耶利米书 35 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 35:1-19

顺服的利甲族和悖逆的犹大人

1犹大约西亚的儿子约雅敬执政期间,耶和华对耶利米说: 2“你去利甲族那里,邀请他们到耶和华殿的一间厢房,给他们酒喝。” 3于是,我将哈巴洗尼雅的孙子、雅利米雅的儿子雅撒尼亚,以及雅撒尼亚的弟兄和儿子等利甲全族的人, 4领到耶和华的殿,进入上帝的仆人伊基大利之子哈难众儿子的房间。这房间靠近官长的房间,在殿门守卫沙龙的儿子玛西雅的房间上面。 5我把盛满酒的杯和壶摆在利甲全族面前,请他们喝酒。 6他们却说:“我们不喝酒,因为我们的祖先利甲的儿子约拿达曾吩咐我们和我们的子孙永远不可喝酒、 7盖房、撒种、栽植葡萄或拥有葡萄园,一辈子都要住帐篷,以便在异乡长久居住。 8我们遵守他的一切吩咐,我们和我们的妻子儿女从不喝酒, 9不盖房,也没有葡萄园、田地和种子。 10我们住帐篷,遵守我们祖先约拿达的一切吩咐。 11但当巴比伦尼布甲尼撒进攻这里的时候,我们决定来耶路撒冷躲避迦勒底亚兰的军队。因此,我们现在住在耶路撒冷。”

12耶和华对耶利米说: 13“这是以色列的上帝——万军之耶和华的话,你去把我的话告诉犹大人和耶路撒冷的居民,‘耶和华说,你们要听从我的教导。 14利甲的儿子约拿达吩咐他的子孙不可喝酒,他们直到现在都不喝酒。但我屡次告诫你们,你们却不听我的话。 15我再三差遣我的仆人——众先知劝你们改邪归正,不要追随、祭拜别的神明,以便你们可以在我赐给你们和你们祖先的土地上安居乐业,你们却充耳不闻,毫不理会。 16利甲的儿子约拿达的子孙尚且听从他们祖先的吩咐,你们却不听从我的话。 17因此,以色列的上帝——万军之耶和华说,我要给犹大耶路撒冷的居民降下我说过的灾祸。因为我对他们说话,他们不听;我呼唤他们,他们不理会。’”

18然后,耶利米利甲族人说:“以色列的上帝——万军之耶和华说,‘你们听从祖先利甲的儿子约拿达的吩咐,遵守他的一切命令, 19因此,利甲的儿子约拿达的子孙必永远事奉我。这是以色列的上帝——万军之耶和华说的。’”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 35:1-19

Arekabu

1Yehova anayankhula ndi Yeremiya nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, kuti: 2“Pita ku banja la Arekabu ndipo ukawayitane kuti abwere mʼchipinda chimodzi cha Nyumba ya Yehova ndipo akafika uwapatse vinyo kuti amwe.”

3Choncho ndinakatenga Yaazaniya (mwana wa Yeremiya winanso amene anali mwana wa Habaziniya), abale ake, ana ake onse aamuna ndi banja lonse la Arekabu. 4Ndinabwera nawo ku Nyumba ya Yehova, ku chipinda cha ophunzira a mneneri Hanani mwana wa Igidaliya, munthu wa Mulungu. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda cha akuluakulu, chimene chinali pamwamba pa chipinda cha Maaseya mwana wa Salumu, mlonda wa pa khomo. 5Kenaka ndinayika mabotolo odzaza ndi vinyo ndi zikho zake pamaso pa Arekabu ndipo ndinawawuza kuti, “Imwani vinyoyu.”

6Koma iwo anayankha kuti, “Ife sitimwa vinyo, chifukwa kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula kuti, ‘Inuyo ngakhale zidzukulu zanu, musadzamwe vinyo mpaka kalekale. 7Musadzamange nyumba kapena kufesa mbewu, kapena kulima minda ya mpesa; musadzakhale ndi zinthu zimenezi. Mʼmalo mwake muzidzakhale mʼmatenti. Mukadzatero mudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukukhalamo.’ 8Ife takhala tikumvera zonse zimene kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula. Ife ngakhale akazi athu kapena ana athu aamuna ndi aakazi sitinamwepo vinyo 9kapena kumanga nyumba kuti tizikhalamo kapenanso kukhala ndi minda ya mpesa, minda ina iliyonse kapena mbewu. 10Koma takhala mʼmatenti ndipo tamvera kwathunthu chilichonse chimene kholo lathu Yehonadabu anatilamula. 11Koma pamene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anathira nkhondo dziko lino, ife tinati, ‘Tiyeni tichoke, tipite ku Yerusalemu kuti tithawe magulu ankhondo a Akasidi ndi Aaramu.’ Kotero ife takhala tikukhala mu Yerusalemu.”

12Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya kuti, 13“Iyeyu, Yehova Mulungu wa Israeli anawuza Yeremiya kuti: Pita ukawawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Kodi simungatengeko phunziro ndi kumvera mawu anga?’ akutero Yehova. 14‘Yehonadabu mwana wa Rekabu analamula ana ake kuti asamwe vinyo ndipo lamulo limeneli alisunga. Mpaka lero lino iwo samwa vinyo, chifukwa akumvera lamulo la kholo lawo. Koma Ine ndakhala ndikuyankhula nanu kawirikawiri kukuchenjezani, koma inu simunandimvere Ine. 15Kawirikawiri ndakhala ndikutumiza atumiki anga, aneneri, kwa inu. Iwo akhala akukuwuzani kuti, ‘Aliyense wa inu asiye ntchito zake zoyipa ndi kukonza makhalidwe ake; musatsatire milungu ina ndi kumayitumikira. Pamenepo mudzakhala mʼdziko limene ndinakupatsani ndi makolo anu.’ Komabe inu simunasamale zimenezi kapena kundimvera Ine. 16Zidzukulu za Yehonadabu mwana wa Rekabu zakhala zikumvera lamulo limene kholo lawo anazilamula, koma inuyo simunandimvere Ine.

17“Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndidzagwetsera pa Yuda ndi pa onse okhala mu Yerusalemu masautso onse amene ndinakonza chifukwa sanandimvere. Ndinawayitana koma iwo sanayankhe.’ ”

18Yeremiya anawuza banja la Arekabu mawu onse a Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, kuti, “Munamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu ndipo mwatsatira malangizo ake onse ndi kuchita chilichonse chimene anakulamulani.” 19Tsono Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Yehonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wonditumikira Ine nthawi zonse.”