申命记 31 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

申命记 31:1-30

立约书亚做摩西的接班人

1摩西继续对以色列人说: 2“我已经一百二十岁了,无法再继续带领你们,耶和华曾说我不得过约旦河。 3你们的上帝耶和华要亲自带领你们过河,在你们面前消灭那里的各族,使你们占领他们的土地。约书亚将做你们的首领,正如耶和华所言。 4耶和华要毁灭那里的各族,像毁灭亚摩利二王西宏及其国家一样。 5耶和华要把他们交给你们,你们要照我的一切吩咐处置他们。 6你们要刚强勇敢,不要怕他们,因为你们的上帝耶和华与你们同在,祂不会撇下你们,也不会离弃你们。”

7摩西约书亚叫来,当着全体以色列人的面对他说:“你要刚强勇敢!因为你要带领百姓进入耶和华起誓赐给他们祖先的土地,把土地分给他们。 8耶和华必带领你,与你同在。祂不会撇下你,也不会离弃你。不要害怕,也不要沮丧。”

每七年当众宣读律法一次

9摩西把这律法写好,交给抬耶和华约柜的利未祭司和以色列的众长老。 10摩西吩咐他们说:“每逢免除债务的第七年的住棚节, 11所有以色列人到你们的上帝耶和华选定的地方朝见祂时,你们要当众大声宣读这律法。 12要招聚所有男女、孩童以及住在你们中间的外族人,让他们聆听这律法,学习敬畏你们的上帝耶和华,谨遵律法上的一切话。 13这样,他们那些还不知道这律法的孩子便有机会听到律法,在你们将要占领的约旦河对岸的土地上,学习终生敬畏你们的上帝耶和华。”

上帝对摩西和约书亚的指示

14耶和华对摩西说:“你快要离世了。叫约书亚与你一起到会幕,我要委派他。”摩西约书亚就去了会幕。 15有云柱停在会幕入口的上方,耶和华在云柱中向他们显现。

16耶和华对摩西说:“你快要与祖先同眠了。这些百姓将很快在要占领的土地上与外族人的神明苟合,背弃我,违背我与他们所立的约。 17那时,我要向他们发怒,离弃他们,掩面不理他们。他们将被吞灭,遭遇许多祸患和灾难,以致他们会说,‘这些祸患临到我们岂不是因为上帝不在我们中间了吗?’ 18那时,我必掩面不理他们,因为他们祭拜别的神明,行为邪恶。

19“现在,你要写一首歌,教导以色列人,让他们背诵,作为我指控他们的证据。 20因为当我把他们带到我起誓应许他们祖先的奶蜜之乡后,当他们在那里吃饱喝足后,就会嫌弃我,违背我与他们所立的约,去供奉别的神明。 21当许多祸患和灾难临到他们的时候,这首歌就要成为指控他们的证据,因为这首歌要在他们的子孙中世代流传。虽然我还没有带领他们进入我起誓应许之地,我已经知道他们的心思意念。” 22当天,摩西就写下这首歌,传授给以色列人。

23耶和华嘱咐的儿子约书亚:“你要刚强勇敢,因为你要带领以色列人进入我起誓应许他们的土地,我必与你同在。”

24摩西把这律法都写在书上以后, 25就吩咐抬耶和华约柜的利未人: 26“把这律法书放在你们的上帝耶和华的约柜旁,作为指控你们的证据。 27我知道你们悖逆、顽固不化,我还活在你们中间的时候,你们尚且背叛上帝,何况我死后呢? 28把你们各支派的长老和首领招聚来,我要把这些话告诉他们,叫天地作证来指控他们。 29我知道,我死后你们会彻底堕落,偏离我吩咐你们行的道,做耶和华视为恶的事,惹祂发怒,将来祸患必临到你们。”

30然后,摩西把这首诗歌读给以色列全体会众听。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 31:1-30

Yoswa Alowa Mʼmalo mwa Mose

1Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse: 2“Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’ 3Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova. 4Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo. 5Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani. 6Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”

7Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo. 8Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”

Kuwerenga Malamulo

9Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli. 10Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa, 11pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva. 12Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa. 13Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”

Aneneratu za Kuwukira kwa Aisraeli

14Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.

15Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti. 16Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo. 17Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’ 18Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.

19“Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa. 20Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa. 21Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.” 22Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.

23Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”

24Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu, 25analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti, 26“Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani. 27Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira! 28Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa. 29Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”

Nyimbo ya Mose

30Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva: