利未记 25 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

利未记 25:1-55

安息年的条例

1耶和华在西奈山上对摩西说: 2“你把以下条例告诉以色列人。

“你们到了我将要赐给你们的土地后,要让土地每七年在耶和华面前休耕一年。 3六年之内,你们可以耕种田地,修整葡萄园,收获出产。 4但第七年是安息年,土地要休息,以尊崇耶和华。你们不可耕种,不可修整葡萄园。 5不可收割自生自长的庄稼,也不可摘未经修剪而结的葡萄。这一年土地要休耕。 6但安息年间土地里自生自长的,你们和你们的仆婢、雇工与住在你们中间的外族人都可以吃, 7你们的牲畜和境内的野兽也可以吃。

禧年的条例

8“你们要计算七个安息年,即七个七年,共四十九年。 9第五十年的七月十日赎罪日那天,你们要在境内各地吹号。 10你们要以这年为圣年,向境内所有居民宣告自由。这年将成为你们的禧年。各人要得回卖掉的祖业,卖身为奴的可以自由回家。 11第五十年是你们的禧年。这一年你们不可耕种,不可收割自生自长的庄稼,也不可摘未经修剪而结的葡萄。 12这是禧年,是你们的圣年,你们可以吃土地里自生自长的。 13在禧年,各人要得回卖掉的地业。 14因此,你们和同胞买卖田地时,不可彼此亏负。 15买卖双方要按照距下个禧年的年数多少定价。 16距下个禧年的年数多,价钱就高;年数少,价钱就低。因为卖的是田地收成的次数。 17要敬畏你们的上帝,不可彼此亏负。我是你们的上帝耶和华。 18你们要遵行我的律例,持守我的典章,就可以在那片土地上安居。 19土地会出产丰富,使你们丰衣足食、安然居住。 20你们可能会问,‘第七年不种不收,我们吃什么?’ 21我要在第六年赐福给你们,使田地的出产够你们吃三年。 22第八年开始耕种时,你们仍会吃陈粮,一直吃到第九年的收割季节。

赎回土地的条例

23“你们不可永远卖掉土地,因为土地是我的,你们只不过是寄居在那片土地上的过客。 24你们购买每一块土地时,都必须让原主保留赎回的权利。 25如果有人因贫穷而卖掉土地,他的近亲要把卖掉的土地赎回来。 26如果无人为他赎回,而他自己渐渐富裕起来,有能力赎回, 27他要计算卖掉土地的年数,退还距下个禧年所剩年数的地价,便可以赎回自己的土地。 28如果他没有能力赎回,所卖的土地在禧年之前要属于买主。到了禧年,买主必须把土地归还原主。

赎回房屋的条例

29“如果有人卖掉自己城里的房子,要保留一年赎回权。卖掉房子的一年之内,他可以赎回。 30如果一年之内他没有赎回,房子便永远归买主所有,就是到了禧年也不用归还。 31如果房子在四围无墙的乡村,要视房子为乡下的土地,原主可以赎回;到了禧年,买主必须将房子归还。 32利未人的城邑里,利未人有权随时赎回所卖的房子。 33如果他们没有赎回,到了禧年要把房子归还他们;因为在利未人的城里,利未人的房屋是他们在以色列人中所拥有的产业。 34但不可出卖利未人城郊的草场。那是他们永远拥有的产业。

照顾同胞的条例

35“如果你们的同胞生活日益贫穷,难以维生,你们要像照顾外族人和寄居者一样照顾他的生活,让他住在你们当中。 36你们不可从中谋利,要敬畏上帝,让他住在你们当中。 37你们借钱给他,不可收取利息;借粮给他,不可谋利。 38我是你们的上帝耶和华。我曾经带领你们离开埃及,为要把迦南赐给你们,并做你们的上帝。

