历代志上 5 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

历代志上 5:1-26

吕便的后裔

1以色列的长子原是吕便,但因为他玷污了父亲的床5:1 指跟父亲的妾通奸一事,参见创世记35:22,他长子的名分就给了他弟弟约瑟的后代。因此,按家谱他不是长子。 2犹大虽然在众弟兄中最强大,君王也是出自他的后裔,长子的名分却属于约瑟3以色列长子吕便的儿子是哈诺法路希斯伦迦米4约珥的儿子是示玛雅示玛雅的儿子是歌革歌革的儿子是示每5示每的儿子是米迦米迦的儿子是利·亚雅利·亚雅的儿子是巴力6巴力的儿子是备·拉备·拉吕便支派的首领,被亚述提革拉·毗尼色掳去。 7按家谱记载,他做族长的亲族是耶利撒迦利雅比拉8比拉亚撒的儿子,亚撒示玛的儿子,示玛约珥的儿子。约珥住在亚罗珥尼波巴力·免一带。 9他们的牲畜在基列繁殖众多,便又向东迁移到幼发拉底河西边的旷野。 10扫罗执政期间,吕便人与夏甲人交战,打败了夏甲人,占领了基列东边的整片土地。

迦得的后裔

11迦得的后代住在毗邻吕便支派的巴珊,向东远至撒迦12巴珊做首领的有族长约珥、副族长沙番以及雅乃沙法13他们同族的弟兄有米迦勒米书兰示巴约赖雅干细亚希伯,共七人。 14这些都是亚比孩的儿子。亚比孩户利的儿子,户利耶罗亚的儿子,耶罗亚基列的儿子,基列米迦勒的儿子,米迦勒耶示筛的儿子,耶示筛耶哈多的儿子,耶哈多布斯的儿子。 15古尼的孙子、押比碟的儿子亚希是他们家族的族长。 16他们住在基列巴珊巴珊附近的乡村以及沙仑所有的草原,直到四围的边界地带。 17这些人是在犹大约坦以色列耶罗波安执政期间被记录在族谱里的。

18吕便支派、迦得支派和玛拿西半个支派中善用盾牌、刀剑、弓箭、能征善战的勇士共有四万四千七百六十人。 19他们与夏甲人、伊突人、拿非施人和挪答人打仗, 20击败了夏甲人及其盟军,因为他们信靠上帝,在作战的时候向上帝求助,上帝应允了他们的祈求。 21他们从敌人那里掳走了五万只骆驼、二十五万只羊、两千头驴和十万人口。 22敌人伤亡惨重,因为他们有上帝的帮助。他们占据敌人的土地,一直到被掳的时候。

玛拿西的半个支派

23玛拿西半个支派的人住在从巴珊巴力·黑们示尼珥黑门山一带。 24他们的族长以弗以示以列亚斯列耶利米何达威雅雅叠都是英勇的战士,是著名的人物和各家族的首领。

25可是,他们却背弃他们祖先的上帝,与当地居民的神明苟合。上帝曾在他们面前毁灭那些居民。 26因此,以色列的上帝驱使亚述普勒,即提革拉·毗尼色,把吕便人、迦得人、玛拿西半个支派的人掳到哈腊哈博哈拉歌散河边,他们至今还在那里。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 5:1-26

Fuko la Rubeni

1Ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli (iye anali woyamba kubadwa, koma atagona ndi mkazi wamngʼono wa abambo ake, ulemu wake wokhala mwana woyamba unaperekedwa kwa ana a Yosefe. Kotero iye sanalembedwe pa mndandanda wa mayina ngati mwana woyamba kubadwa, 2ndipo ngakhalenso Yuda anali wamphamvu kwambiri pakati pa abale ake, ndi kuti wolamulira anachokera mwa iye, ulemu wa mwana woyamba kubadwa unaperekedwa kwa Yosefe) 3ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli ndi awa:

Hanoki, Palu, Hezironi, ndi Karimi.

4Ana a Yoweli anali awa:

Semaya, Gogi,

Simei, 5Mika,

Reaya, Baala,

6ndiponso Beeri, amene Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri anamugwira ukapolo. Mtsogoleri wa fuko la Rubeni anali Beeri.

