撒母耳记上 17 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

撒母耳记上 17:1-58

大卫迎战歌利亚

1非利士人在犹大梭哥招聚军队,准备作战。他们在梭哥亚西加之间的以弗·大悯扎营。 2扫罗以色列人也聚集起来在以拉谷安营,摆好阵势准备迎战。 3双方的军队在两边的山上对峙,中间隔着山谷。 4非利士营中有个名叫歌利亚的巨人出来讨战。他来自迦特,身高三米, 5头戴铜盔,身穿重达五十七公斤的铠甲, 6腿上有铜护膝,肩背铜戟。 7戟柄粗如织布机的轴,铁戟头重七公斤。有卫士拿着他的盾牌走在前面。 8他挑战以色列人,说:“你们为什么列阵打仗呢?我是非利士人,你们是扫罗的仆人,你们选一个人下来跟我一比高下。 9如果他打得过我,将我杀了,我们就做你们的奴隶。但如果我战胜他,把他杀了,你们就要做我们的奴隶,服侍我们。 10我今天向以色列军队骂阵,你们找一个人出来跟我比个高下吧!” 11扫罗和所有以色列人听了非利士人的这些话,都吓得惊恐不已。

12大卫以法他耶西的儿子。扫罗执政期间,耶西已经年纪老迈,住在犹大伯利恒,有八个儿子。 13他的三个儿子已经跟随扫罗去打仗了,他们是长子以利押、次子亚比拿达和三子沙玛14大卫年纪最小,他的三个哥哥跟随扫罗期间, 15他有时去扫罗的军营,有时回伯利恒为他父亲放羊。 16非利士人早晚都出来骂阵,长达四十天。

17一天,耶西大卫说:“你带上十公斤烤麦和十个饼,赶快到军营中送给你的哥哥们。 18再带十块奶饼送给他们的千夫长,看望一下他们,带个信儿回来。 19他们跟随扫罗率领的以色列军在以拉谷跟非利士人打仗。”

20大卫清早起来把羊交给一个牧人看顾,然后照父亲的吩咐带着食物出发了。他来到军营的时候,大军正吶喊着出战。 21以色列人与非利士人摆好阵势,两军对垒。 22大卫把带来的东西交给负责看守的人保管,自己跑到阵中去问候哥哥们。 23他们正在交谈的时候,非利士军中的迦特歌利亚出来像往常一样向以色列军骂阵,大卫都听见了。 24以色列人一看见歌利亚都竞相奔逃,极其害怕。 25以色列人彼此议论说:“看那个人!他是来向以色列军骂阵的。谁要能杀死他,王必有重赏,还会把女儿嫁给他为妻,并免去他父亲家在以色列应缴的赋税。” 26大卫问站在旁边的人:“如果有人杀了这非利士人,洗掉以色列人的羞辱,他会得到什么呢?这个未受割礼的非利士人是谁?竟敢向永活上帝的军队骂阵!” 27他们就把刚才的话一一告诉大卫

28大卫的长兄以利押听见他跟人说话,就愤怒地对他说:“你来这里做什么?你把旷野的那几只羊交给谁了?我知道你骄傲自大,心怀恶意,你来只是想看打仗。” 29大卫说:“我做错了什么?我问一下都不行吗?” 30他又去问其他人同样的问题,得到了同样的答复。 31有人听见了大卫的话,就去告诉扫罗扫罗便派人来召大卫32大卫扫罗说:“大家不要因这个非利士人而丧胆,让仆人去战他。” 33扫罗说:“你不能去,你年纪还小,他却是一个久经沙场的战士。” 34大卫说:“我一直替父亲放羊,有时候狮子或熊会从羊群中叼走羊, 35我会去追打它,把羊从它口中救出来。如果它起来攻击我,我就揪着它的胡子把它打死。 36我曾打死过狮子和熊。这未受割礼的非利士人竟敢向永活上帝的军队骂阵,他的下场也必像狮子和熊一样。 37耶和华曾经从狮子和熊的利爪下拯救我,祂也必从非利士人手中拯救我。”扫罗大卫说:“去吧,愿耶和华与你同在。” 38扫罗把自己的战袍给大卫穿上,又给他戴上自己的头盔,穿上自己的铠甲。 39大卫把刀挎在战袍上,试着走了几步,却不习惯这种装束,就对扫罗说:“我穿着这些无法作战,因为我不习惯。”他便摘下头盔,卸下铠甲, 40然后拿着杖,在溪里捡了五块光滑的石头放进牧人用的袋子,拿着投石器向歌利亚走去。

