民数记 8 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

民数记 8:1-26

安置七盏灯

1耶和华对摩西说: 2“你告诉亚伦,安放灯的时候,七盏灯都要照向灯台的前面。” 3亚伦就照耶和华对摩西的吩咐把灯放好,使灯照向前方。 4整座灯台,从灯座到上面的花苞,都是照耶和华对摩西的吩咐用金子锤制而成的。

为利未人行洁净与奉献礼

5耶和华对摩西说: 6“你要把利未人从其他以色列人中分别出来,洁净他们。 7要用以下的方法洁净他们,把洁净水洒在他们身上,叫他们用剃刀剃净全身,洗净衣服,这样他们就洁净了。 8然后叫他们带来一头公牛犊及作素祭的调了油的细面粉,你要另献一头公牛犊作赎罪祭。 9你要招聚以色列全体会众,将利未人带到会幕前, 10带到耶和华面前,会众要按手在他们身上。 11亚伦要把他们献给耶和华,作为以色列人献的摇祭,使他们可以事奉耶和华。 12利未人要按手在那两头公牛的头上,然后你要把一头作为赎罪祭,一头作为燔祭献给耶和华,好为利未人赎罪。 13你要让利未人站在亚伦父子们面前,把他们当作摇祭献给耶和华。 14这样,你就把利未人从其他以色列人中分别出来,使他们归给我。 15利未人被洁净、当作摇祭献上以后,就可以进会幕司职, 16因为在以色列人中,他们完全属于我,我拣选他们归我所有,以代替以色列人所有的长子。 17以色列人所有的长子和头生的牲畜都属于我。我击杀埃及人所有的长子和头生的牲畜那天,已把以色列人所有的长子和头生的牲畜都分别出来,使之圣洁,归给我。 18我现在已拣选利未人代替以色列人所有的长子, 19把他们交给亚伦父子们,替以色列人在会幕中司职,为以色列人赎罪,免得以色列人因接近圣所而遭祸。”

20摩西亚伦以色列全体会众就按照耶和华对摩西的吩咐把利未人献上。 21利未人自洁、洗净衣服后,亚伦把他们当作摇祭献给耶和华,又为他们赎罪,使他们洁净。 22之后,利未人便进入会幕,在亚伦父子们的监督下司职。以色列人照耶和华对摩西的吩咐奉献了利未人。

23耶和华对摩西说: 24“二十五岁以上的利未人都要到会幕司职, 25五十岁时退休。 26退休之后,他们可以协助本族弟兄看守会幕,不用再司职。你要这样给他们分派工作。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 8:1-26

Za Nyale

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aaroni kuti pamene uyimika nyale zisanu ndi ziwiri, nyalezo ziziyaka kutsogolo kwa choyikapo nyale.”

3Aaroni anachitadi zomwezo. Anayimika nyale ndi kuziyangʼanitsa kumene kunali choyikapo nyale monga Yehova analamulira Mose. 4Choyikapo nyalecho chinapangidwa motere: chinasulidwa kuchokera ku golide, kuyambira pa tsinde pake mpaka ku maluwa ake. Choyikapo nyalecho chinapangidwa monga momwe Yehova anaonetsera Mose.

Za Kupatulidwa kwa Alevi

5Yehova anawuza Mose kuti, 6“Tenga Alevi pakati pa Aisraeli ndipo uwayeretse. 7Powayeretsa uchite izi: uwawaze madzi oyeretsa ndipo amete thupi lawo lonse ndi kuchapa zovala zawo kuti adziyeretse. 8Atenge ngʼombe yayimuna yayingʼono ndi chopereka cha chakudya cha ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Atengenso ngʼombe ina yayimuna, yayingʼono, ya chopereka chopepesera machimo. 9Ubwere nawo Aleviwo kutsogolo kwa tenti ya msonkhano ndipo usonkhanitse gulu la Aisraeli. 10Ubwere nawo pamaso pa Yehova, ndipo Aisraeli asanjike manja awo pa iwo. 11Aaroni apereke Alevi aja pamaso pa Yehova ngati chopereka choweyula kuchokera kwa Aisraeli kuti akhale okonzeka kugwira ntchito ya Yehova.

12“Alevi akatsiriza kusanjika manja awo pa mitu ya ngʼombe zazimuna, imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza ya kwa Yehova, kupepesera machimo a Alevi. 13Uyimiritse Aleviwo pamaso pa Aaroni ndi ana ake aamuna ndipo uwapereke ngati nsembe yoweyula kwa Yehova. 14Pochita zimenezi mudzapatula Alevi pakati pa Aisraeli ndipo Aleviwo adzakhala anga.

15“Utatha kuyeretsa ndi kupereka Aleviwo monga nsembe yoweyula, apite kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano. 16Iwo ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwathunthu kwa Ine. Ndawatenga kuti akhale anga mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa wa Mwisraeli aliyense wamkazi. 17Mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa mu Israeli, kaya wa munthu kapena wa ziweto, ndi wanga. Pamene ndinakantha ana oyamba kubadwa ku Igupto, ndinawapatulira kwa Ine mwini. 18Ndipo ndatenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna onse oyamba kubadwa mu Israeli. 19Mwa Aisraeli onse, ndapereka Alevi kuti akhale mphatso kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kugwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti azikapereka nsembe yopepesera machimo, kuti mliri usadzaphe Aisraeli pamene ayandikira ku malo wopatulika.”

20Mose, Aaroni pamodzi ndi gulu lonse la Israeli anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose. 21Alevi anadziyeretsa ndi kuchapa zovala zawo. Kenaka Aaroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe yopepesera machimo yowayeretsa. 22Zitatha zimenezi, Alevi anapita kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.

23Yehova anawuza Mose kuti, 24“Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano. 25Koma akakwana zaka makumi asanu, apume pa ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku ndi kulekeratu kugwira ntchitoyo. 26Atha kuthandiza abale awo kugwira ntchito za ku tenti ya msonkhano, koma iwowo asamagwire ntchitoyo. Mmenemu ndimo ugawire ntchito yomwe azigwira Alevi.”