诗篇 116 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 116:1-19

第 116 篇

感谢拯救之恩

1我爱耶和华,

因为祂垂听了我的呼求和祷告。

2因为祂垂听我的祈求,

我一生都要向祂祷告。

3死亡的绳索缠绕我,

阴间的恐怖笼罩我,

我被困苦和忧愁淹没。

4于是,我求告耶和华,

说:“耶和华啊,求你拯救我。”

5耶和华仁慈、公义,

我们的上帝充满怜悯。

6耶和华保护心地单纯的人,

危难之时祂救了我。

7我的心啊,再次安宁吧,

因为耶和华恩待你。

8祂救我的性命脱离死亡,

止住我眼中的泪水,

使我双脚免于滑倒。

9我要在世上事奉耶和华。

10我相信,所以才说:

“我受尽了痛苦。”

11我曾惊恐地说:

“人人都说谎。”

12我拿什么报答耶和华赐给我的一切恩惠呢?

13我要为耶和华的拯救之恩而举杯称颂祂的名。

14我要在耶和华的子民面前还我向祂许的愿。

15耶和华的眼目顾惜祂圣民的死亡。

16耶和华啊!我是你的仆人,

是你的仆人,是你婢女的儿子。

你除去了我的锁链。

17我要向你献上感恩祭,

呼求你的名。

18-19我要在耶路撒冷

在耶和华的殿中,

在耶和华的子民面前还我向祂许的愿。

你们要赞美耶和华!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 116:1-19

Salimo 116

1Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga;

Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.

2Pakuti ananditchera khutu,

ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.

3Zingwe za imfa zinandizinga,

zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera;

ndinapeza mavuto ndi chisoni.

4Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova:

“Inu Yehova, pulumutseni!”

5Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama

Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.

6Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima;

pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.

7Pumula iwe moyo wanga,

pakuti Yehova wakuchitira zokoma.

8Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa,

maso anga ku misozi,

mapazi anga kuti angapunthwe,

9kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova

mʼdziko la anthu amoyo.

10Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati,

“Ndasautsidwa kwambiri.”

11Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati,

“Anthu onse ndi abodza.”

12Ndingamubwezere chiyani Yehova,

chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?

13Ndidzakweza chikho cha chipulumutso

ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.

14Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova

pamaso pa anthu ake onse.

15Imfa ya anthu oyera mtima

ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.

16Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu:

ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu;

Inu mwamasula maunyolo anga.

17Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu

ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.

18Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova

pamaso pa anthu ake onse,

19mʼmabwalo a nyumba ya Yehova,

mʼkati mwako iwe Yerusalemu.

Tamandani Yehova.