41歌利亚也迎着大卫走来,卫士拿着他的盾牌走在前面。 42歌利亚大卫是个面色红润、相貌英俊的少年,就藐视他。 43他对大卫说:“你拿着棍子来战我,难道我是一条狗吗?”他就凭自己的神明咒诅大卫44又说:“你过来,我要把你的肉丢给天上的飞禽和地上的走兽。” 45大卫答道:“你是靠刀枪剑戟来攻击我,我是靠万军之耶和华的名,就是你所蔑视的以色列军队的上帝来迎战你。 46今天,耶和华必把你交在我手中,我必杀死你,砍掉你的头,用非利士军兵的尸体喂天上的飞禽和地上的走兽,使普天下都知道以色列有上帝。 47这里所有的人都必知道耶和华拯救人不靠刀枪,因为祂掌管战争的胜负。祂必把你们交在我们手中。” 48歌利亚迎面走来的时候,大卫就飞快地跑上去应战, 49他从袋里拿出一块石子用投石器猛力抛去,石子击中歌利亚的额头,嵌了进去,他迎面栽倒在地。

50大卫就这样不用刀剑,只用投石器和一块石子战胜了那个非利士人,杀死了他。 51大卫跑到那非利士人身边,从他刀鞘里拔出刀杀了他,并割下他的头颅。非利士人看见自己的英雄死了,纷纷逃跑。 52以色列人和犹大人乘势吶喊,追杀非利士人,直追到迦特以革伦的城门。通往迦特以革伦沙拉音大道上到处是非利士人的尸体。 53以色列军队追杀非利士人回来,又掳掠了他们的营地。 54大卫把那非利士人的头颅带到耶路撒冷,把那人的兵器存放在自己的帐篷中。

55扫罗看见大卫出去迎战歌利亚,就问押尼珥元帅:“押尼珥啊,那少年是谁的儿子?”押尼珥答道:“王啊,我向你发誓,我真的不知道。” 56扫罗王说:“你去查查他是谁的儿子。” 57大卫杀了歌利亚回来,押尼珥就把他带到扫罗那里,他手上还拿着那非利士人的头颅。 58扫罗问他:“年轻人,你是谁的儿子?”大卫答道:“我是你仆人伯利恒耶西的儿子。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 17:1-58

Davide ndi Goliati

1Afilisti anasonkhanitsa ankhondo awo ku Soko mʼdziko la Yuda. Iwo anamanga misasa yawo ku Efesi-Damimu, pakati pa Soko ndi Azeka. 2Sauli ndi Aisraeli anasonkhana namanga misasa mʼchigwa cha Ela ndipo anandandalitsa ankhondo kuti amenyane ndi Afilisti. 3Afilisti anali phiri lina ndipo Aisraeli analinso phiri lina, ndipo pakati pawo panali chigwa.

4Tsono munthu wina wamphamvu, dzina lake Goliati wochokera ku Gati anatuluka ku misasa ya Afilisti. Msinkhu wake unali pafupipafupi mamita atatu. 5Iye ankavala chipewa chamkuwa ndi malaya achitsulo olemera makilogalamu 57. 6Ankavalanso zokuta miyendo yake zamkuwa, ndipo ankanyamula nthungo ya mkuwa pa phewa pake. 7Thunthu la mkondo wake linali ngati mkombero wowombera nsalu, ndipo mutu wa mkondowo unkalemera makilogalamu asanu ndi awiri. Patsogolo pake pamakhala munthu wonyamula zida zake za nkhondo.

8Goliatiyo anayimirira ndi kufuwula kwa ankhondo a Israeli, nati, “Nʼchifukwa chiyani mwakonzekera nkhondo chotere? Kodi sindine Mfilisiti ndipo inu sindinu akapolo a Sauli? Sankhani munthu kuti abwere kwa ine. 9Ngati angathe kumenyana nane ndi kundipha, ife tidzakhala akapolo anu, koma ngati ine ndimugonjetsa ndi kumupha, inu mudzakhala akapolo athu ndi kumatitumikira.” 10Ndipo Mfilisitiyo anati, “Bwerani lero timenyane basi! Patseni munthu kuti ndimenyane naye.” 11Atamva mawu a Mfilisitiyo, Sauli ndi Aisraeli onse anataya mtima nachita mantha kwambiri.

12Davide anali mwana wa munthu wa fuko la Efurati dzina lake Yese amene amachokera ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Yese anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri. Pa nthawi ya Sauli nʼkuti ali wokalamba. 13Ana atatu oyamba kubadwa a Yese nʼkuti atapita nawo ku nkhondo pamodzi ndi Sauli. Woyamba dzina lake anali Eliabu, wachiwiri anali Abinadabu, ndipo wachitatu anali Sama. 14Davide ndiye anali mzime. Ana aakulu atatuwo ndiwo anapita ku nkhondo ndi Sauli. 15Koma Davide ankapita ku misasa ya Sauli ndi kubwerako kuti azikaweta nkhosa za abambo ake ku Betelehemu.

