约伯记 25 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 25:1-6

比勒达的回答

1书亚比勒达回答说:

2“上帝掌管一切,威严可畏,

祂在高天之上缔造和平。

3谁能计算祂天军的数目?

谁不被祂的光辉照耀?

4世人怎能在上帝面前算为义人?

妇人所生的怎能纯洁?

5在祂眼中,月亮算不上明亮,

星辰也算不上皎洁,

6更何况是像蛆一样的人,

像虫一样的世人呢?”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 25:1-6

Mawu a Bilidadi

1Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

2“Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu,

Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.

3Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka?

Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?

4Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu?

Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?

5Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni,

ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,

6nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi,

mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”