约翰福音 19 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约翰福音 19:1-42

1于是彼拉多命人鞭打耶稣。 2士兵用荆棘编成冠冕戴在祂头上,又拿紫袍给祂穿上, 3来到祂面前说:“犹太人的王万岁!”然后又用手掌打祂。

4彼拉多又走到外面对众人说:“我把祂带到你们面前,好让你们知道我查不出祂有什么罪。” 5于是,耶稣戴着荆棘冠冕、穿着紫色长袍出来。彼拉多对众人说:“你们看这个人!”

6祭司长和差役一见耶稣,就喊道:“把祂钉在十字架上!把祂钉在十字架上!”

彼拉多说:“你们自己把祂带去钉十字架吧!因为我查不出祂有什么罪。”

7犹太人回答说:“我们有律法,按照那律法,祂应当被处死,因为祂自称是上帝的儿子。”

8彼拉多听了这话,更加害怕, 9连忙将耶稣带回总督府,问祂:“你到底是从哪里来的?”但耶稣没有回答。

10彼拉多说:“你不回答我吗?难道你不知道我有权释放你,也有权把你钉在十字架上吗?”

11耶稣回答说:“除非从上面赐下权柄给你,否则你无权处置我。因此,把我交给你的那人罪更大。”

12从那时起,彼拉多想要释放耶稣,可是犹太人却一直喊叫:“如果你释放这个人,你就不是凯撒的忠臣19:12 忠臣”希腊文是“朋友”。。凡自以为王的,就是背叛凯撒。”

13彼拉多听了这话,就带着耶稣来到一个地方,名叫“铺石地”,那地方希伯来话叫厄巴大彼拉多在那里开庭审判祂。 14那天正是逾越节的预备日,大约在中午十二时,彼拉多犹太人说:“看啊!你们的王。”

15众人喊道:“除掉祂!除掉祂!把祂钉在十字架上!”

彼拉多说:“我可以把你们的王钉在十字架上吗?”

祭司长答道:“除了凯撒,我们没有别的王!”

16于是,彼拉多将耶稣交给他们去钉十字架,他们就把耶稣带走了。

钉十字架

17耶稣背着自己的十字架出来,前往髑髅地19:17 可能当地的石灰岩地形看起来像一具骷髅头,故此得名。,那地方希伯来话叫各各他18他们在那里把耶稣钉在十字架上。同时还钉了两个人,一边一个,耶稣在当中。 19彼拉多写了一个告示,安在十字架上,上面写着“犹太人的王,拿撒勒人耶稣”。 20因为耶稣被钉十字架的地方离城不远,告示上面的字是用希伯来罗马希腊三种文字写的,所以很多犹太人读了上面的字。

21犹太人的祭司长对彼拉多说:“不要写‘犹太人的王’,应该写‘这人自称是犹太人的王’。”

22彼拉多说:“我写了就写了。”

23士兵把耶稣钉在十字架上,又把祂的衣服分成四份,每人一份。剩下的内衣从上到下是一块布,没有缝口。 24他们就商量说:“不要撕破它,让我们抽签决定给谁吧。”这件事是要应验圣经上的话:“他们分了我的外衣,又为我的内衣抽签。”士兵果然这样做了。

25耶稣的十字架旁边站着祂母亲、祂母亲的一个姊妹、革罗罢的妻子玛丽亚抹大拉玛丽亚26耶稣看见祂的母亲和祂所爱的门徒都站在旁边,就对母亲说:“妇人,看啊,他是你的儿子。” 27然后对门徒说:“看啊,她是你的母亲。”从那天起,那个门徒就把她接到自己家里去了。

耶稣之死

28后来,耶稣知道一切的事已经完成,就说:“我渴了。”这是要应验圣经上的话。 29那里有一个器皿盛满了醋酒。有人用海绵蘸满了醋酒绑在牛膝草上送到祂的嘴里, 30耶稣尝了那醋酒,然后说:“成了!”就垂下头来,将灵魂交给了上帝。

31因为那天是预备日,第二天的安息日是个大日子,为了避免在安息日有尸首留在十字架上,犹太人便求彼拉多叫人打断他们的腿,好把他们搬走。 32于是,士兵上前把与耶稣同钉十字架的两个人的腿都打断了。 33但是他们来到耶稣那里时,发现祂已经死了,就没有打断祂的腿, 34只是有一个士兵用矛刺了一下祂的肋旁,顿时有血和水流了出来。 35看见这事的人为此做见证,他的见证是真实的,他知道自己所说的是事实,好让你们可以相信。 36这些事的发生是为了应验圣经上的话:“祂的骨头一根也不会折断”; 37“他们要仰望自己所刺的那位。”

