申命记 19 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

申命记 19:1-21

设立避难城

1“你们的上帝耶和华毁灭那些民族,把他们的土地赐给你们,使你们赶走他们,住进他们的城邑和房屋后, 2-3你们要把土地划分为三个地区,在每个地区设立一座避难城,修好通往这三座城的道路,以便误杀人者可以逃往最近的避难城。

4“如果有人无意间杀了素无冤仇的同伴,他可以逃往避难城,以保住性命。 5例如,有人和朋友去森林砍树,斧头脱柄,误杀了朋友,他就可以逃往避难城,以保住性命。 6否则,如果避难城离误杀人者太远,怒火中烧的报仇者就会追上去杀死他。其实他是不该死的,因为他与被误杀的人素无冤仇。 7因此,我吩咐你们要设立三座避难城。

8-9“如果你们谨遵我今天吩咐你们的这一切诫命,爱你们的上帝耶和华,一生遵行祂的旨意,祂就会按照祂对你们祖先所起的誓,扩张你们的疆域,把应许给你们祖先的土地赐给你们。那时,你们要再设三座避难城, 10免得无辜人的血流在你们的上帝耶和华赐给你们作产业之地,以致你们担当枉杀无辜的罪。

11“如果有人因憎恨邻居而暗中埋伏,杀了邻居,然后逃到避难城, 12他本城的长老要派人去把他带回来,交给复仇的人,将他处死。 13不可怜悯他,要从以色列除掉这种滥杀无辜的罪,这样你们才会顺利。

14“在你们的上帝耶和华将要赐给你们作产业之地,你们不可挪动邻居的界石,因为那是先人立的。

15“如果人犯了什么罪或有什么过失,不可凭一个证人作证就定罪,要有两三个证人才可以定案。 16如果有人作伪证诬陷别人, 17诉讼双方要站在耶和华面前,让当值的祭司和审判官定夺。 18审判官要仔细审查案件,如果发现那人作伪证, 19就要按照他企图加给被诬告者的伤害处罚他。这样,就从你们当中除掉了罪恶。 20其他人听说后,都会害怕,不敢再做这种恶事。 21你们对恶人不可心软,要以命偿命,以眼还眼,以牙还牙,以手还手,以脚还脚。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 19:1-21

Mizinda Yothawirako

1Yehova Mulungu wanu akadzawononga anthu amene dziko lawo akukupatsani, ndipo inu mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼmizinda ndi mʼnyumba zawo, 2mukapatule mizinda itatu imene ili pakati pa dziko lomwe Yehova Mulungu akukupatsani kukhala lanu. 3Mudzakonze misewu ndi kuligawa patatu dzikolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, kuti aliyense wopha munthu akhoza kuthawirako.

4Ili ndi lamulo lokhudza munthu amene wapha mnzake mosazindikira osati mwadala, nathawira kumeneko kupulumutsa moyo wake. Ndi munthu amene wapha mnzake mosazindikira, popanda maganizo oyipa. 5Mwachitsanzo, munthu atapita ku nkhalango ndi mnzake kukadula mitengo, ndiye posamula nkhwangwa kuti adule mtengo, nkhwangwa ikhoza kuguluka nʼkukagwera mnzake uja nʼkumupha. Munthu ameneyo akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizindayo napulumutsa moyo wake. 6Kupanda kutero ndiye kuti wolipsira akhoza kumuthamangitsa mwaukali ndi kumugwira ngati mtunda utalika, ndipo akhoza kumupha ngakhale kuti sanayenera kufa popeza sanaphe mnzake mwadala. 7Ichi ndi chifukwa chake ndikukulamulani kuti mudzipatulire nokha mizinda itatu.

8Ngati Yehova Mulungu wanu akulitsa malire anu monga analonjezera pa malumbiro ndi makolo anu, nakupatsani dziko lonse monga analonjezera, 9chifukwa chotsatira bwino malamulo onse amene ndikukuwuzani lero, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse, ndiye kuti mukuyenera kupatula mizinda itatu yowonjezera. 10Muchite zimenezi kuti musakhetse magazi wosalakwa mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa, ndipo kuti musapezeke ndi mlandu wokhetsa magazi.

11Koma ngati munthu adana ndi mnzake namubisalira panjira nʼkumuvulaza mpaka kumupha, nathawira ku umodzi mwa mizindayi, 12akuluakulu a mu mzinda wake akamugwire ndi kumubwezera ku mzinda wake namupereka kwa wolipsira kuti aphedwe. 13Osamumvera chisoni. Muyenera kuchotsa tchimo lokhetsa magazi wosalakwa mu Israeli kuti zinthu zizikuyenderani bwino.

14Musamasunthe mwala wa malire anu ndi mnzanu amene anayikidwa ndi makolo anu pa cholowa chimene mulandire mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.

Mboni

15Mboni imodzi siyokwanira kupeza munthu kuti ndi wolakwa pa mlandu uliwonse umene wapalamula. Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.

16Ngati mboni yonama ifuna kunamizira munthu mlandu, 17anthu awiri okhudzidwa ndi mlanduwo ayenera kuyima pamaso pa Yehova pali ansembe ndi oweruza amene ali pa ntchito pa nthawiyo. 18Oweruza afufuze bwinobwino, ndipo ngati zatsimikizika kuti mboniyo ndi yabodza, yopereka umboni wonama pa mʼbale wake, 19ndiye kuti amuchitire iyeyo zimene anafuna kuchitira mʼbale wakezo. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu. 20Anthu ena onse adzamva zimenezi nachita mantha, ndipo choyipa choterechi sichidzachitikanso pakati panu. 21Osachita chisoni, moyo uzilipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja ndi phazi kulipira phazi.