买卖奴隶的条例

39“如果你们的同胞穷得把自己卖给你们,不可把他当作奴隶, 40要待他像雇工和寄居者一样。他要为你工作到禧年。 41到了禧年,他和孩子们便可以离开你们,回到自己的宗族和祖业。 42因为以色列人是我的仆人,是我从埃及带出来的,所以他们不可卖身为奴。 43你们也不可苛待他们,要敬畏你们的上帝。 44你们可以从邻国购买奴隶, 45也可以买居住或出生在你们境内的外族人。这些人可以作你们的产业。 46你们可以将他们作为产业传给你们的子孙,使他们终身做奴隶。但你们不可苛待自己的同胞。

47“如果你们中间的外族人渐渐富裕,你们同胞中却有人日益贫穷,把自己卖给外族人或他们的族人, 48他可以保留赎身的权利。他的兄弟、 49叔伯、堂兄弟或其他近亲都可以赎回他。如果他富裕起来,也可以赎回自己。 50他要和买主计算从自己卖身为奴到下个禧年之间的年数,然后按雇工的工价,照年数计算赎价。 51如果离禧年还有很多年,他就要按比例偿还大部分卖身款为自己赎身。 52如果离禧年只有不多的几年,他就要按年数偿还卖身款为自己赎身。 53买主要待他如按年雇佣的工人。你们要确保买主不会苛待他。 54如果禧年来临前他没有被赎回,到了禧年他和孩子们都要获得自由。 55因为以色列人是我的仆人,是我从埃及领出来的仆人。我是你们的上帝耶和华。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 25:1-55

Za Chaka Chopumula

1Yehova anawuza Mose pa phiri la Sinai kuti, 2“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukadzalowa mʼdziko limene ndikukupatsani, nthakayo iyenera kumakasunga Sabata la Yehova. 3Pa zaka zisanu ndi chimodzi muzikalima minda yanu, ndipo kwa zaka zisanu ndi chimodzi muzikasadza mitengo yanu ya mpesa ndi kuthyola zipatso zake. 4Koma chaka chachisanu ndi chiwiri ndi chaka choti nthaka ipume, chaka cha Sabata la Yehova. Musalime mʼminda yanu kapena kusadza mitengo yanu ya mpesa. 5Musakolole zimene zinamera zokha mʼmunda mwanu. Musakakolole kapena kuthyola mphesa za mʼmitengo imene simunasadze. Chaka chimenechi nʼchoti nthaka ipumule. 6Chaka chimene nthakayo ipumula mudzakhala ndi chakudya chokwanira inuyo, akapolo anu aamuna ndi aakazi, antchito ndi alendo okhala nanu. 7Ziweto zanu pamodzi ndi nyama za mʼdziko lanu zizidzadya zipatso za mʼnthaka.

Chaka Chokondwerera Zaka Makumi Asanu

8“ ‘Muzichotsera Masabata asanu ndi awiri a zaka, ndi kuchulukitsa zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawirinso kuti Masabata asanu ndi awiri a zakawo akwane zaka 49. 9Ndipo pa tsiku la khumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri mulize lipenga mofuwula. Tsiku lochita mwambo wopepesera machimo muziliza lipenga mʼdziko lanu lonse. 10Mupatule chaka cha makumi asanu, ndipo mulengeze kuti pakhale ufulu mʼdziko lonse kwa onse amene ali mʼmenemo. Kwa inu chakachi chidzakhala choyimba lipenga la chikondwerero. Aliyense wa inu adzayenera kubwerera pa munda wake, ndipo aliyense wa inu adzabwerera ku fuko lake. 11Kwa inu chakachi chidzakhaladi chaka choyimba lipenga kukondwerera zaka makumi asanu. Pa chaka chimenechi musadzale kanthu ndipo musakolole mbewu zomera zokha kapenanso kuthyola mphesa pa mitengo yosasadzira. 12Chimenechi ndi chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Choncho chikhale chaka chopatulika kwa inu. Muzidya zokhazo zimene zakololedwa mʼminda.

