约伯记 38 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 38:1-41

耶和华回答约伯

1那时,耶和华从旋风中回答约伯说:

2“是谁用无知的话蒙蔽我的旨意?

3你要像勇士一样束腰备战,

我来提问,你来回答。

4“我立大地根基的时候,你在哪里?

你若那么聪明,请告诉我。

5你可知道谁为大地定的尺寸?

谁用准绳把它丈量?

6是什么支撑大地的根基?

谁为它安放的基石?

7当时晨星齐声歌唱,

众天使都发出欢呼。

8“大海从母胎奔腾而出时,

谁为它划定界限?

9是我为大海披上云彩,

为它裹上厚厚的幽暗。

10是我为它划定界限,

并安上门和闩,

11说,‘你到此为止,不可越界;

你狂傲的波涛要停在这里。’

12“你生平可曾向晨曦发号施令,

为黎明的曙光指定岗位,

13使阳光普照大地,

抖出藏匿的恶人?

14日光使大地改观,如泥上盖印,

万物如衣服般显出颜色。

15恶人得不到光明,

强横的臂膀必折断。

16你可曾到过大海的源头,

走过深渊的底部?

17死亡之门可曾向你显露?

你可曾见过幽冥之门?

18你知道大地有多广阔吗?

你若知道,就告诉我吧。

19“哪条路通往光明的居所?

哪里是黑暗的住处?

20你能把它们带回原处吗?

你认识通往其居所的路吗?

21你肯定知道,

因为那时你已出生,

你的寿数又很长久!

22“你曾到过雪库,

或见过雹仓吗?

23那是我为降灾之时,

为争战之日而预备的。

24光从哪条路散开?

东风从哪条路吹向大地?

25谁为豪雨开水道,

为雷电辟路径,

26使雨水降在杳无人烟之地,

降在无人居住的旷野,

27以滋润荒凉不毛之地,

使土地长出青草?

28雨水有父亲吗?

谁生的露珠?

29冰出自谁的胎?

谁生的天上的霜?

30水变得坚硬如石,

深渊表面凝结成冰。

31“你能系住昴星的结,

解开参星的带吗?

32你能按季节领出星座,

引导北斗及其众星吗?

33你知道天的定律吗?

你能使地服从天律吗?

34你能号令云彩,

使倾盆大雨覆盖你吗?

35你能命闪电发出,

让它听候调遣吗?

36谁将智慧放在人胸中?

谁使人内心有聪明?

37-38尘土结成硬团,

土块黏在一起时,

谁能凭智慧数算云彩?

谁能倾倒天上的水囊?

39-40“狮子卧在洞中,

壮狮埋伏在隐秘处,

你能为它们猎取食物,

使它们饱餐吗?

41乌鸦的幼雏饿得飞来飞去,

向上帝哀鸣时,

谁供应乌鸦食物?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 38:1-41

Yehova Ayankhula

1Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:

2“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga

poyankhula mawu opanda nzeru?

3Onetsa chamuna;

ndikufunsa

ndipo undiyankhe.

4“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi?

Ndiwuze ngati ukudziwa.

5Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa!

Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?

6Kodi maziko ake anawakumba potani,

kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,

7pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi

ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?

8“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa,

pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,

9pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake

ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,

10pamene ndinayilembera malire ake

ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.

11Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire

apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’

12“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa,

kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,

13kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi

ndi kuthamangitsa anthu oyipa?

14Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo;

zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.

15Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa,

ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.

16“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja

kapena pa magwero ake ozama?

17Kodi anakuonetsapo zipata za imfa?

Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?

18Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa?

Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.

19“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti?

Nanga mdima umakhala kuti?

20Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi?

Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?

21Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale!

Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!

22“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana

kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,

23zimene ndazisungira nthawi ya mavuto

ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?

24Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani

kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?

25Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula,

nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,

26kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu,

chipululu chopandamo munthu,

27kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa

ndi kumeretsamo udzu?

28Kodi mvula ili ndi abambo ake?

Nanga madzi a mame anawabereka ndani?

29Kodi madzi owundana anawabereka ndani?

Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba

30pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala,

pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?

31“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi?

Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?

32Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake

kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?

33Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa?

Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?

34“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo

kuti igwetse mvula ya chigumula?

35Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime?

Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’

36Kodi ndani anayika nzeru mu mtima,

ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?

37Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo?

Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo

38pamene fumbi limasanduka matope,

ndipo matopewo amawumbika?

39“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi

ndi kukhutitsa misona ya mikango

40pamene ili khale mʼmapanga mwawo

kapena pamene ikubisala pa tchire?

41Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani

pamene ana ake akulirira kwa Mulungu

ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?