安葬耶稣

38事后,有一个名叫约瑟亚利马太人请求彼拉多让他为耶稣收尸。他因为畏惧犹太人,只是暗中做耶稣的门徒。彼拉多批准了,他就把耶稣的遗体领去。 39曾经夜访耶稣的尼哥德慕也来了,他带来了没药和沉香调成的香料,重约三十四公斤。 40他们按照犹太人殡葬的习俗,用细麻布加上香料把耶稣的遗体裹好。 41在耶稣被钉十字架的地方有一个园子,里边有一座新坟墓,从来没有安葬过人。 42因为那天是犹太人的预备日,这座新坟墓也在附近,他们就把耶稣安放在那里。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 19:1-42

Yesu Aweruzidwa kuti Aphedwe

1Kenaka Pilato anatenga Yesu namukwapula mwankhanza. 2Asilikali analuka nkhata yaminga ndi kumuveka pamutu pake. Kenaka anamuveka mkanjo wapepo 3ndipo ankapita kwa Iye mobwerezabwereza ndi kumanena kuti, “Moni mfumu ya Ayuda?” Ndipo amamumenya makofi.

4Pilato anatulukanso ndipo anati kwa Ayuda, “Taonani, ine ndikumubweretsa kuti inu mudziwe kuti ine sindikupeza chifukwa chomuyimbira mlandu.” 5Pamenepo Yesu anatuluka atavala nkhata yaminga ndi mkanjo wapepo ndipo Pilato anawawuza kuti, “Nayu munthu uja!”

6Atangomuona Iye akulu a ansembe ndi akuluakulu ena anafuwula kuti, “Mpachikeni! Mpachikeni!”

Koma Pilato anayankha kuti, “Inu mutengeni ndi kumupachika. Koma ine sindikupeza chifukwa chomuyimbira mlandu.”

7Ayuda anayimirira nati, “Ife tili ndi lamulo, ndipo molingana ndi lamulolo, Iyeyu ayenera kuphedwa chifukwa akudzitcha kuti ndi Mwana wa Mulungu.”

8Pilato atamva zimenezi, anachita mantha kwambiri, 9ndipo anabwereranso mʼnyumba yaufumu. Iye anafunsa Yesu kuti, “Kodi umachokera kuti?” Koma Yesu sanayankhe. 10Pilato anati, “Kodi ukukana kundiyankhula ine? Kodi sukuzindikira kuti ine ndili ndi mphamvu yokumasula ndiponso mphamvu yokupachika?”

11Yesu anayankha kuti, “Inu simukanakhala ndi mphamvu pa Ine akanapanda kukupatsani kumwamba. Nʼchifukwa chake amene wandipereka Ine kwa inu ndiye wochimwa kwambiri.”

12Kuyambira pamenepo Pilato anayesa kuti amumasule Yesu, koma Ayuda anapitirira kufuwula kuti, “Ngati mumumasula munthuyu kuti apite, inu si bwenzi la Kaisara.”

13Pilato atamva zimenezi, iye anamutulutsa Yesu kunja ndi kukhala pansi pa mpando wa woweruza pamalo otchedwa Mwala Wowaka (umene pa Chiaramaiki ndi Gabata). 14Linali tsiku lokonzekera Sabata la Paska ndipo nthawi inali ora lachisanu ndi chimodzi masana.

Pilato anati kwa Ayuda, “Nayi mfumu yanu.”

15Koma iwo anafuwula kuti, “Choka nayeni! Choka nayeni! Mpachikeni!”

Pilato anafunsa kuti, “Kodi ine ndipachike mfumu yanuyi?”

Akulu a ansembe anayankha kuti, “Ife tilibe mfumu ina koma Kaisara.”

16Pomaliza Pilato anamupereka kwa iwo kuti akapachikidwe. Choncho asilikali anamutenga Yesu.

Kupachikidwa kwa Yesu

17Atanyamula mtanda wake, anapita kumalo otchedwa “Malo a Bade” (mʼChiaramaiki amatchedwa Gologota). 18Pamenepo iwo anamupachika Iye pamodzi ndi anthu ena awiri, mmodzi mbali ina ndi wina mbali inanso ndipo Yesu pakati.

