列王纪下 22 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

列王纪下 22:1-20

约西亚做犹大王

1约西亚八岁登基,在耶路撒冷执政三十一年。他母亲叫耶底大,是波斯加亚大雅的女儿。 2约西亚做耶和华视为正的事,事事效法他祖先大卫,不偏不离。

发现律法书

3约西亚执政第十八年,他派米书兰的孙子、亚萨利的儿子沙番书记去耶和华的殿,并吩咐他说: 4“你去见大祭司希勒迦,让他清点奉献到耶和华殿中的银子,那些银子是殿门守卫从民众收集来的。 5-6然后把银子交给负责修理耶和华殿的督工,他们就可以购买木料和凿好的石头,雇用木匠、建筑工人和石匠来修理耶和华的殿。 7你不用查核他们的账目,因为他们都是忠诚可靠的人。”

8大祭司希勒迦告诉书记沙番说:“我在耶和华的殿里找到了律法书。”希勒迦把书交给沙番看。 9沙番禀告王说:“你的臣仆已经把殿里的银子清点完毕,交给了殿里的督工和工人。” 10他又告诉王:“希勒迦祭司给了我一卷书。”沙番就在王面前诵读这书。 11王听了律法书上的话,就撕裂衣服, 12吩咐希勒迦祭司、沙番的儿子亚希甘米该亚的儿子亚革波、书记沙番和王的臣仆亚撒雅13“你们为我、为民众和整个犹大去求问耶和华有关这书卷上的话。耶和华的烈怒已经临到我们身上,因为我们的祖先没有遵守这书卷上的话,没有遵行这书卷上的吩咐。”

户勒妲的预言

14于是,希勒迦祭司、亚希甘亚革波沙番亚撒雅去求问女先知户勒妲。她是负责管理礼服的沙龙的妻子,沙龙哈珥哈斯的孙子、特瓦的儿子。户勒妲住在耶路撒冷第二区。他们向她说明来意。 15她对他们说:“以色列的上帝耶和华要你们回去告诉差你们来见我的人, 16耶和华说,‘我要照犹大王所读的那书上的一切话,降灾难给这地方及这里的居民。 17因为他们背弃我,给别的神明烧香,制造偶像惹我发怒,我的怒火要在这地方燃烧,绝不止息。 18你们告诉差你们来求问耶和华的犹大王,至于你所听见的那些话,以色列的上帝耶和华说, 19因为你听到我对这地方及其居民的警告,知道这地方要受咒诅、沦为荒场,便悔改,在我面前谦卑,撕裂衣服,向我哭泣。因此,我垂听了你的祷告。这是我耶和华说的。 20我会让你平安入土到你祖先那里。你不会看到我要降给这地方的一切灾难。’”他们便回去禀告王。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 22:1-20

Buku la Malamulo Lipezeka

1Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati. 2Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.

3Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati, 4“Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu. 5Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova, 6amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova. 7Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”

8Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga. 9Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.” 10Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.

11Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake. 12Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti, 13“Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”

14Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.

15Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti, 16‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga. 17Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’ 18Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva: 19Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova. 20Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’ ”

Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.