第 45 篇
婚礼诗歌
可拉后裔作的训诲诗,也是婚礼上唱的情歌,交给乐长,调用“百合花”。
1我心中涌出美丽的诗章,
我要把它献给王,
我的舌头是诗人手上的妙笔。
2你俊美无比,口出恩言,
因此上帝永远赐福给你。
3伟大的王啊,
佩上你的宝剑,
你是何等尊贵、威严!
4你威严无比,所向披靡,
捍卫真理和正义,
保护卑微的人。
愿你的右手彰显可畏的作为!
5你的利箭刺穿敌人的心窝,
列国臣服在你脚下。
6上帝啊,你的宝座永远长存,
你以公义的杖执掌王权。
7你喜爱公义,憎恶邪恶,
因此上帝,你的上帝,
用喜乐之油膏你,
使你超过同伴。
8你的衣袍散发出没药、沉香和肉桂的芬芳,
你陶醉在象牙宫的弦乐中。
9众公主在你的贵客中,
戴俄斐金饰的王后站在你右边。
10女子啊,
要侧耳倾听:不要再挂念家乡的父老,
11王喜欢你的美貌,
你要敬重他,因他是你的主。
12泰尔人必来送礼,
富人必来取悦你。
13公主身穿金线衣,无比华贵。
14她身披锦绣,
由侍女伴随前来见王,
15她们欢喜快乐地进入王宫。
16你的子孙将来要继承祖先的王位,
你要立他们在各地做王。
17我要使你的名世代受尊崇,
万民必永远称谢你。
Salimo 45
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati.
1Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma
pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu;
lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
2Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse
ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika,
popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
3Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu;
mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
4Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso
mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo;
dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
5Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu,
mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
6Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi;
ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
7Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;
choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu
pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
8Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya;
kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu
nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
9Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka;
ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
10Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu;
iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako;
mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso,
amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
13Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake,
chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu;
anamwali okhala naye akumutsatira
ndipo abweretsedwa kwa inu.
15Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo;
akulowa mʼnyumba yaufumu.
16Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako;
udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse;
choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.