哥林多后书 6 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

哥林多后书 6:1-18

1身为上帝的同工,我们劝你们不要辜负祂的恩典。 2因为祂说:

“在悦纳的时候,

我应允了你;

在拯救的日子,

我帮助了你。”

看啊,现在正是悦纳的时候!看啊,现在正是拯救的日子!

上帝仆人的品格

3为了避免有人毁谤我们的职分,我们凡事尽量不妨碍别人, 4反倒在任何事上都显明自己是上帝的仆人。不论遭遇什么患难、艰苦、贫穷、 5鞭打、囚禁、暴乱、辛劳、无眠或饥饿,我们都坚忍到底, 6靠着纯洁、知识、忍耐、仁慈、圣灵的感动、无伪的爱心、 7真理之道、上帝的大能、左右手中的公义兵器, 8无论是得荣耀还是受羞辱,遭毁谤还是得称赞,都显明自己是上帝的仆人。我们被视为骗子,却是诚实无伪; 9似乎默默无闻,却是家喻户晓;似乎快死了,看啊!我们却仍然活着;受严刑拷打,却没有丧命; 10似乎郁郁寡欢,却常常喜乐;似乎一贫如洗,却使多人富足;似乎一无所有,却样样都有!

11哥林多人啊!我们对你们推心置腹,开诚布公, 12毫无保留,只是你们自己心胸太窄。 13现在请你们也向我们敞开心怀。我这样说,是把你们当成自己的儿女。

永活上帝的殿

14不要和非信徒同负一轭,因为公义和不法怎能合作呢?光明和黑暗怎能共存呢? 15基督与魔鬼6:15 魔鬼”希腊文是“彼列”。怎能相容呢?信徒与非信徒有什么相干呢? 16上帝的殿与偶像怎能相提并论呢?因为我们就是永活上帝的殿,正如上帝说:

“我要住在他们中间,

在他们当中往来;

我要做他们的上帝,

他们要做我的子民。”

17又说:

“所以,你们要从他们中间出来,

离开他们,不要沾染污秽之物,

我就接纳你们。

18我要做你们的父亲,

你们要做我的儿女。

这是全能的主说的。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 6:1-18

1Pogwira naye ntchito pamodzi, tikukudandaulirani kuti musangolandira chisomo cha Mulungu pachabe. 2Pakuti akunena kuti,

“Pa nthawi yanga yabwino yokomera anthu mtima ndinakumvera,

ndipo pa nthawi yopulumutsa ndinakuthandiza.

Taonani, ndikukuwuzani kuti, ino ndiyo nthawi yabwino ya Ambuye, lero ndiye tsiku la chipulumutso.”

Masautso a Paulo

3Ife sitikuyika chokhumudwitsa pa njira ya wina aliyense, kuti utumiki wathu usanyozeke. 4Mʼmalo mwake, mwanjira iliyonse timasonyeza kuti ndife atumiki a Mulungu popirira kwambiri mʼmasautso, mʼzowawa ndi mʼzodetsa nkhawa. 5Pomenyedwa, kuponyedwa mʼndende ndi mʼzipolowe. Pogwira ntchito mwamphamvu, posagona usiku onse, posowa chakudya; 6pokhala moyo woyera mtima, pomvetsa zinthu, wokoma mtima ndi wachifundo mwa Mzimu Woyera ndi mwachikondi choonadi 7ndi poyankhula choonadi mwamphamvu ya Mulungu. Zida zimene zili mʼdzanja lamanja ndi lamanzere ndizo chilungamo. 8Timatumikira Mulungu ngakhale ena amatinyoza ndi ena amatilemekeza, ena amatinenera chipongwe, enanso amatiyamikira. Ena amatitenga kukhala ngati onena zoona, ndipo enanso amatitenga kukhala ngati onena zabodza. 9Amatiyesa osadziwika komatu ndife odziwika kwambiri. Amatiyesa wooneka ngati tikufa, koma tikupitirirabe ndi moyo, okanthidwa, koma osaphedwa. 10Amatiyesa achisoni, koma ndife achimwemwe nthawi zonse, aumphawi, koma olemeretsa ambiri; wopanda kanthu, koma tili ndi zonse.

11Tayankhula momasuka kwa inu, Akorinto, ndipo tanena zonse za kumtima kwathu. 12Ife sitikukubisirani chikondi chathu pa inu, koma inu mukubisa chikondi chanu pa ife. 13Pofuna kufanana zochita ndi kuyankhula monga kwa ana anga, nanunso muzinena za kukhosi kwanu.

Kukhala Pamodzi ndi Osakhulupirira

14Musamasenze goli pamodzi ndi osakhulupirira. Kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kulungama ndi kusalungama? Kapena kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kuwala ndi mdima? 15Pali mgwirizano wanji pakati pa Khristu ndi Beliyali? Kapena munthu wokhulupirira angayanjane bwanji ndi munthu wosakhulupirira? 16Pali mgwirizano wanji pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi nyumba ya mafano? Popezatu ndife Nyumba ya Mulungu wamoyo. Monga Mulungu wanena kuti,

“Ndidzakhala mwa iwo

ndipo ndidzayendayenda pakati pawo,

ndipo ndidzakhala Mulungu wawo,

ndipo adzakhala anthu anga.”

17Nʼchifukwa chake

“Tulukani pakati pawo

ndi kudzipatula,

akutero Ambuye.

Musakhudze chodetsedwa chilichonse,

ndipo ndidzakulandirani.”

18Ndipo

“Ndidzakhala Atate anu,

ndipo inu mudzakhala ana anga aamuna ndi aakazi,

akutero Ambuye, Wamphamvuzonse.”