启示录 3 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

启示录 3:1-22

给撒狄教会的信

1“你要写信告诉撒狄教会的天使,有上帝的七灵又有七颗星的主说,

‘我知道你的行为,你名义上活着,实际上是死的。 2你要警醒!把所剩无几、奄奄一息的生命振作起来,因为我发现你的行为在我的上帝面前不纯全。 3因此,要回想你以前所领受、所听见的教导,遵守这些教导,并且悔改。你若不警醒,我必在你意想不到的时候像贼一样忽然来到。 4不过在撒狄,你还有几个人未曾玷污自己的衣服,他们要穿白袍与我同行,因为他们配得这样。 5得胜者必同样穿上白袍,我绝不会从生命册上抹去他的名字,我必在我父和众天使面前承认他的名。

6‘圣灵对各教会所说的话,凡有耳朵的都应当听。’

给非拉铁非教会的信

7“你要写信告诉非拉铁非教会的天使,那位圣洁、真实、拿着大卫的钥匙、开了门无人能关、关了门无人能开的主说,

8‘我知道你的行为,你力量微小,却遵守了我的教导,没有背弃我的名。所以,看啊!我在你面前为你打开了一扇无人能关闭的门。 9看啊!我要使撒旦的同伙,就是那些假冒犹太人的说谎者,在你面前俯伏下拜,让他们知道你是我所疼爱的。 10因为你遵守我有关坚忍的教导,所以当将来的试炼临到全人类的时候,我必使你免受磨难。 11我很快就要来了!你要持守你所拥有的,免得有人夺去你的冠冕。 12我要使得胜者在我上帝的殿中作栋梁,永不离开。我要将我上帝的名号和我上帝圣城的名号,就是从天上我上帝那里降下来的新耶路撒冷和我自己的新名号,都刻在他上面。

13‘圣灵对各教会所说的话,凡有耳朵的都应当听。’

给老底嘉教会的信

14“你要写信告诉老底嘉教会的天使,那位实实在在3:14 那位实实在在”希腊文是“那位阿们的”。、诚信无伪的见证人,就是上帝所造万物的元首说,

15‘我知道你的行为,你不冷也不热。我情愿你或冷或热, 16可是现在你却像温水一样不冷不热,我必将你从我口中吐出去! 17你说,我很富有,已经发了财,什么都不缺。你却不知道自己困苦、可怜、贫穷、瞎眼、赤身露体。 18我劝你向我买精炼的金子,使你真正富有。你也要向我买白袍穿在身上,好遮盖你赤身露体的羞辱。你也要向我买眼药抹眼睛,使你能看见。 19凡我所爱的,我都会责备、管教。因此,你要热心起来,也要悔改。 20看啊!我站在门外敲门,若有谁闻声开门,我必进去,我与他,他与我,一同坐席吃饭。 21得胜者可以和我一同坐在我的宝座上,正如我得胜后与我父一同坐在祂的宝座上一样。

22‘圣灵对各教会所说的话,凡有耳朵的都应当听。’”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 3:1-22

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Sarde

1“Lembera mngelo wampingo wa ku Sarde kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa amene amasunga mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri. Iye akuti: Ndimadziwa ntchito zako; umadziwika kuti ndiwe wamoyo koma ndiwe wakufa. 2Dzuka! Limbitsa zimene zatsalira zomwe zatsala pangʼono kufa, pakuti ndaona kuti ntchito zako nʼzosakwanira pamaso pa Mulungu. 3Choncho, kumbukira zimene unalandira ndi kumva; uzisunge ndipo ulape. Koma ngati sudzuka, ndidzabwera ngati mbala ndipo sudzadziwa nthawi imene ndidzabwere kwanu.

4Komabe uli ndi anthu angapo mu Sarde amene sanadetse zovala zawo. Amenewa adzayenda ndi Ine atavala zoyera popeza ndi oyenera kutero. 5Amene adzapambane adzavala zoyera ngati ena aja. Sindidzafafaniza dzina lake mʼbuku lamoyo, koma ndidzamuchitira umboni pamaso pa Atate anga ndi angelo ake. 6Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.”

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Filadefiya

7“Lembera mngelo wampingo wa ku Filadefiya kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa amene ndi woyera ndi woonadi, amene ali ndi kiyi ya Davide. Iye akatsekula palibe amene angatseke; ndipo akatseka palibe amene angatsekule. 8Iye akuti, ‘Ine ndimadziwa ntchito zako. Taona, ndakutsekulira pa khomo ndipo palibe wina amene angatseke. Ndikudziwa kuti uli ndi mphamvu zochepa komabe wasunga mawu anga ndipo sunandikane. 9Amene ndi mpingo wa Satana, amene amadzitcha kuti ndi Ayuda pamene sali choncho, koma ndi onama, ndidzawabweretsa kwa inu ndi kuwagwetsa pansi pa mapazi anu kuti adzazindikire kuti ndimakukondani. 10Popeza mwasunga mawu anga woti mupirire ndipo mwawugwira mtima, Inenso ndidzakupulumutsani nthawi ya mayesero imene idzabwera pa dziko lonse lapansi kuyesa onse okhala pa dziko lapansi.

11Ine ndikubwera msanga. Gwiritsitsa chimene uli nacho kuti wina angakulande chipewa chako chaufumu. 12Iye amene adzapambane ndidzamusandutsa mzati wa mʼNyumba ya Mulungu wanga. Sadzatulukamonso. Pa iye ndidzalemba dzina la Mulungu wanga ndi dzina la mzinda wa Mulungu wanga, Yerusalemu watsopano, umene ukubwera pansi kuchokera kumwamba kwa Mulungu wanga; ndipo pa iye ndidzalembanso dzina langa latsopano. 13Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.’ ”

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Laodikaya

14“Lembera mngelo wampingo wa ku Laodikaya kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa Ameni, mboni yokhulupirika ndi yoona, gwero la zolengedwa zonse za Mulungu. 15Ine ndimadziwa ntchito zako, kuti sindiwe wozizira kapena wotentha. Ndikanakonda ukanakhala wozizira kapena wotentha! 16Tsono popeza ndiwe wofunda chabe, sindiwe wotentha kapena wozizira, ndatsala pangʼono kuti ndikulavule mʼkamwa mwanga. 17Iwe umati: ‘Ndine wolemera, ndine wachuma ndipo sindisowa kanthu.’ Koma sudziwa kuti ndiwe wovutika, womvetsa chisoni, waumphawi, wosaona ndi wamaliseche. 18Ndikukulangiza kuti ugule kwa Ine golide woyengedwa ndi moto kuti ukhale wolemera. Ugule zovala zoyera kuti uvale ndi kuphimba umaliseche wako wochititsa manyaziwo. Ndiponso ugule kwa Ine mankhwala a mʼmaso kuti uwone.

19Amene ndimawakonda ndimawadzudzula ndi kuwalanga. Choncho chita changu ndipo lapa. 20Taonani ndayima pa khomo ndikugogoda. Ngati wina amva mawu anga natsekula chitseko, Ine ndidzalowamo ndi kudya naye, Ine ndi iyeyo.

21Amene adzapambana, ndidzamupatsa ufulu wokhala nane pamodzi pa mpando wanga waufumu monga mmene Ine ndinapambana ndi kukhala pansi ndi Atate anga pa mpando wawo waufumu. 22Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.”