利未记 17 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

利未记 17:1-16

杀祭牲的条例

1耶和华对摩西说: 2“你把以下条例告诉亚伦父子们及全体以色列人。

3“任何在营内或营外宰杀公牛、绵羊或山羊的以色列人, 4若没有把牲畜带到会幕门口,在耶和华的圣幕前献给耶和华,便是犯了流血之罪,要将他从民中铲除。 5这是为促使以色列人把祭牲带到会幕门口交给祭司,献给耶和华作平安祭,而非在野外杀祭牲献祭。 6祭司要将祭牲的血洒在会幕门口耶和华的祭坛上,把脂肪焚烧献给耶和华作馨香之祭。 7他们不可再献祭物给山羊神,与其苟合。这是一条永远不变的律例,他们世世代代都要遵守。 8不论是以色列人,还是寄居在以色列人中间的外族人,献燔祭或其他祭物时, 9如果有人没把祭物带到会幕门口献给耶和华,要将他从民中铲除。

禁止吃血

10“任何以色列人或寄居在以色列人中间的外族人若吃血,耶和华必严惩,把他从民中铲除。 11因为生命在血中,耶和华把血赐给你们,使你们可以用血在祭坛上为自己赎罪。血可以为人的生命赎罪。 12所以耶和华吩咐以色列人和寄居在以色列人中间的外族人不可吃血。 13以色列人或寄居在以色列人中间的外族人如果捕到可吃的鸟或兽,必须放尽它的血,用土掩埋, 14因为众生的生命都在血中。因此,耶和华吩咐以色列人不可吃任何动物的血,因为血就是生命。凡吃血的都要被铲除。 15不论以色列人还是外族人,若吃了自然死亡或被野兽撕裂的动物,就不洁净。他必须洗衣、沐浴,等到傍晚才能洁净, 16否则他要承担罪责。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 17:1-16

Za Kusadya Magazi

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi: 3Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa, 4mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake. 5Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano. 6Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova. 7Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’ ”

8“Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse 9popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’ ”

10“Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake. 11Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo. 12Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’ ”

13“Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi, 14chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.

15“ ‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa. 16Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’ ”