16Kwa masiku makumi anayi, Mfilisiti uja ankabwera mmawa ndi madzulo kumadzionetsera.

17Tsiku lina Yese anawuza mwana wake Davide kuti, “Atengere abale ako makilogalamu khumi a tirigu wokazinga ndi malofu a buledi khumi ndipo upite nazo mofulumira ku misasa yawo. 18Utengerenso wolamulira wa gulu lawo tchizi khumi uyu. Ukaone mmene abale ako akukhalira ndipo ubwere ndi kanthu kosonyeza kuti ali bwino. 19Sauli, abale akowo ndi asilikali onse a Israeli ali ku chigwa cha Ela, akumenyana ndi Afilisti.”

20Mʼmamawa mwake Davide anasiya nkhosa mʼmanja mwa munthu wina ndipo anatenga zakudyazo nanyamuka monga momwe Yese abambo ake anamulamulira. Anakafika ku misasa pamene asilikali ankapita kukandanda pa mzere ku nkhondo, nʼkufuwula mfuwu wankhondo. 21Aisraeli ndi Afilisti anandanda pa mzere wankhondo moyangʼanana. 22Tsono Davide anasiyira zakudya zija munthu wosunga katundu nathamangira kumene kunali ankhondo kuja ndi kukalonjera abale ake. 23Pamene iye ankayankhula nawo anangoona Goliati wa ku Gati uja akuchoka pa mzere wa Afilisti akufuwula mawu onyoza monga mwa masiku onse, ndipo Davide ankawamva. 24Aisraeli ataona munthuyo, anamuthawa ndi mantha aakulu.

25Ndipo Aisraeli ankanena kuti, “Kodi mwamuona munthu akubwerayo? Iye amangobwera kudzanyoza Israeli. Tsono mfumu inati kuti idzapereka chuma chambiri kwa munthu amene adzamuphe. Idzaperekanso mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndiponso banja la abambo ake silidzaperekanso msonkho mu Israeli.”

26Davide anafunsa anthu amene anayima pafupi naye kuti, “Kodi adzamuchita chiyani munthu amene adzapha Mfilisiti uyu ndi kuchotsa chitonzo pakati pa Israeli? Mfilisiti wosachita mdulidweyu ndi ndani kuti azinyoza gulu lankhondo la Mulungu wamoyo?”

27Anthu anamuwuzanso zonse zimene mfumu inanena kuti idzachitira munthu amene adzapha Mfilisitiyo.

28Eliabu, mkulu wake wa Davide, atamumva akuyankhula ndi anthuwo, anamukwiyira ndipo anamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabwera kuno? Ndipo wasiyira yani nkhosa zochepazo mʼchipululu? Ndikudziwa kuti ndiwe wodzikuza ndiponso woyipa mtima. Unabwera kuno kuti udzaonere nkhondo.”

29Davide anati, “Kodi ndachita chiyani ine? Kodi ndisamayankhule?” 30Ndipo anamuchokera napita kwa munthu wina ndipo anamufunsa nkhani yomweyo, ndipo anthu anamuyankha iye monga poyamba paja. 31Mawu amene Davide anayankhula atamveka, anthu anakafotokozera Sauli ndipo Sauli anamuyitanitsa.

32Davide anati kwa Sauli, “Munthu aliyense asataye mtima chifukwa cha Mfilisitiyu. Ine kapolo wanu ndipita kukamenyana naye.”

33Sauli anayankha Davide kuti, “Iwe sungathe kupita kukamenyana ndi Mfilisitiyu. Iwe ukanali mnyamata, koma iyeyu ndi amene wakhala akumenya nkhondo kuyambira unyamata wake.”

34Koma Davide anati kwa Sauli, “Kapolo wanune ndinkaweta nkhosa za abambo anga. Ndipo mkango kapena chimbalangondo chikamabwera ndi kugwira mwana wankhosa pakati pa nkhosazo, 35ine ndinkatsatira ndi kupha chirombocho. Choncho ndinkapulumutsa mwana wankhosa uja mʼkamwa mwake. Ndipo chinkati chikandiwukira, ine ndinkagwira tchowa lake, nʼkuchikantha mpaka kuchipha. 36Ine kapolo wanu ndinapha mkango ngakhalenso chimbalangondo. Tsono Mfilisiti wosachita mdulidweyu adzaphedwa monga zinazo chifukwa wanyoza ankhondo a Mulungu wamoyo. 37Yehova amene anandilanditsa mʼkamwa mwa mkango ndi chimbalangondo adzandilanditsa mʼmanja mwa Mfilisiti uyu.”

