启示录 14 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

启示录 14:1-20

天上的新歌

1我看到羔羊站在锡安山上,与祂在一起的有十四万四千人,他们额上都有祂和祂父的名字。 2我听见有声音从天上传来,像江河澎湃,像雷霆万钧,又像竖琴合奏的声音。 3他们在宝座前,在四个活物和二十四位长老面前唱一首新歌。除了从地上被赎出来的十四万四千人以外,没有人能学得会这歌。 4这些人从未沾染过妇女,都是童身。无论羔羊往哪里去,他们都紧随其后。他们是从世人中被赎出来的,作为初熟的果实献给上帝和羔羊。 5他们从未说谎,纯洁无瑕。

三位天使的信息

6我看见另一位天使在空中飞翔,要将永远的福音传给地上的各国家、各部落、各语言族群、各民族。 7他大声说:“当敬畏上帝,归荣耀给祂,因为祂审判的时候到了。要敬拜造天、地、海和一切水源的那位。”

8接着又一位天使说:“巴比伦大城倒塌了!倒塌了!她曾引诱万民喝她那淫乱的烈酒。”

9之后,第三位天使高喊:“一切敬拜怪兽和它的像、在手或额上接受兽印的, 10都要喝上帝震怒的烈酒,就是祂怒杯里毫无掺杂的烈酒。他们要在圣天使和羔羊面前,在火和硫磺中受煎熬。 11他们受煎熬所发出的烟不断上升,永无休止。那些拜兽、兽像和接受了兽名印记的人昼夜不得安宁。” 12但持守上帝诫命和耶稣真道的圣徒们需要坚忍。

13我听见天上有声音说:“你将下面的话写下来,从今以后,那些为主而死的人有福了!”

圣灵说:“是的!他们将得享安息,不再劳苦。他们工作的成果必随着他们。”

地上的收割

14我再观看,见有一朵白云,上面坐着的好像是人子,祂头戴金冠,手拿锋利的镰刀。 15有一位天使从殿中出来,扬声向坐在云上的那位说:“挥动你的镰刀收割吧!地上的庄稼已经熟透了,可以收割了。” 16于是,坐在云上的那位便向大地挥动镰刀,把地上的庄稼都收割了。

17另一位天使手里也拿着锋利的镰刀从天上的殿中出来。 18又有一位掌管烈火的天使从祭坛那里出来,对手拿镰刀的天使高喊:“挥动你锋利的镰刀,收取地上葡萄树的果实吧!它们已经熟透了。” 19于是,那天使挥动镰刀,收取了地上的葡萄,抛到上帝烈怒的大榨酒池中。 20葡萄在城外的榨酒池中被踩踏,血从榨酒池中涌出,高至马的嚼环,流了三百公里14:20 三百公里”希腊文是“一千六百司他町”。远。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 14:1-20

Mwana Wankhosa ndi Anthu 144,000

1Kenaka ndinaona patsogolo panga panali Mwana Wankhosa, atayimirira pa Phiri la Ziyoni, ndipo Iye anali pamodzi ndi anthu 144,000 amene pa mphumi pawo panalembedwa dzina la Mwana Wankhosayo ndi la Atate ake. 2Ndipo ndinamva liwu lochokera kumwamba ngati mkokomo wa madzi ambiri, ndiponso ngati kugunda kwamphamvu kwa bingu. Liwu limene ndinamvalo linali ngati a anthu akuyimba azeze awo. 3Anthuwo ankayimba nyimbo yatsopano patsogolo pa mpando waufumu ndi zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu aja. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatha kuphunzira nyimboyo kupatula anthu 144,000 aja amene anawomboledwa pa dziko lapansi. 4Awa ndiwo amene sanadzidetse koma anadzisunga ndipo sanadziyipitse ndi akazi. Anthu amenewa ndiwo ankatsatira Mwana Wankhosa kulikonse kumene ankapita. Ndiwo amene anagulidwa pakati pa anthu a dziko lapansi kuti akhale oyambirira kuperekedwa kwa Mulungu ndi kwa Mwana Wankhosa. 5Iwo sananenepo bodza ndipo alibe cholakwa.