13“ ‘Chaka chimenechi ndi choliza lipenga, kukondwerera zaka makumi asanu, ndipo aliyense abwerere pa malo ake.

14“ ‘Ngati unagulitsa kapena kugula malo ako kwa mnzako wa mʼdzikomo, pasakhale kuchenjeretsana. 15Ugule kwa mnzako potsata chiwerengero cha zaka zimene zatha kuyambira pa chikondwerero cha chaka cha makumi asanu chapita. Ndipo mnzakoyo akugulitse potsata chiwerengero cha zaka zokolola zomwe zatsala. 16Zaka zikakhala zochuluka, uwonjezere mtengo, ndipo zaka zikakhala zochepa, uchepetse mtengo, pakuti chimene iye akukugulitsa ndi zaka zokolola. 17Musachenjeretsane koma muope Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

18“ ‘Tsatirani malangizo anga ndipo mverani mosamala malamulo anga ndipo mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere. 19Ndipo nthaka idzakupatsani zipatso zake. Mudzadya mpaka kukhuta ndiponso mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere. 20Mwina nʼkafunsa kuti, ‘Kodi chaka chachisanu ndi chiwiri tidzadya chiyani ngati sitidzala kapena kukolola mbewu zathu?’ 21Ine ndidzatumiza madalitso ambiri chaka chachisanu ndi chimodzi moti nthaka yanu idzabala zinthu zokwanira kudya zaka zitatu. 22Pamene mukudzala chaka chachisanu ndi chitatu, muzidzadya chakudya chogonera ndipo mudzapitirira kudya mpaka nthawi yokolola mʼchaka chachisanu ndi chinayi.

23“ ‘Malo asagulitsidwe mpaka muyaya chifukwa dzikolo ndi langa. Inu ndinu alendo okhala ndi Ine. 24Malo onse amene ali mʼmanja mwanu mudzalole kuti amene anakugulitsani awawombole.

25“ ‘Ngati Mwisraeli mnzanu wasauka nagulitsako gawo lina la malo ake, mʼbale wake wapaphata abwere kudzawombola malo amene mʼbale wakeyo wagulitsa. 26Koma ngati munthuyo alibe wachibale woti nʼkuwombola malowo koma pambuyo pake iye mwini nʼkulemera ndi kupeza zokwanira kuwombolera, awombole malowo. 27Awerengerane zaka kuyambira pamene anagulitsa mundawo ndipo amubwezere amene anagulayo ndalama zimene akanayenera kuzipereka mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Atatero angathe kubwerera pa malo ake. 28Koma ngati sakhala nazo zokwanira kuti amubwezere amene anagula malowo, gawo limene anagulitsalo lidzakhala mʼmanja mwa munthu amene anagulayo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Malowo adzabwezedwa chaka chimenechi, ndipo iye adzatha kubwerera pa malo ake.

29“ ‘Ngati munthu agulitsa nyumba ya mu mzinda umene uli mu linga, angathe kuyiwombola nyumbayo chisanathe chaka chathunthu chigulitsire. Mu nthawi imeneyi wogulitsayo atha kuyiwombola. 30Ngati nyumbayo siwomboledwa chisanathe chaka chimodzicho, nyumbayo idzakhala ya amene anagulayo ndi zidzukulu zake mpaka muyaya. Sidzabwezedwanso kwa mwini wake mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu. 31Koma nyumba za mʼmizinda yosazingidwa ndi linga ziwomboledwe monga mmene achitira ndi minda ya mʼdzikomo.

32“ ‘Alevi ali ndi ufulu owombola nyumba zawo za mʼmidzi yawo nthawi ina iliyonse. 33Koma ngati Mlevi sawombola nyumba imene inagulitsidwa mʼmudzi mwake, ndiye kuti idzabwezedwe mʼchaka choliza lipenga pokondwerera zaka makumi asanu, popeza nyumba zimenezi zili mʼmidzi ya Alevi ndi yawo pakati pa Aisraeli. 34Koma malo owetera ziweto a mʼmidzi yawoyo sayenera kugulitsidwa. Awa ndi malo awo mpaka muyaya.

