约伯记 2 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 2:1-13

约伯失去健康

1又有一天,众天使来朝见耶和华,撒旦也在他们当中。 2耶和华问撒旦:“你从哪里来?”撒旦答道:“我在地上到处游走。” 3耶和华问道:“你注意到我的仆人约伯了吗?世上没有人像他那样纯全正直,敬畏我,远离罪恶。虽然你鼓动我无缘无故地攻击他、毁灭他,他仍然持守自己的纯正。” 4撒旦回答说:“人会以皮换皮,为了保全生命,情愿舍弃一切。 5倘若你伸手伤害他的骨和肉,他必当面亵渎你。” 6耶和华说:“好吧,他在你手中,但要留他一命。” 7于是,撒旦从耶和华面前退去,开始加害约伯,使他从头到脚长毒疮。 8约伯坐在炉灰中,拿瓦片刮身体。 9他的妻子对他说:“你还要持守自己的纯正吗?不如亵渎上帝,死掉算了!” 10约伯回答说:“你说话像个愚昧的妇人。难道我们只从上帝手里接受祝福,却不接受灾殃吗?”约伯遭此不幸,仍毫无怨言。

约伯的三个朋友

11约伯的三个朋友提幔以利法书亚比勒达拿玛琐法听到他的不幸遭遇,便各自从家乡动身,相约一起来探望、安慰他。 12他们远远地看见约伯,几乎认不出是他,禁不住放声大哭,各自撕裂外袍,扬起尘土,让土落在头上。 13他们看到约伯极其痛苦,就陪着他在地上坐了七天七夜,没有对他说一句话。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 2:1-13

Yobu Ayesedwa Kachiwiri

1Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova. 2Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?”

Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”

3Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”

4Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo. 5Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”

6Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”

7Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse. 8Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.

9Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”

10Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?”

Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.

Abwenzi Atatu a Yobu

11Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza. 12Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo. 13Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.