19Pilato analemba chikwangwani chomwe anachikhoma pa mtandapo. Panalembedwa mawu akuti, yesu wa ku nazareti, mfumu ya ayuda. 20Ayuda ambiri anawerenga chikwangwanichi, pakuti pamalo pamene Yesu anapachikidwapo panali pafupi ndi mzinda ndipo chikwangwanicho chinalembedwa mu Chiaramaiki, Chilatini ndi Chigriki. 21Kenaka mkulu wa ansembe wa Ayuda anakadandaula kwa Pilato nati, “Musalembe kuti ‘Mfumu ya Ayuda,’ koma kuti munthuyu amadzitcha kuti ndi mfumu ya Ayuda.”

22Pilato anayankha kuti, “Chimene ine ndalemba, ndalemba.”

23Asilikali atamupachika Yesu, anatenga zovala zake ndi kuzigawa zigawo zinayi, gawo limodzi la aliyense wa iwo, ndi kutsala mwinjiro wamʼkati wokha. Chovala ichi chinawombedwa kuyambira pamwamba mpaka pansi wopanda msoko.

24Iwo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni tisachingʼambe koma tichite maere kuti tione amene achitenge.”

Izi zinachitika kuti malemba akwaniritsidwe amene anati,

“Iwo anagawana zovala zanga pakati pawo

ndi kuchita maere pa zovala zangazo.”

Choncho izi ndi zimene asilikali anachita.

25Pafupi ndi mtanda wa Yesu panayima amayi ake, mngʼono wa amayi ake, Mariya mkazi wa Kaliyopa ndi Mariya wa ku Magadala. 26Yesu ataona amayi ake pamenepo ndi wophunzira amene Iye anamukonda atayima pafupipo, Iye anati kwa amayi ake, “Amayi nayu mwana wanu.” 27Anawuzanso wophunzirayo kuti, “Nawa amayi ako.” Kuyambira nthawi imeneyo, wophunzirayo anatenga amayiwo kupita nawo kwawo.

Imfa ya Yesu

28Atadziwa kuti zonse zatha tsopano komanso kuti malemba akwaniritsidwe, Yesu anati, “Ine ndili ndi ludzu.” 29Pomwepo panali mtsuko wodzaza ndi vinyo wosasa, choncho iwo ananyika chinkhupule ndi kuchisomeka ku mtengo wa hisope nachifikitsa kukamwa kwa Yesu. 30Yesu atalandira chakumwachi anati, “Kwatha.” Ndipo Iye anaweramitsa mutu wake napereka mzimu wake.

31Popeza linali Tsiku Lokonzekera ndipo tsiku linalo linali Sabata lapadera; Ayuda sanafune kuti mitembo ikhale pa mtanda pa Sabata, iwo anapempha Pilato kuti akathyole miyendo ndi kutsitsa mitemboyo. 32Chifukwa chake asilikali anabwera ndi kuthyola miyendo ya munthu oyamba amene anapachikidwa ndi Yesu ndipo kenaka ya winayo. 33Koma atafika pa Yesu ndi kupeza kuti anali atamwalira kale, iwo sanathyole miyendo yake. 34Mʼmalo mwake, mmodzi wa asilikaliwo anamubaya Yesu ndi mkondo mʼnthiti, ndipo nthawi yomweyo munatuluka magazi ndi madzi. 35Munthu amene anaona izi wapereka umboni ndipo umboni wake ndi woona. Iye akudziwa kuti akunena choonadi kuti inunso mukhulupirire. 36Zinthu izi zinachitika kuti malemba akwaniritsidwe: “Palibe limodzi la mafupa limene lidzathyoledwa,” 37ndi monga lemba linanso linena, “Iwo adzayangʼana Iye amene iwo anamubaya.”

Yesu Ayikidwa Mʼmanda

38Kenaka, Yosefe wa ku Arimateyu anakapempha mtembo wa Yesu kwa Pilato. Tsono Yosefe anali wophunzira wa Yesu koma mobisa chifukwa iye ankaopa Ayuda. Atalandira chilolezo kwa Pilato, anakatsitsa mtembo wa Yesu. 39Nekodimo, munthu amene poyamba pake anabwera kwa Yesu usiku, anatenga mafuta osakaniza ndi mure ndi aloe wolemera pafupifupi makilogalamu 32. 40Pamenepo anatenga mtembo wa Yesu nawukulunga pamodzi ndi zonunkhiritsa mu nsalu za mtundu woyera monga mwa mwambo wa maliro wa Ayuda. 41Pamalo pamene anapachikidwa Yesu panali munda ndipo mʼmundamo munali manda atsopano mʼmene munali simunayikidwemo aliyense. 42Chifukwa linali Tsiku la Ayuda Lokonzekera ndi kuti mandawo anali pafupipo, iwo anayika Yesu mʼmenemo.