Angelo Atatu

6Kenaka ndinaona mngelo wina akuwuluka mu mlengalenga ndipo anali ndi Uthenga Wabwino wamuyaya woti akalalikire kwa anthu okhala pa dziko lapansi, kwa a mtundu uliwonse, a fuko lililonse, a chiyankhulo chilichonse ndi kwa anthu onse. 7Mngeloyo anayankhula mokweza mawu kuti, “Wopani Mulungu ndi kumutamanda, chifukwa nthawi yoweruza anthu yafika. Mumupembedze Iye amene analenga thambo, dziko lapansi, nyanja ndi akasupe amadzi.”

8Mngelo wachiwiri anatsatana naye ndipo anati, “Wagwa! Wagwa Babuloni womveka uja, amene anachititsa anthu a mitundu yonse kumwa vinyo wa zilakolako zake zachigololo.”

9Mngelo wachitatu anatsatana nawo ndi mawu ofuwula anati, “Ngati wina apembedza chirombo chija ndi fano lake ndi kulembedwa chizindikiro pa mphumi kapena pa dzanja, 10nayenso adzamwa vinyo waukali wa Mulungu, umene wathiridwa popanda kuchepetsa mphamvu zake mʼchikho cha ukali wa Mulungu. Munthuyo adzazunzidwa ndi moto wamiyala yasulufure pamaso pa angelo oyera ndi pa Mwana Wankhosa. 11Ndipo utsi wa moto wowazunzawo udzakwera kumwamba mpaka muyaya. Sikudzakhala kupumula usana ndi usiku kwa amene anapembedza chirombo chija ndi fano lake kapena kwa aliyense amene analembedwa chizindikiro cha dzina lake lija.” 12Pamenepa ndi pofunika kupirira kwa anthu oyera mtima amene amasunga malamulo a Mulungu ndi kukhalabe okhulupirika kwa Yesu.

13Kenaka ndinamva mawu kuchokera kumwamba akuti, “Lemba kuti, Odala anthu amene akufa ali mwa Ambuye kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo.”

“Inde,” akutero Mzimu, “akapumule ntchito zawo zotopetsa pakuti ntchito zawo zidzawatsata.”

Zokolola za Dziko la Pansi

14Ndinayangʼana patsogolo panga ndinaona mtambo woyera patakhalapo wina ngati Mwana wa Munthu, kumutu atavala chipewa chaufumu chagolide ndipo mʼdzanja mwake munali chikwakwa chakunthwa. 15Tsono mngelo wina anatuluka mʼNyumba ya Mulungu nafuwula mwamphamvu kwa uja wokhala pa mtamboyu. Mngeloyo anati, “Tenga chikwakwa chako ndipo kolola, pakuti nthawi yokolola ya dziko la pansi yakwana” 16Choncho wokhala pa mtambo uja anayamba kukolola dzinthu pa dziko lapansi ndi chikwakwa chakecho.

17Mngelo wina anatuluka mʼNyumba ya Mulungu kumwamba ndipo nayenso anali ndi chikwakwa chakunthwa. 18Kenaka mngelo winanso amene amalamulira moto, anatuluka kuchokera ku guwa lansembe nayitana mwamphamvu mngelo uja amene anali ndi chikwakwa chakunthwa chija, nati, “Tenga chikwakwa chako chakunthwacho yamba kudula mphesa za mʼmunda wamphesa wa pa dziko lapansi, pakuti mphesa zapsa kale.” 19Pamenepo mngeloyo anayambadi kugwiritsa ntchito chikwakwa chake nadula mphesa za dziko lapansi, naziponya mʼchopondera mphesa chachikulu cha ukali woopsa wa Mulungu. 20Mphesazo zinapondedwa mʼchopondera mphesa kunja kwa mzinda. Mʼchopondera mphesamo munatuluka magazi amene anayenderera ngati mtsinje, kuzama kwake mita ndi theka ndipo kutalika kwake makilomita 300.