诗篇 35 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 35:1-28

第 35 篇

求上帝申冤

大卫的诗。

1耶和华啊,

求你与我的敌人为敌,

攻击那些攻击我的人。

2求你拿起大小盾牌来帮助我,

3举起矛枪攻击追赶我的人。

求你对我说:

“我是你的拯救。”

4愿谋杀我的人蒙羞受辱,

谋害我的人落荒而逃!

5愿耶和华的天使驱散他们,

如风吹散糠秕!

6愿他们的道路漆黑泥泞,

有耶和华的天使在后追赶!

7因为他们无故设网罗,

挖陷阱要害我。

8愿他们突遭祸患,

作茧自缚,自食恶果!

9我要因耶和华而欢欣,

因祂的拯救而快乐。

10我从心底发出赞叹:

耶和华啊,谁能像你?

你拯救弱者免受欺压,

拯救穷人免遭掠夺。

11恶人诬告我,

盘问我毫无所知的事情。

12他们对我以恶报善,

令我伤心欲绝。

13他们生病时,

我披上麻衣,

谦卑地为他们禁食祷告,

但上帝没有垂听。

14我为他们哀伤,

视他们为朋友、弟兄;

我低头为他们哭泣,

如同哀悼自己的母亲。

15我遭遇患难时,

他们却聚在一起幸灾乐祸,

合伙诽谤我。

素不相识的人也群起攻击我,

不住地毁谤我。

16他们肆无忌惮地嘲弄我,

咬牙切齿地憎恶我。

17耶和华啊,

你袖手旁观要到何时?

求你救我的性命免遭残害,

救我脱离这些狮子。

18我要在大会中称谢你,

在众人面前赞美你。

19求你不要让无故攻击我的人幸灾乐祸,

不要让无故恨我的人沾沾自喜。

20他们言语暴戾,

谋害安分守己的人。

21他们高喊:“哈哈!哈哈!

我们亲眼看见了。”

22耶和华啊,这一切你都看见了,

求你不要再缄默,不要远离我。

23我的上帝,我的主啊,

求你起来为我辩护,为我申冤。

24我的上帝耶和华啊,

求你按你的公义宣告我无罪,

别让他们幸灾乐祸。

25别让他们说:

“哈哈,我们如愿以偿了!”

别让他们说:

“我们除掉他了!”

26愿幸灾乐祸的人蒙羞受辱,

自高自大的人无地自容!

27愿盼望我冤屈得雪的人扬声欢呼!

愿他们常说:“耶和华当受尊崇!

祂乐意赐福给自己的仆人。”

28我要诉说你的公义,

终日赞美你。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 35:1-28

Salimo 35

Salimo la Davide.

1Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane;

mumenyane nawo amene akumenyana nane.

2Tengani chishango ndi lihawo;

dzukani ndipo bwerani mundithandize.

3Tengani mkondo ndi nthungo,

kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa.

Uzani moyo wanga kuti,

“Ine ndine chipulumutso chako.”

4Iwo amene akufunafuna moyo wanga

anyozedwe ndi kuchita manyazi;

iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke

abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.

5Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo

pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.

6Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera

pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.

7Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa

ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,

8chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa

ukonde umene iwo abisa uwakole,

agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.

9Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova

ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.

10Thupi langa lidzafuwula mokondwera,

“Ndani angafanane nanu Yehova?

Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri,

osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”

11Mboni zopanda chisoni zinayimirira,

zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.

12Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino

ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.

13Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli

ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya.

Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,

14ndinayendayenda ndi kulira maliro,

kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga.

Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima

kukhala ngati ndikulira amayi anga.

15Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala;

ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa.

Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.

16Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe;

anandikukutira mano awo.

17Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana?

Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo,

moyo wanga wopambana ku mikango.

18Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu;

pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.

19Musalole adani anga onyenga

akondwere chifukwa cha masautso anga;

musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa

andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.

20Iwowo sayankhula mwamtendere,

koma amaganizira zonamizira

iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.

21Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa!

Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”

22Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete.

Ambuye musakhale kutali ndi ine.

23Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza!

Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.

24Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga.

Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.

25Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!”

Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”

26Onse amene amakondwera ndi masautso anga

achite manyazi ndi kusokonezeka.

Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana,

avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.

27Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa,

afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo.

Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke,

Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”

28Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu

ndi za matamando anu tsiku lonse.