诗篇 40 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 40:1-17

第 40 篇

赞美上帝之歌

大卫的诗,交给乐长。

1我曾耐心等候耶和华,

祂倾听了我的呼求。

2祂把我从绝望的深渊拉出来,

救我脱离泥泞沼泽,

把我安置在磐石上,

使我步履稳健。

3祂赐给我一首新歌,

一首赞美我们上帝的诗歌。

许多人看见便敬畏、信靠耶和华。

4信靠耶和华的人有福了!

他们不随从骄傲自大、信靠假神的人。

5我的上帝耶和华啊,

你行了许多奇事,

为我们定了许多美好的计划,

谁能与你相比!

你奇妙的作为不可胜数。

6祭物和供品非你所悦,

你开通了我的耳朵,

燔祭和赎罪祭非你所要。

7于是我说:

“看啊,我来了,

正如经卷上有关我的记载。

8我的上帝啊,

我乐意遵行你的旨意,

我铭记你的律法。”

9耶和华啊,你知道我在大会中宣扬你的公义,

没有闭口不言。

10我述说你的信实和拯救之恩,

没有把你的公义隐而不宣,

没有在大会中避而不谈你的慈爱和真理。

11耶和华啊,

求你不要收回你的怜悯,

愿你的慈爱和真理时刻守护我!

12我患难重重,罪恶缠身,

看不到出路。

我的罪过比我的头发还多,

我心惊胆战。

13耶和华啊,求你拯救我!

耶和华啊,求你快来帮助我!

14愿谋取我性命的人蒙羞受辱!

愿喜欢我被害的人狼狈逃窜!

15愿那些哈哈嘲笑我的人羞愧难当!

16愿所有寻求你的人因你而欢喜快乐!

愿渴望蒙你拯救的人时常说:

“耶和华当受尊崇!”

17我贫穷困苦,

但主眷顾我。

我的上帝啊,

你是我的帮助、我的拯救,

求你不要迟延!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 40:1-17

Salimo 40

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mofatsa ndinadikira Yehova

Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.

2Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko,

mʼthope ndi mʼchithaphwi;

Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe

ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.

3Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga,

nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga.

Ambiri adzaona,

nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.

4Ndi wodala munthu

amakhulupirira Yehova;

amene sayembekezera kwa odzikuza,

kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.

5Zambiri, Yehova Mulungu wanga,

ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita.

Zinthu zimene munazikonzera ife

palibe amene angathe kukuwerengerani.

Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera,

zidzakhala zambiri kuzifotokoza.

6Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna,

koma makutu anga mwawatsekula;

zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo

Inu simunazipemphe.

7Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera.

Mʼbuku mwalembedwa za ine.

8Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga;

lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”

9Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu;

sinditseka milomo yanga

monga mukudziwa Inu Yehova.

10Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga;

ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu.

Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu

pa msonkhano waukulu.

11Musandichotsere chifundo chanu Yehova;

chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.

12Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira;

machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona.

Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga,

ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.

13Pulumutseni Yehova;

Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.

14Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga

achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;

onse amene amakhumba chiwonongeko changa

abwezedwe mwamanyazi.

15Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!”

abwerere akuchita manyazi.

16Koma iwo amene amafunafuna Inu

akondwere ndi kusangalala mwa Inu;

iwo amene amakonda chipulumutso chanu

nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”

17Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa;

Ambuye andiganizire.

Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga;

Inu Mulungu wanga, musachedwe.