7Abale awo mwa mabanja awo, potsata mndandanda wa mʼbado wawo, ndi awa:

Yeiyeli, mtsogoleri, Zekariya, 8ndiponso Bela mwana wa Azazi, mwana wa Sema, mwana wa Yoweli. Iwo ankakhala ku Aroeri mpaka ku Nebo ndi Baala-Meoni. 9Iwo anakhala cha kummawa mpaka kukafika polowera mʼchipululu cha mbali ina ya Mtsinje wa Yufurate, chifukwa ziweto zawo zinaswana kwambiri mʼdziko la Giliyadi.

10Pa nthawi ya Sauli anachita nkhondo ndi Ahagiri ndi kuwagonjetsa. Tsono iwo anakhala mʼmatenti a Ahagiri ku dera lonse la kummawa kwa Giliyadi.

Fuko la Gadi

11Anthu a fuko la Gadi anakhala moyandikana ndi fuko la Rubeni ku Basani mpaka ku Saleka:

12Mtsogoleri wawo ku Basani anali Yoweli, wachiwiri anali Safamu, kenaka Yanayi ndi Safati.

13Abale awo mwa mabanja awo anali awa:

Mikayeli, Mesulamu, Seba, Yorayi, Yakani, Ziya ndi Eberi, onse ali asanu ndi awiri.

14Amenewa ndiwo anali ana a Abihaili, mwana wa Huri, mwana wa Yarowa, mwana wa Giliyadi, mwana wa Mikayeli, mwana wa Yesisayi, mwana wa Yahido, mwana wa Buzi.

15Ahi mwana wa Abdieli, mwana wa Guni, anali mtsogoleri wa banja la makolo awo.

16Fuko la Gadi linakhala ku Giliyadi, ku Basani ndi midzi yozugulira, madera onse a msipu a ku Saroni mpaka kumene amalekezera.

17Mayina onsewa analembedwa potsata mndandanda wa mibado yawo pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu mfumu ya Yuda ndi Yeroboamu mfumu ya Israeli.

18Mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la Manase, anali ndi anthu 44, 760 okonzeka kulowa usilikali; anthu amatupi amphamvu, amene amatha kugwiritsa ntchito chishango ndi lupanga, amene amatha kugwiritsa ntchito uta, amene anaphunzitsidwa kumenya nkhondo. 19Iwo anachita nkhondo ndi Ahagiri, Yeturi, Nafisi ndi Nodabu. 20Iwowo anathandizidwa polimbana nawo ndipo Mulungu anapereka Ahagiri mʼmanja mwawo; popeza iwo anafuwulira kwa Mulungu pa nkhondopo. Iye anayankha mapemphero awo chifukwa anamudalira. 21Choncho iwo analanda ziweto za Ahagiri: ngamira 50,000, nkhosa ndi mbuzi 250,000 ndi abulu 2,000. Ndiponso anagwira akapolo 100,000, 22enanso ambiri anaphedwa, chifukwa nkhondoyo inali ya Mulungu. Ndipo iwo anakhala mʼdzikomo mpaka pa nthawi ya ukapolo.

Theka la Fuko la Manase

23Theka la fuko la Manase linkakhala ku dziko la kummawa kuyambira ku Basani mpaka ku Baala-Herimoni, kumene ndi ku Seniri (Phiri la Herimoni) ndipo anthuwo anali ochuluka kwambiri.

24Atsogoleri a mabanja awo anali awa: Eferi, Isi, Elieli, Azirieli, Yeremiya, Hodaviya ndi Yahidieli. Iwo anali asilikali olimba mtima, anthu otchuka, ndiponso atsogoleri a mabanja awo. 25Koma iwo anali osakhulupirika kwa Mulungu wa makolo awo ndipo anadzipereka okha kwa milungu ya anthu okhala mʼdzikomo amene Mulungu anawawononga pamene iwowo ankafika. 26Kotero Mulungu wa Israeli anayika mkwiyo mwa Puli mfumu ya Asuri (ameneyu ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri) amene anatenga fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase kupita nawo ku ukapolo. Iye anapita nawo ku Hala, Habori, Hara ndi ku mtsinje wa Gozani, kumene ali mpaka lero lino.