约伯记 20 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 20:1-29

琐法再度发言

1拿玛琐法回答说:

2“我感到烦躁不安,

心中有话不吐不快。

3我听见你侮辱我的斥责,

我的理智催促我回答。

4难道你不知道,从古至今,

自从世上有人以来,

5恶人得势不会长久,

不信上帝者的快乐转瞬即逝?

6虽然他傲气冲天,

把头挺到云端,

7终必如自己的粪便永远消亡,

见过他的人都不知他在何处。

8他如梦消逝,踪影杳然;

如夜间的异象,飞逝而去。

9见过他的人不会再见到他,

他将从家乡消失无踪。

10他的儿女要向穷人乞怜,

他要亲手偿还不义之财。

11他的筋骨依然强健,

却要随他葬入尘土。

12“他以邪恶为甘饴,

将其藏在舌下,

13含在口中,

慢慢品味。

14这食物在腹中变酸,

变成了蛇的毒液。

15他要吐出所吞下的财富,

上帝要倒空他腹中之物。

16他吸吮蛇的毒液,

被蛇的舌头害死。

17他无法享用流淌不尽的奶与蜜。

18他留不住劳碌的成果,

无法享用所赚的财富。

19他欺压、漠视穷人,

强占别人的房屋。

20他贪欲无度,

不放过任何喜爱之物。

21他吞掉一切所有,

他的福乐不能长久。

22他在富足时将陷入困境,

各种灾祸将接踵而至。

23上帝的怒火如雨降在他身上,

填满他的肚腹。

24他躲过了铁刃,

却被铜箭射穿。

25利箭穿透他的后背,

闪亮的箭头刺破他的胆囊,

恐怖笼罩着他。

26他的财宝消失在幽冥中,

天火20:26 天火”希伯来文是“非人手点燃的火”。要吞噬他,

焚毁他帐篷中残留的一切。

27天要揭露他的罪恶,

地要站出来指控他。

28在上帝发烈怒的日子,

洪流将席卷他的家产。

29这便是上帝为恶人定下的结局,

为他们预备的归宿。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 20:1-29

Mawu a Zofari

1Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti

2“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe

chifukwa ndasautsidwa kwambiri.

3Ndikumva kudzudzula kondinyoza,

ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.

4“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale,

kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,

5kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha,

chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.

6Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba

ndipo mutu wake uli nengʼaa,

7iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe;

iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’

8Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso,

adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.

9Diso limene linamuona silidzamuonanso;

sadzapezekanso pamalo pake.

10Ana ake adzabwezera zonse

zimene iyeyo analanda anthu osauka;

11Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake

zidzagona naye limodzi mʼfumbi.

12“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake

ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,

13ngakhale salola kuzilavula,

ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,

14koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake;

chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.

15Adzachisanza chuma chimene anachimeza;

Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.

16Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo

ululu wa mphiri udzamupha.

17Sadzasangalala ndi timitsinje,

mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.

18Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya;

sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.

19Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo;

iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.

20“Chifukwa choti umbombo wake sutha,

sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.

21Palibe chatsala kuti iye adye;

chuma chake sichidzachedwa kutha.

22Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera;

mavuto aakulu adzamugwera.

23Akadya nʼkukhuta,

Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto

ngati mvula yosalekeza.

24Ngakhale athawe mkondo wachitsulo,

muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.

25Muviwo adzawutulutsira ku msana,

songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake.

Adzagwidwa ndi mantha aakulu;

26mdima wandiweyani ukudikira chuma chake.

Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza

ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.

27Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake;

dziko lapansi lidzamuwukira.

28Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake,

katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.

29Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa,

mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”