但以理书 4 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

但以理书 4:1-37

尼布甲尼撒的第二个梦

1尼布甲尼撒王传谕天下各族、各邦、各语种的人:“愿你们大享平安! 2我乐意向你们述说至高的上帝对我所行的神迹奇事。

3“祂的神迹何其伟大!

祂的奇事何其可畏!

祂的国度永远长存,

祂的统治直到万代。

4“我尼布甲尼撒安居在家,在宫中享受荣华。 5但我做了一个梦,令我害怕。我躺在床上的时候,脑中出现的情景和异象使我恐惧。 6我便召巴比伦所有的智者来为我解梦。 7术士、巫师、占星家和占卜者都来了,我将梦告诉他们,他们却不能给我解梦。 8最后但以理来到我面前,他又名伯提沙撒——取自我神明的名,他有圣洁神明的灵。我将梦告诉他,说, 9‘术士的首领伯提沙撒啊,我知道你有圣洁神明的灵,任何奥秘都难不倒你。请你为我解释我梦中所见的异象。

10“‘以下是我躺在床上时脑中出现的异象:我看见大地中央有棵非常高大的树。 11这树长得苍劲有力,高可参天,从地极都能看见。 12它的叶子美丽,果实累累,可作众生的食物。野兽在它的荫下躺卧,飞鸟在它的枝头栖息,一切生灵都从它那里得到食物。

13“‘我躺在床上时脑中出现了异象,我看见一位圣洁的守望者从天而降。 14他大声说,砍倒那棵树,削掉它的枝子,剥光它的叶子,抛散它的果子,使野兽逃离树下,飞鸟离开枝头。 15但把树丕留在地里,用铁环和铜环箍住他留在野地的青草中,让他被天上的露水浸湿,与野兽一起吃草。 16要改变他的人心,给他一个兽心,达七年之久。 17这是守望者的命令,是圣者的决定,要让众生知道至高者主宰世上万国,祂要把国赐给谁就赐给谁,即使是最卑微的人。’

18“这就是我尼布甲尼撒王所做的梦。伯提沙撒啊,你要为我解梦,因为我国中所有的智者都不能为我解梦。但是你能,因为你有圣洁神明的灵。”

但以理解梦

19但以理,又名伯提沙撒,一时非常惊讶,惶恐不安。王说:“伯提沙撒啊,不要因为这梦和梦的意思而惶恐不安。”伯提沙撒回答说:“我主啊,愿这梦发生在恨你的人身上,梦的意思应验在你的仇敌身上。 20你梦见的树苍劲有力,高可参天,从地极都能看见。 21它的叶子美丽,果实累累,可作众生的食物。野兽住在它的荫下,飞鸟宿在它的枝头。 22王啊,这苍劲有力的树就是你,你的威名高达穹苍,你的权柄延至地极。 23王看见圣洁的守望者从天而降,说,‘将这树砍倒、毁灭,但把树丕用铁环和铜环箍住留在野地的青草中,让他被天上的露水浸湿,与野兽一起吃草,达七年之久。’

24“王啊,以下是梦的意思,是至高者裁定要临到我主我王的事: 25你必从人群中被赶走,与野兽同住,像牛一样吃草,被天上的露水浸湿,达七年之久,直到你知道至高者主宰世上万国,祂要把国赐给谁就赐给谁。 26守望者命令留下树丕,表示等到你承认上天掌权后,你将重掌国权。 27王啊,请接受我的劝谏,你要秉公行义,以断绝罪恶;怜悯穷人,以除掉罪过。这样,你的国运也许可以延续。”

梦兆应验

28这一切事果然发生在尼布甲尼撒王身上。 29十二个月后,他在巴比伦王宫的屋顶散步时, 30说:“这宏伟的巴比伦岂不是我用大能建立为京都,以显我的威严和荣耀吗?” 31话未说完,天上就有声音说:“尼布甲尼撒王啊,你听着,你已失去王权。 32你必从人群中被赶走,与野兽同住,像牛一样吃草,达七年之久,直到你知道至高者主宰世上万国,祂要把国赐给谁就赐给谁。” 33这话立刻应验在尼布甲尼撒身上。他从人群中被赶走,像牛一样吃草,身体被天上的露水浸湿,直到他的头发长如鹰毛,指甲长如鸟爪。

34“七年后,我尼布甲尼撒举目望天,恢复了神智,便称颂至高者,赞美、尊崇永活者。

“祂的统治永无穷尽,

祂的国度直到万代。

35世人都微不足道,

祂在天军和世人中独行其道,

无人能拦阻祂的手,

或质问祂的作为。

36“那时,我恢复了神智,也恢复了我的威严和荣耀,重现我国度的辉煌。我的谋士和大臣都来朝见我,我重掌国权,势力比以前更大。 37现在我尼布甲尼撒颂赞、尊崇、敬奉天上的王,因为祂的作为公正,祂行事公平,能够贬抑行为骄傲的人。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 4:1-37

Maloto Achiwiri a Nebukadinezara

1Mfumu Nebukadinezara anatumiza mawu awa kwa anthu a mitundu yonse, ndi chiyankhulo chilichonse, amene amakhala pa dziko lonse lapansi:

Mtendere uchuluke pakati panu!

