撒母耳记上 29 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

撒母耳记上 29:1-11

非利士人不信任大卫

1非利士人把全部军队聚集在亚弗以色列军则在耶斯列水泉旁扎营。 2非利士首领统率以百人和千人为单位的士兵向前推进,大卫和他的部下跟着亚吉走在队伍的后面。 3非利士人的官长说:“这些希伯来人在这里做什么?”亚吉告诉他们说:“这是以色列扫罗的臣仆大卫,他追随我有一段日子了,自从他投奔我以来,我没发现他有什么过错。” 4他们却生气地说:“请送这个人回到你安置他的地方,他不可和我们一起去打仗,免得他在战场上倒戈。他提着我们的脑袋去重投故主岂不是最好的方法吗? 5以前妇女们跳舞歌唱‘扫罗杀死千千,大卫杀死万万’,歌颂的不就是这个大卫吗?”

6亚吉便叫大卫过来,对他说:“我凭永活的耶和华起誓,你一向忠心耿耿,自从你投奔我以来,我没发现你有什么过错,我很愿意你与我一同作战,只是众首领不赞成。 7你安心地回去吧,免得他们不悦。” 8大卫说:“我究竟做错了什么?自从仆人投奔你以来,你发现仆人有什么过错?为什么不让我为我主我王杀敌呢?” 9亚吉说:“你在我眼中就像上帝的天使一样好,只是非利士众官长反对你与我们一起出战。 10明天一早,你就和从扫罗手下投奔你的人启程回去吧。”

11于是,大卫和部下清早起来返回非利士非利士军则前往耶斯列

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 29:1-11

Afilisti Akana Davide

1Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli. 2Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi. 3Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?”

Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”

4Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa? 5Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti,

“ ‘Sauli wapha anthu 1,000

koma Davide wapha miyandamiyanda?’ ”

6Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna. 7Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”

8Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”

9Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’ 10Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”

11Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.