Sauli anati kwa Davide, “Pita, ndipo Yehova akhale nawe.”

38Ndipo Sauli anamveka Davide mwinjiro wake. Anamuveka zovala zankhondo ndi chipewa cha mkuwa. 39Davide anamangirira lupanga pa mwinjirowo. Atayesa kuyenda nazo, analephera chifukwa anali asanazizolowere.

Iye anati kwa Sauli, “Sindingathe kuyenda nazo chifukwa sindinazizolowere.” Ndipo anazivula. 40Pambuyo pake anatenga ndodo yake mʼmanja. Kenaka anasankha miyala yosalala bwino mu mtsinje ndi kuyiika mʼthumba lake la ku ubusa. Legeni ili mʼmanja mwake, Davide ananyamuka kukakumana ndi Mfilisiti uja.

41Tsono Mfilisiti uja anayambapo kupita kumene kunali Davide, mnyamata wonyamula zida zake za nkhondo ali patsogolo pake. 42Mfilisitiyo atangomuona Davide, anamunyoza popeza kuti Davide anali mnyamata chabe wofiirira ndi wa maonekedwe abwino. 43Iye anati kwa Davide, “Kodi ndine galu, kuti ubwere kwa ine ndi ndodo?” Ndipo Mfilisitiyo anamutemberera Davide potchula mayina a milungu yake. 44Iye anatinso, “Bwera kuno ndipo ndidzapereka mnofu wako kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa zirombo zakuthengo!”

45Koma Davide anati kwa Mfilisitiyo, “Iwe wabwera kwa ine ndi lupanga, mkondo ndi nthungo, koma ine ndikubwera kwa iwe mʼdzina la Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa ankhondo Aisraeli amene iwe ukuwanyoza. 46Anatinso lero lino Yehova adzakupereka mʼmanja mwanga. Ndidzakukantha ndi kudula mutu wako. Ndidzapereka mitembo ya asilikali a Afilisti kwa mbalame za mlengalenga, ndi kwa zirombo zakuthengo ndipo dziko lonse lapansi lidzadziwa kuti mu Israeli muli Mulungu. 47Onse amene asonkhana pano adzadziwa kuti Mulungu sapulumutsa anthu ndi lupanga kapena mkondo, pakuti nkhondo ndi ya Yehova. Iye adzakuperekani mʼmanja mwathu.”

48Mfilisitiyo akusendera pafupi kuti akumane naye, Davideyo anathamangira mofulumira ku mzere wa nkhondo kukakumana naye. 49Davideyo anapisa dzanja lake mʼthumba lake natengamo mwala ndipo anawuponya, nalasa pa mphumi pa Mfilisitiyo. Mwalawo unalowa pa chipumi chake, ndipo anagwa chafufumimba.

50Kotero Davide anamupambana Mfilisitiyo pomugenda ndi mwala wa legeni ndi kumupha. Mʼmanja mwa Davide munalibe lupanga.

51Davide anathamanga nakayimirira pamwamba pa Mfilisiti uja. Anasolola lupanga lake lomwe moyikamo mwake, namupha pomudula mutu wake.

Afilisti ataona kuti ngwazi yawo yafa, anathawa. 52Ndipo Aisraeli ndi anthu a ku Yuda ananyamuka, ndipo akufuwula anathamangitsa Afilisti aja mpaka ku Gati ndi ku zipata za Ekroni. Anthu akufa awo amagwa njira yonse ya ku Saaraimu mpaka ku Gati ndi ku Ekroni. 53Aisraeli anabwerako kothamangitsa Afilisti kuja ndipo anadzatenga zonse zimene zinali mʼmisasa ya Afilistiwo. 54Pambuyo pake Davide anatenga mutu wa Mfilisitiyo napita nawo ku Yerusalemu, koma anayika zida za Mfilisitiyo mu tenti yake.

55Sauli ataona Davide akupita kukakumana ndi Mfilisitiyo anafunsa Abineri, mkulu wa ankhondo kuti, “Abineri, kodi mnyamatayu ndi mwana wa yani?”

Abineri anayankha kuti, “Ndithu mfumu muli apa ine sindikumudziwa.”

56Mfumu inati, “Pita kafufuze kuti mnyamata ameneyu ndi mwana wa yani.”

57Davide atangobwerako kokapha Mfilisiti kuja, Abineri anamutenga nabwera naye kwa Sauli, mutu wa Mfilisiti uja uli mʼmanja mwake.

58Sauli anamufunsa, “Mnyamata iwe, kodi paja ndiwe mwana wayani?”

Davide anati, “Ndine mwana wa mtumiki wanu Yese wa ku Betelehemu.”