约伯记 15 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 15:1-35

以利法再次发言

1提幔以利法回答说:

2“智者岂会用空谈作答,

满腹东风?

3申辩时岂会讲无用的话,

说无益之言?

4你摒弃对上帝的敬畏,

拒绝向祂祷告。

5你的罪指示你开口,

使你说出诡诈之言。

6并非我定你的罪,

定你罪的是你的口,

指控你的是你的嘴唇。

7你岂是第一个出生的人?

你岂在群山之前被造?

8你岂听过上帝的密旨?

你岂独揽智慧?

9有何事你知而我们不知,

你懂而我们不懂?

10我们这里有白发老人,

比你父亲还年长。

11上帝用温柔的话安慰你,

难道你还嫌不够吗?

12你为何失去理智,

为何双眼冒火,

13以致你向上帝发怒,

口出恶言?

14人算什么,怎能纯洁?

妇人所生的算什么,怎能公义?

15连上帝的圣者都无法令祂信任,

连诸天在祂的眼中都不洁净,

16更何况可憎败坏、

嗜恶如喝水的世人?

17“让我告诉你,你好好听着。

我要把所见的陈明——

18那是智者的教导,

是他们未曾隐瞒的祖训。

19这片土地只赐给了他们,

没有外人在他们中间出入。

20恶人一生受折磨,

残暴之徒终身受苦。

21他耳边响着恐怖的声音,

他安逸时遭强盗袭击。

22他不指望能逃脱黑暗,

他注定要丧身刀下。

23他到处流浪,寻找食物,

他知道黑暗之日快要来临。

24患难和痛苦使他害怕,

像君王上阵一样震慑他。

25因为他挥拳对抗上帝,

藐视全能者,

26拿着坚盾傲慢地挑战祂。

27他满脸肥肉,

腰间堆满脂肪。

28他住的城邑必倾覆,

他的房屋必成为一堆瓦砾,

无人居住。

29他不再富足,

家财不能久留,

地产无法加增。

30他无法逃脱黑暗,

火焰要烧焦他的嫩枝,

上帝口中的气要毁灭他。

31他不可自欺,信靠虚空,

因为虚空必成为他的回报。

32在他离世以前,虚空必临到他,

他的枝子再不会青绿。

33他必像一颗葡萄树,

葡萄未熟已掉落;

又像一颗橄榄树,

花刚开便凋零。

34不信上帝之辈必不生育,

受贿者的帐篷必被火烧。

35他们心怀不轨,生出罪恶,

他们满腹诡诈。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 15:1-35

Mawu a Elifazi

1Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

2“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere,

kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?

3Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake,

kapena kuyankhula mawu opanda phindu?

4Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu

ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.

5Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo;

ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.

6Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga;

milomo yakoyo ikukutsutsa.

7“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa?

Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?

8Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu?

Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?

9Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa?

Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?

10Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu,

anthu amvulazakale kupambana abambo ako.

11Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira,

mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?

12Chifukwa chiyani ukupsa mtima,

ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,

13moti ukupsera mtima Mulungu

ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?

14“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima

kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?

15Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake,

ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,

16nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota,

amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.

17“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera;

ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,

18zimene anandiphunzitsa anthu anzeru,

sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.

19(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa

pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).

20Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake,

munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.

21Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake,

pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.

22Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa;

iyeyo ndi woyenera kuphedwa.

23Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya;

amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.

24Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri;

zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,

25chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu

ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.

26Amapita mwa mwano kukalimbana naye

atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.

27“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa

ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,

28munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka

ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu,

nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.

29Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa,

ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.

30Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo;

lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake,

ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.

31Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe,

pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.

32Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane,

ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.

33Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse,

adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.

34Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala

ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.

35Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa;

mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”