约伯记 37 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 37:1-24

1“因此我心战栗,

在胸膛跳动。

2请仔细听祂发出的雷声,

听祂口中发出的轰鸣。

3祂使闪电划过整个天空,

亮光直照到地极。

4随后雷声隆隆,

祂发出威严之声。

祂一发声,雷电交加。

5上帝发出奇妙的雷声,

我们无法测度祂伟大的作为。

6祂命雪降在大地,

令雨倾盆倒下,

7使人们停下工作,

以便世人都知道祂的作为。

8野兽躲进窝里,

留在洞中。

9暴风从南天而来,

寒流由北方而至。

10上帝嘘气成冰,

使宽阔的水面凝结。

11祂使密云布满水气,

从云端发出闪电。

12云随祂的指令旋转,

在地面之上完成祂的吩咐,

13或为惩罚大地,

或为彰显慈爱。

14约伯啊,请留心听,

要驻足沉思上帝的奇妙作为。

15你知道上帝如何发出命令,

使云中电光闪烁吗?

16你知道全知者的奇妙作为——

祂如何使云彩飘浮吗?

17南风吹来,大地沉寂时,

你就汗湿衣襟,你知道为何吗?

18你能像祂那样铺展坚如铜镜的穹苍吗?

19我们因愚昧而无法陈诉,

请指教我们如何与祂对话。

20我怎敢与祂对话?

岂有人自取灭亡?

21风吹散天空的云后,

无人能仰视太阳的强光。

22北方出现金色的光芒,

上帝充满可怕的威严。

23我们无法测度全能者,

祂充满能力,无比正直公义,

不恃强凌弱。

24所以,人们都敬畏祂,

祂不看顾自以为有智慧的人。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 37:1-24

1“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso

ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.

2Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake,

kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.

3Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse

ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.

4Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka.

Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero.

Pamene wabangula,

palibe chimene amalephera kuchita.

5Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa

Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.

6Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’

ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’

7Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake.

Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.

8Zirombo zimakabisala

ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.

9Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake,

kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.

10Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi

ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.

11Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula,

amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.

12Mulungu amayendetsa mitamboyo

mozungulirazungulira dziko lonse lapansi

kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.

13Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu,

kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.

14“Abambo Yobu, tamvani izi;

imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.

15Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo

ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?

16Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo,

ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?

17Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta

pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,

18kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo

limene ndi lolimba ngati chitsulo?

19“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye;

sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.

20Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu?

Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?

21Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa,

ndi kunyezimira mlengalenga,

kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.

22Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto;

Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.

23Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa;

pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.

24Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri,

kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”