2Chandikomera kukuwuzani zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene Mulungu Wammwambamwamba wandichitira.

3Zizindikiro zake ndi zazikulu,

zozizwitsa zake ndi zamphamvu!

Ufumu wake ndi wamuyaya;

ulamuliro wake ndi wa mibadomibado.

4Ine Nebukadinezara, ndinali kwathu mʼnyumba yanga yaufumu, mwa mtendere ndipo ndinali wokhutitsidwa. 5Ndili chigonere pa bedi langa, ndinalota maloto amene anandichititsa mantha. Zinthu ndi masomphenya zimene ndinaziona zinandiopsa. 6Choncho ndinalamula kuti anthu onse a nzeru a ku Babuloni abwere pa maso panga kunditanthauzira malotowo. 7Pamene amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula anabwera, ndinawafotokozera maloto, koma sanathe kunditanthauzira. 8Potsiriza, anabwera Danieli uja amatchedwa Belitesezara, potsata dzina la mulungu wanga, ndipo mzimu wa milungu yoyera uli mwa iye. Iyeyu ndinamufotokozera malotowo.

9Ndinati, “Belitesezara, mkulu wa amatsenga, ndikudziwa kuti mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe, ndipo palibe chinsinsi chomwe sungachidziwe. Awa ndi maloto anga; unditanthauzire. 10Awa ndi masomphenya amene ine ndinaona pamene ndinali kugona pa bedi: Ndinaona, mtengo wautali kwambiri utayima pakati pa dziko lapansi. 11Mtengowo unakula ndi kulimba ndipo msonga yake inafika mpaka mlengalenga; umaonekera pa dziko lonse lapansi. 12Masamba ake anali okongola, zipatso zinali zochuluka, ndipo mu mtengomo munali chakudya chokwanira anthu onse. Zirombo zakuthengo zimapeza mthunzi mʼmunsi mwake, ndipo mbalame zamlengalenga zimakhala pa nthambi zake: Cholengedwa chilichonse chinkadya za mu mtengowu.

13“Ndikanali chigonere ndinaona mʼmasomphenya mngelo atayima pamaso panga, woyera, atatsika kuchokera kumwamba. 14Anayankhula mofuwula kuti, ‘Gwetsa mtengo ndi kusadza nthambi zake; yoyola masamba ake kuti nyama zakuthengo zithawe pa mthunzi pake ndi mbalame zithawe pa nthambi zake. 15Koma musiye tsinde ndi mizu yake mʼnthaka. Tsindelo mulimange maunyolo a chitsulo ndi mkuwa, zikhalebe mʼnthaka, nʼkudya udzu mʼmunda.

“ ‘Mumulole iye anyowe ndi mame akumwamba, ndipo iye akhale ndi nyama pakati pa zomera za mʼnthaka. 16Maganizo ake a umunthu asinthidwe ndipo apatsidwe maganizo a nyama ya kuthengo, mpaka zaka zisanu ndi ziwiri zitadutsa.

17“ ‘Angelo oyera ndiwo akutsimikiza chilangochi. Tsono anthu adziwe kuti Mulungu Wammwambamwamba ali ndi mphamvu yolamulira maufumu onse, ndipo amawapereka kwa aliyense akumufuna, ngakhale munthu wamba kuti alamulire.’

18“Amenewa ndi maloto amene ine, mfumu Nebukadinezara, ndinalota. Tsopano Belitesezara, undifotokozere tanthauzo lake, popeza palibe mwa anthu anzeru a mu ufumu wanga amene angathe kunditanthauzira. Koma iwe ukhoza, chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.”

Danieli Atanthauzira Maloto

19Pamenepo Danieli, amene amatchedwa Belitesezara, anavutika mu mtima kwambiri kwa kanthawi, ndipo anasautsidwa mʼmaganizo ake. Choncho mfumu inati, “Belitesezara usalole malotowa kapena tanthauzo lake likuopse.”

