为,

忘记了祂为他们所行的奇事。

12祂曾在埃及,在琐安当着他们祖先的面行神迹。

13祂把海水分开,

带领他们安然渡过;

祂使海水堆起如墙壁。

14祂白天以云柱带领他们,

晚上用火柱引导他们。

15祂在旷野劈开磐石,

供应他们丰沛的水源。

16祂使水从磐石中滚滚流出,

如滔滔江河。

17然而,他们仍旧犯罪,

在旷野反叛至高的上帝。

18他们顽梗地试探上帝,

索要他们想吃的食物。

19他们抱怨上帝,说:

“难道上帝可以在旷野摆宴席吗?

20祂击打磐石,

水就涌出,流淌成河,

但祂能赐给我们——祂的子民食物和肉吗?”

21耶和华听后大怒,

祂的怒火烧向雅各

祂的怒气撒向以色列

22因为他们不相信上帝,也不信靠祂的拯救。

23祂向穹苍发出命令,

又打开天门,

24降下吗哪给他们吃,赐下天粮。

25他们吃了天使的食物,

上帝赐给他们丰富的食物。

26祂使空中刮起东风,

用大能引来南风,

27使飞鸟像雨点一般降在他们当中,多如尘埃,

使他们有多如海沙的肉吃。

28祂使飞鸟降落在他们营中的帐篷周围,

29让他们尽情地吃,

遂了他们的心愿。

30但是,他们还没有吃完,

肉还在口中的时候,

31上帝就向他们发怒,

杀掉了他们当中最强壮的,

消灭了以色列的青年。

32即使如此,

他们依旧犯罪,

不相信上帝奇妙的作为。

33所以上帝使他们虚度一生,

让他们的岁月充满恐惧。

34直到上帝击杀他们的时候,

他们才回转,诚心寻求上帝。

35他们才想起上帝是他们的磐石,

至高的上帝是他们的救赎主。

36他们却虚情假意,满口谎言。

37他们不忠于祂,

也不信守祂的约。

38但上帝充满怜悯,

赦免了他们的罪,

没有毁灭他们。

祂多次收住怒气,

没有完全发出祂的烈怒。

39祂顾念他们不过是血肉之躯,

像一阵风转眼消逝。

40他们在旷野屡屡反叛祂,

使祂伤心。

41他们再三试探上帝,

以色列的圣者发怒。

42他们忘记了祂的大能,

忘记了祂救他们脱离压迫的日子,

43也忘记了祂在埃及所行的神迹,

琐安的田野所行的奇事。

44祂曾使江河溪流变成血,

以致无人能喝。

45祂曾使成群的苍蝇吞没他们,

使青蛙毁灭他们。

46祂将他们的五谷赏给蚱蜢,

让蝗虫吃尽他们的收成。

47祂用冰雹毁坏他们的葡萄树,

用严霜毁坏他们的无花果树,

48又用冰雹毁灭他们的牛群,

用闪电毁灭他们的牲畜。

49祂把怒火、烈怒、愤恨和祸患倾倒在他们身上,

遣下一群降灾的天使。

50祂的怒气尽发,

使他们被瘟疫吞噬,难逃一死。

51祂击杀了埃及人所有的长子,

就是帐篷中头生的儿子。

52祂领出自己的子民,

好像领出羊群,

引领他们经过旷野,

53使他们一路平安,免受惊吓,

大海却淹没了他们的仇敌。

54祂带领自己的子民来到圣地的边界,

来到祂亲手为他们预备的山区,

55从他们面前赶出外族人,

把外族人的土地分给他们,

作为他们的产业,

使以色列各支派安顿下来。

56可是,他们仍旧试探上帝,

反叛至高者,不遵行祂的法度。

57他们跟祖先一样背信弃义,

像断弓一样毫不可靠。

58他们建造丘坛,惹祂发怒;

他们竖起神像,令祂愤怒。

59上帝知道了他们的恶行,

怒不可遏,

彻底弃绝了以色列人。

60祂离弃了设在示罗的圣幕,

就是祂在人间的居所。

61祂任凭自己的约柜被人掳去,

让自己的荣耀落在敌人手中。

62祂使自己的子民被刀剑杀戮,

向自己的产业大发怒气。

63青年被烈火吞噬,

少女无法婚嫁。

64祭司丧身刀下,

寡妇无法哭丧。

65那时,主像从睡眠中醒来,

又如酒后醒来的勇士。

66祂击退仇敌,

叫他们永远蒙羞。

67祂丢弃了约瑟的子孙,

没有拣选以法莲支派。

68祂拣选了犹大支派,

祂所喜爱的锡安山。

69祂为自己建造高耸的圣所,

使它像大地一样长存。

70祂拣选了祂的仆人大卫

把他从羊圈中召来,

71让他离开牧羊的生活,

去牧养祂的子民雅各的后裔,

牧养祂的产业以色列

72于是,大卫以正直的心牧养他们,

用灵巧的手带领他们。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 78:1-72

Salimo 78

Ndakatulo ya Asafu.

1Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa;

mvetserani mawu a pakamwa panga.

2Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo,

ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale

3zimene tinazimva ndi kuzidziwa,

zimene makolo athu anatiwuza.

4Sitidzabisira ana awo,

tidzafotokozera mʼbado wotsatira

ntchito zotamandika za Yehova,

mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.

5Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo

ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli,

zimene analamulira makolo athu

kuphunzitsa ana awo,

6kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa,

ngakhale ana amene sanabadwe,

ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.

7Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu

ndipo sadzayiwala ntchito zake

koma adzasunga malamulo ake.

8Iwo asadzakhale monga makolo awo,

mʼbado wosamvera ndi wowukira,

umene mitima yake inali yosamvera Mulungu,

umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.

9Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta,

anathawabe pa nthawi ya nkhondo;

10iwo sanasunge pangano la Mulungu

ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.

11Anayiwala zimene Iye anachita,

zozizwitsa zimene anawaonetsa.

12Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona,

mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.

13Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo,

Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.

14Anawatsogolera ndi mtambo masana

ndi kuwala kwa moto usiku wonse.

15Iye anangʼamba miyala mʼchipululu

ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;

16Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala

ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.

17Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye,

kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.

18Ananyoza Mulungu mwadala

pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.

19Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti,

“Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?

20Iye atamenya thanthwe

madzi anatuluka,

ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi.

Koma iye angatipatsenso ife chakudya?

Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”

21Yehova atawamva anakwiya kwambiri;

moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo,

ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,

22pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu

kapena kudalira chipulumutso chake.

23Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba

ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;

24anagwetsa mana kuti anthu adye,

anawapatsa tirigu wakumwamba.

25Anthu anadya buledi wa angelo,

Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.

26Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba,

ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.

27Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi,

mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.

28Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo,

kuzungulira matenti awo onse.

29Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka

pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.

30Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho,

chakudya chili mʼkamwa mwawobe,

31mkwiyo wa Mulungu unawayakira;

Iye anapha amphamvu onse pakati pawo,

kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.

32Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa;

ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.

33Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya.

Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.

34Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo;

iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.

35Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo,

kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.

36Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo,

kumunamiza ndi malilime awo;

37Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye,

iwo sanakhulupirike ku pangano lake.

38Komabe Iye anali wachifundo;

anakhululukira mphulupulu zawo

ndipo sanawawononge.

Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake

ndipo sanawutse ukali wake wonse.

39Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe,

mphepo yopita imene sibwereranso.

40Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu

ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!

41Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu;

ankamuputa Woyera wa Israeli.

42Sanakumbukire mphamvu zake,

tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,

43tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto,

zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.

44Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi;

Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.

45Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga,

ndiponso achule amene anawasakaza.

46Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala,

zokolola zawo kwa dzombe.

47Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala

ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.

48Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala,

zoweta zawo ku zingʼaningʼani.

49Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo,

anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso.

Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.

50Analolera kukwiya,

sanawapulumutse ku imfa

koma anawapereka ku mliri.

51Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto,

zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu

52Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto;

anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.

53Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha

koma nyanja inamiza adani awo.

54Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera,

ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.

55Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo

ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo;

Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.

56Koma iwo anayesa Mulungu

ndi kuwukira Wammwambamwamba;

sanasunge malamulo ake.

57Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo,

anapotoka monga uta wosakhulupirika.

58Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano;

anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.

59Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri;

Iye anakana Israeli kwathunthu.

60Anasiya nyumba ya ku Silo,

tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.

61Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo,

ulemerero wake mʼmanja mwa adani.

62Anapereka anthu ake ku lupanga;

anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.

63Moto unanyeketsa anyamata awo,

ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;

64ansembe awo anaphedwa ndi lupanga,

ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.

65Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo,

ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.

66Iye anathamangitsa adani ake;

anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.

67Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe,

sanasankhe fuko la Efereimu;

68Koma anasankha fuko la Yuda,

phiri la Ziyoni limene analikonda.

69Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda,

dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.

70Anasankha Davide mtumiki wake

ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;

71kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa

kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo,

wa Israeli cholowa chake.

72Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama;

ndi manja aluso anawatsogolera.