历代志上 24 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

历代志上 24:1-31

祭司的职务

1下面是亚伦子孙的班次。亚伦的儿子是拿答亚比户以利亚撒以他玛2拿答亚比户比父亲先死,而且没有留下儿子,因此以利亚撒以他玛做了祭司。 3以利亚撒的子孙撒督以他玛的子孙亚希米勒的协助下,大卫亚伦的子孙分成班次,让他们各司其职。 4以利亚撒的子孙中做首领的比以他玛的子孙中做首领的多,他们被分成班次,以利亚撒的子孙中有十六个族长,以他玛的子孙中有八个族长。 5因为以利亚撒的子孙中和以他玛的子孙中都有人在圣所做首领事奉上帝,他们便用抽签的方法公平地分班,分别在以利亚撒以他玛家族中抽签。 6利未拿坦业的儿子示玛雅是书记。他在君王、首领、撒督祭司、亚比亚他的儿子亚希米勒、众祭司和利未人的族长面前把抽出的名字记录下来。

7第一签抽出来的是耶何雅立,第二签是耶大雅8第三签是哈琳,第四签是梭琳9第五签是玛基雅,第六签是米雅民10第七签是哈歌斯,第八签是亚比雅11第九签是耶书亚,第十签是示迦尼12第十一签是以利亚实,第十二签是雅金13第十三签是胡巴,第十四签是耶是比押14第十五签是璧迦,第十六签是音麦15第十七签是希悉,第十八签是哈辟悉16第十九签是毗他希雅,第二十签是以西结17第二十一签是雅斤,第二十二签是迦末18第二十三签是第来雅,第二十四签是玛西亚19他们照这班次,按以色列的上帝耶和华借他们的祖先亚伦所定的条例,在耶和华的殿里司职。

20其他的利未人还有暗兰的后代书巴业书巴业的后裔耶希底亚21利哈比雅的长子伊示雅22以斯哈的后代示罗摩示罗摩的后代雅哈23希伯仑的长子耶利雅、次子亚玛利亚、三子雅哈悉、四子耶加缅24乌薛的后代米迦米迦的后代沙密25米迦的弟兄伊示雅伊示雅的后代撒迦利雅26米拉利的儿子抹利姆示雅西雅雅西雅的儿子比挪27米拉利的后代雅西雅的儿子比挪朔含撒刻伊比利28抹利的儿子以利亚撒——以利亚撒没有儿子, 29基士的后代耶拉篾30姆示的儿子末力以得耶利摩。这些按宗族都是利未人的后代。 31他们也在大卫王、撒督亚希米勒、众祭司和利未人的族长面前抽签,不分长幼,正如他们的亲族亚伦的后代所做的一样。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 24:1-31

Magulu a Ansembe

1Magulu a ana a Aaroni anali awa:

Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara. 2Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe. 3Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira. 4Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara. 5Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.

6Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.

7Maere woyamba anagwera Yehoyaribu,

achiwiri anagwera Yedaya,

8achitatu anagwera Harimu,

achinayi anagwera Seorimu,

9achisanu anagwera Malikiya,

achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,

10achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi,

achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,

11achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa,

a khumi anagwera Sekaniya,

12a 11 anagwera Eliyasibu,

a 12 anagwera Yakimu,

13a 13 anagwera Hupa,

a 14 anagwera Yesebeabu,

14a 15 anagwera Biliga,

a 16 anagwera Imeri,

15a 17 anagwera Heziri,

a 18 anagwera Hapizezi,

16a 19 anagwera Petahiya,

a 20 anagwera Ezekieli,

17a 21 anagwera Yakini,

a 22 anagwera Gamuli,

18a 23 anagwera Delaya,

ndipo a 24 anagwera Maaziya.

19Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.

Alevi Ena Onse

20Za zidzukulu zina zonse za Levi:

Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli;

kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.

21Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake:

Mtsogoleri anali Isiya.

22Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti;

kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.

23Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.

24Mwana wa Uzieli: Mika;

kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.

25Mʼbale wa Mika: Isiya;

kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.

26Ana a Merari: Mahili ndi Musi.

Mwana wa Yaaziya: Beno.

27Ana a Merari:

Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.

28Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.

29Kuchokera kwa Kisi:

Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.

30Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti.

Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo. 31Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.