Belitesezara anayankha kuti, “Mbuye wanga, ndikanakonda malotowa akanakhudza adani anu okha, ndi tanthauzo lake kwa iwo okusautsani! 20Mtengo munawuona uja, umene unkakulirakulira kwambiri ndi kulimba, ndi msonga yake inafika mlengalenga, ndi kuonekera ku dziko lonse lapansi, 21mtengo umene masamba ake anali okongola ndiponso unali ndi zipatso zochuluka zokwanira kudya anthu onse a dziko lapansi. Mtengowu unkapereka mthunzi ku zirombo zonse zakuthengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinayika zisa pa nthambi zake. 22Inu mfumu, ndinu mtengo umenewo! Inu mwakhala wamkulu ndi wamphamvu; ukulu wanu wakula mpaka wakhudza mlengalenga, ndipo ufumu wanu wafika mpaka ku malo akutali a dziko lapansi.

23“Inu mfumu munaona mthenga woyera, akuchokera kumwamba ndipo anati, ‘Gwetsani mtengo ndipo muwuwononge, koma musiye tsinde ndi mizu yake. Tsindelo mulimange ndi unyolo wa chitsulo ndi mkuwa ndipo mulisiye pakati pa udzu wa mʼmunda. Mulole kuti linyowe ndi mame akumwamba. Likhale ngati nyama zakuthengo, mpaka zaka zidutse zisanu ndi ziwiri.’

24“Tanthauzo lake ndi ili mfumu, izi ndi zimene Mulungu Wammwambamwamba watsimikiza kuti zikugwereni mbuye wanga mfumu: 25Inu mudzachotsedwa pakati pa anthu ndipo mudzakhala ndi nyama zakuthengo; mudzadya udzu monga ngʼombe ndi kunyowa ndi mame akumwamba. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka mudzavomereze kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa ma ufumu a anthu, ndipo amawapereka kwa aliyense amene Iye wafuna. 26Lamulo losiya tsinde la mtengo ndi mizu yake litanthauza kuti ufumu wanu udzabwezeredwa kwa inu mukadzavomereza kuti Mulungu ndiye amalamulira. 27Nʼchifukwa chake mfumu, chikukomereni kulandira malangizo anga: Lekani machimo ndipo muzichita zabwino, lekani mphulupulu zanu ndipo muzikomera mtima anthu opsinjika. Nʼkutheka kuti mtendere wanu udzapitirira.”

Maloto Akwaniritsidwa

28Zonsezi zinamuchitikira mfumu Nebukadinezara. 29Itapita miyezi khumi ndi iwiri, pamene mfumu inkayenda pa denga la nyumba ya ufumu ya ku Babuloni, 30iye anati, “Kodi Babuloni si mzinda wamphamvu ndi wokongola umene ndinamanga ndi mphamvu zanga ngati nyumba yanga yaufumu, kuonetsera ulemerero wa ufumu wanga?”

31Akuyankhulabe izi mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Imvani izi, mfumu Nebukadinezara: Ufumu wako wachotsedwa. 32Udzachotsedwa pakati pa anthu ndipo udzakhala ndi zirombo zakuthengo; udzadya udzu monga ngʼombe. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka iwe utavomereza kuti Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene iye afuna.”

33Nthawi yomweyo zonse zimene zinanenedwa zokhudza Nebukadinezara zinakwaniritsidwa. Iye anachotsedwa pakati pa anthu ndipo ankadya udzu ngati ngʼombe. Thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba mpaka tsitsi lake linakula ngati nthenga za chiwombankhanga ndi zikhadabo ngati zikhadabo za mbalame.

34Pomaliza pa zaka zimenezo ine, Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndipo nzeru zanga zinabwereramo. Kenaka ndinatamanda Wammwambamwamba; ndinamupatsa ulemu ndi kumulemekeza Iye amene akhala nthawi zonse.

Ulamuliro wake ndi ulamuliro wa nthawi zonse;

ufumu wake udzakhala ku mibadomibado.

35Anthu onse a dziko lapansi

ali chabe pamaso pake.

Pakati pa angelo akumwamba

ndi anthu a dziko lapansi

palibe amene akhoza kumuletsa

Mulungu kuchita zimene afuna.

Kapena kunena kwa Iye kuti, “Kodi mwachita chiyani?”

36Pa nthawi yomweyo nzeru zanga zinabwereramo. Ndinalandiranso ulemu wanga ndi ufumu wanga. Nduna ndi akalonga anga anandilandiranso. Ndipo anandibwezera ufumu wanga ndi kukhalanso wamphamvu kuposa kale. 37Tsopano ine Nebukadinezara, ndikutamanda, kukweza ndi kulemekeza Mfumu yakumwamba chifukwa zonse zimene amachita ndi zoyenera ndipo njira zake zonse ndi zachilungamo. Ndipo onse amene amayenda modzikuza adzawatsitsa.