箴言 17 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

箴言 17:1-28

1粗茶淡饭但相安无事,

胜过佳肴满桌却勾心斗角。

2精明的仆人必管辖主人的不肖子,

并与他们一同承受家业。

3鼎炼银,炉炼金,

耶和华试炼人心。

4作恶者留心听恶言,

说谎者侧耳听坏话。

5嘲笑穷人等于侮辱造物主,

幸灾乐祸的人必难逃惩罚。

6子孙是老人的华冠,

父母是儿女的荣耀。

7愚人高谈阔论不相称,

统治者说谎更不合适。

8行贿者视贿赂为法宝,

可以使他无往不利。

9饶恕过犯,促进友爱;

重提旧恨,破坏友情。

10责备哲士一句,

胜过杖打愚人百下。

11恶人一心反叛,

残忍的使者必奉命来惩罚他。

12宁愿遇见丢失幼崽的母熊,

也不愿碰上做蠢事的愚人。

13人若以恶报善,

家里必祸患不断。

14争端爆发如洪水决堤,

当在爆发前将其制止。

15放过罪人、冤枉义人,

都为耶和华所憎恶。

16愚人无心求智慧,

手中有钱有何用?

17朋友时时彼此关爱,

手足生来患难与共。

18无知的人才会为他人作保。

19喜爱争斗的喜爱犯罪,

骄傲自大的自招灭亡。

20心术不正,难觅幸福;

口吐谎言,陷入祸患。

21生愚昧子带来忧伤,

愚人之父毫无喜乐。

22喜乐的心乃是良药,

忧伤的灵使骨枯干。

23恶人暗中收受贿赂,

颠倒是非。

24哲士追求智慧,

愚人漫无目标。

25愚昧的孩子令父亲忧虑,让母亲苦恼。

26责罚义人不妥,

杖责君子不义。

27谨言慎行的有知识,

温和冷静的有悟性。

28愚人缄默可算为智慧,

闭口不言可算为明智。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 17:1-28

1Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere,

kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.

2Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi,

ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.

3Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo,

koma Yehova amayesa mitima.

4Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa;

munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.

5Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake;

amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.

6Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba,

ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.

7Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru,

nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?

8Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo;

kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.

9Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi;

wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.

10Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha,

munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.

11Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi;

ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.

12Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake

kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.

13Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino,

ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.

14Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi,

choncho uzichokapo mkangano usanayambe.

15Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa,

zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.

16Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru

poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?

17Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse,

ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.

18Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole

ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.

19Wokonda zolakwa amakonda mkangano,

ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.

20Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino;

ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.

21Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake,

abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.

22Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino,

koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.

23Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri

kuti apotoze chiweruzo cholungama.

24Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru,

koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.

25Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake

ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.

26Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa,

kapena kulanga anthu osalakwa.

27Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu,

ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.

28Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete;

ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.