撒母耳记下 4 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

撒母耳记下 4:1-12

伊施波设被杀

1扫罗的儿子伊施波设听到押尼珥死在希伯仑,吓得手脚发软,整个以色列都震惊不已。 2那时,扫罗的儿子有两个带兵的将领,一个叫巴拿,一个叫利甲,他们是来自比录便雅悯临门的儿子。 3原来的比录人逃到基他音,寄居在那里,直到今日。

4扫罗的儿子约拿单有个儿子叫米非波设,双腿是瘸的。扫罗约拿单耶斯列阵亡的时候,他才五岁。乳娘抱着他仓皇逃命,不慎把他掉在地上,摔成了瘸子。

5一天,伊施波设正在午睡,临门的两个儿子利甲巴拿来到他家。 6-7他们装作是来取麦子,进入伊施波设的寝室,趁他正躺在床上熟睡,用刀刺透他的肚子杀了他,割下他的首级,拿着连夜穿过亚拉巴逃跑了。 8他们把伊施波设的首级带到希伯仑献给大卫王,说:“这便是扫罗的儿子伊施波设的首级。扫罗是你的仇敌,曾试图杀害你,今天耶和华为我主我王惩罚了扫罗和他的子孙。” 9大卫比录临门的儿子利甲及其兄弟巴拿说:“我凭救我脱离一切危难的永活的耶和华起誓, 10洗革拉曾有人向我报信说扫罗死了,他以为是来报喜讯,我抓住他,把他杀了。那就是我给他的报酬。 11更何况你们这些恶徒在这个无辜人的家里把他杀死在床上,我怎能不向你们讨这血债,把你们从世上除掉?” 12于是,大卫命令部下杀了他们,斩断他们的手脚,把尸体挂在希伯仑的池旁。他们把伊施波设的头颅葬在希伯仑押尼珥的坟墓里。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 4:1-12

Kuphedwa kwa Isiboseti

1Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri. 2Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini, 3chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.

4(Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).

5Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula. 6Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.

7Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba. 8Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”

9Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse, 10pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake! 11Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”

12Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.