哥林多后书 5 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

哥林多后书 5:1-21

天上的房屋

1我们知道,我们的身体好比是地上的帐篷,如果毁坏了,我们就从上帝那里得到一个住处,不是人手造的,而是天上永恒的“房屋”。 2我们在这地上的“帐篷”里叹息,渴望早日迁进那天上的“房屋”,好像更换衣服一样。 3我们一旦穿上新衣,就不会赤身露体了。 4我们在这“帐篷”里劳苦叹息,并非想脱去这地上的身体,而是切望能穿上那天上的新身体,让永恒的生命吞灭必朽的身体。 5是上帝为此目的预备了我们,并赐给了我们圣灵作担保。

6所以,我们总是坦然无惧,尽管知道住在肉身之内便无法与主在一起。 7因为我们行事为人,是凭对上帝的信心,不是凭眼见。 8是的,我们坦然无惧,甚至更乐意离开身体,回到天家与主相聚。 9因此,我们立定心志,无论是住在肉身之内还是离开肉身,都要取悦主。 10因为我们所有的人都要出现在基督的审判台前,好按照各人在肉身之时所行的善恶接受赏罚。

劝人与上帝和好

11我们知道主是当受敬畏的,所以劝人归信祂。我们的内心如何,上帝知道,我盼望你们的良心也知道。 12我们不是称赞自己,而是让你们有机会以我们为荣,叫你们可以反驳那些只贪图外表虚荣、不注重内在实质的人。 13如果我们疯狂,那是为了上帝;如果我们清醒,那是为了你们。 14因为基督的爱激励我们,因为我们确信:基督一人既代替所有的人死了,所有的人就都死了。 15祂为众人死,是要叫那些活着的人不再为自己活,而是要为替他们死而复活的基督活。

16从今以后,我们不再以貌取人了,虽然我们曾这样看待基督,现在却不再这样看待祂了。 17若有人在基督里,他就是新造的人,旧事已过,看啊,一切都更新了。 18这一切都是上帝的作为,祂借着基督使我们与祂和好,又把劝人与祂和好的职分赐给了我们。 19也就是说,上帝在基督里使世人与自己和好,不再追究他们的过犯。祂已托付我们去传扬这和好之道。 20所以我们现在是基督的大使,可以说上帝正借着我们发出呼求。我们替基督恳求你们:要与上帝和好! 21上帝使无罪的基督担当我们的罪,使我们可以借着基督成为被上帝接纳的义人。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 5:1-21

Matupi Atsopano

1Popeza tikudziwa kuti ngati msasa wa dziko lapansi umene tikukhalamo uwonongeka, tili ndi nyumba yochokera kwa Mulungu, nyumba yamuyaya yakumwamba, osati yomangidwa ndi manja a anthu. 2Pakali pano tibuwula, ndi kulakalaka kuvala nyumba yathu ya kumwambayo, 3chifukwa tikavala, sitidzapezekanso amaliseche. 4Pamene tili mu msasa uno, timalemedwa ndipo timabuwula, chifukwa sitifuna kukhala amaliseche koma ovala nyumba yathu ya kumwamba, kuti chimene chili chakufa chimezedwe ndi moyo. 5Tsono ndi Mulungu amene anatikonzeratu ife kuti tilandire zimenezi. Iye anatipatsa Mzimu ngati chikole, kutsimikizira zimene zikubwera.

6Nʼchifukwa chake nthawi zonse timalimba mtima, ndipo timadziwa kuti pamene tikukhala mʼthupi, ndiye kuti tili kutali ndi Ambuye. 7Ife timakhala mwachikhulupiriro, osati mwa zooneka ndi maso. 8Inde, ife tikulimba mtima, ndipo tikanakonda kulekana nalo thupi lathu ndi kukhala ndi Ambuye. 9Choncho timayesetsa kukondweretsa Ambuye, ngakhale tikhale mʼthupi, kapena tichokemo. 10Pakuti tonsefe tiyenera kukaonekera pa mpando woweruza wa Khristu, kuti aliyense wa ife akalandire zomuyenera molingana ndi zimene anachita ali mʼthupi; zabwino kapena zoyipa.

Ntchito Yoyanjanitsa

11Tsono popeza tikudziwa tanthauzo la kuopa Ambuye, ife timayesetsa kukopa anthu. Mulungu amatidziwa bwino lomwe, ndipo tikukhulupirira kuti inunso mumatidziwa bwino mʼmitima mwanu. 12Sitikudzichitiranso tokha umboni kwa inu, koma tikukupatsani mwayi oti muzitinyadira. Tikufuna kuti muwayankhe amene amanyadira zinthu zooneka ndi maso osati zimene zili mu mtima. 13Ngati ndife amisala, monga amanenera ena, nʼchifukwa chofuna kuti Mulungu alemekezedwe. Ngati si ife amisala, nʼkuti inu muthandizike. 14Pakuti chikondi cha Khristu ndicho chimatikakamiza, chifukwa tikutsimikiza kuti mmodzi anafera anthu onse, kotero kuti anthu onse anafanso. 15Ndipo Iye anafera anthu onse kuti amene ali ndi moyo, asakhale ndi moyo wofuna kudzikondweretsa okha, koma azikondweretsa amene anawafera naukitsidwa chifukwa cha iwowo.

16Choncho, kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ife sitiganizirapo za munthu aliyense monga mwanzeru za umunthu, ngakhale kuti poyamba tinkaganiza za Khristu mʼnjira imeneyi, koma tsopano sititeronso. 17Nʼchifukwa chake, ngati munthu aliyense ali mwa Khristu, ndi wolengedwa kwatsopano; zinthu zakale zapita taonani, zakhala zatsopano. 18Zonsezi zichokera kwa Mulungu amene anatiyanjanitsa ndi Iye mwini kudzera mwa Khristu ndipo anatipatsa ife utumiki wa chiyanjanitso. 19Mulungu ankayanjanitsa dziko lapansi kwa Iye mwini kudzera mwa Khristu, osawerengera anthu monga mwa zochimwa zawo. Ndipo watisungitsa ife uthenga uwu wa chiyanjanitso. 20Choncho ife ndi akazembe a Khristu, monga ngati Mulungu akudandaulira anthu kudzera mwa ife. Ife tikukupemphani inu mʼmalo mwa Khristu kuti, yanjanitsidwani ndi Mulungu. 21Chifukwa cha ife, Mulungu anasandutsa wopanda tchimoyo kukhala tchimo, kuti mwa Iye ife tikakhale chilungamo cha Mulungu.