35“ ‘Ngati mʼbale wako akhala wosauka kuti sangathe kudzisamalira yekha, umuthandize. Ukhale naye ngati mlendo kapena ngati munthu amene ukhala naye kwa kanthawi. 36Usalandire chiwongoladzanja chilichonse kuchokera kwa iye kapena kuwonjezerapo kanthu kena, koma uziopa Mulungu kuti mʼbale wakoyo akhale nawe. 37Musakongoze mnzanu ndalama kuti mulandire chiwongoladzanja, kapena kumugulitsa chakudya kuti mupeze phindu. 38Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikupatseni dziko la Kanaani ndi kuti ndikhale Mulungu wanu.

39“ ‘Ngati mʼbale wanu asauka ndipo adzigulitsa yekha kwa inu, musamugwiritse ntchito ngati kapolo. 40Akhale ngati wantchito kapena ngati mlendo. Akugwirireni ntchito mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. 41Kenaka iye ndi ana ake achoke, ndipo apite ku fuko lake ndi kubwerera ku malo a makolo ake. 42Chifukwa Aisraeli ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto, asagulitsidwe ngati akapolo. 43Musawalamulire mwankhanza koma wopani Mulungu wanu.

44“ ‘Kunena za akapolo aamuna ndi aakazi, amenewa mungathe kuwagula kuchokera kwa mitundu ya anthu imene yakuzungulirani. 45Mungathenso kugula akapolo kuchokera kwa alendo amene akukhala nanu kapena kuchokera ku mabanja amene mukukhala nawo amene ndi mbadwa za mʼdziko lanu. Iwowa akhoza kukhala akapolo anu. 46Akapolowo mungathe kuwasiya mʼmanja mwa ana anu inu mutafa kuti akhale cholowa chawo moyo wawo wonse. Koma musawalamulire mwankhanza Aisraeli anzanu.

47“ ‘Ngati mlendo kapena munthu amene akukhala nanu kwa kanthawi kochepa alemera ndipo mmodzi wa abale anu amene akukhala naye pafupi nʼkusauka, nadzigulitsa yekha kwa mlendo amene akukhala pakati panuyo kapena kwa mmodzi wa fuko la munthu wongokhala pafupi nayeyo, 48wodzigulitsayo ali ndi ufulu wowomboledwa. Mmodzi mwa abale ake angathe kumuwombola: 49amalume ake kapena mwana wa amalume ake, kapena wachibale wa mu fuko lake. Kapena ngati iye mwini alemera, atha kudziwombola yekha. 50Iye pamodzi ndi munthu amene anamugulayo awerengerane kuyambira chaka chimene anadzigulitsa kwa iyeyo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Mtengo wodziwombolera ukhale wofanana ndi zakazo. Ndipo nthawi imene anali ndi mbuye wakeyo iwerengedwe ngati nthawi ya munthu wantchito. 51Ngati patsala zaka zambiri, iye ayenera kulipira mtengo woposera umene anamugulira. 52Ngati kwatsala zaka zochepa kuti ifike nthawi ya chaka chokondwerera zaka makumi asanu, iye awerengerane ndi mbuye wake, ndipo apereke ndalama za zowomboledwera molingana ndi zaka zotsalazo. 53Azikhala naye ngati wantchito wolembedwa chaka ndi chaka. Ndipo muonetsetse kuti mbuye wakeyo sakumulamulira mwankhanza.

54“ ‘Ngakhale munthuyo atapanda kuwomboledwa mwa njira zimenezi, iye ndi ana ake ayenera kumasulidwa mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu, 55pakuti Aisraeli ndi atumiki anga. Iwo ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.