传道书 7 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

传道书 7:1-29

1美好的名声胜过珍贵的膏油,

人死之日胜过出生之时。

2探望丧家胜过参加宴席,

因为死亡是每个人的结局,

活着的人要把这事铭记在心。

3哀伤胜过欢笑,

因为哀伤磨炼人的心灵。

4智者的心思考生死大事,

愚人的心只顾作乐。

5听智者的责备,

胜过听愚人的颂歌。

6愚人的笑声像锅底下烧荆棘的劈啪声。

这也是虚空。

7欺压使智者变愚昧,

贿赂败坏人心。

8事情的结局胜过事情的开端;

恒久忍耐胜过心骄气傲。

9不要轻易发怒,

因为愚人心怀怒气。

10不要问为什么过去比现在好,

因为这样问不明智。

11智慧如同产业一样美好,

有益于得见日光的世人。

12智慧如同金钱,

是一种保障,

能保全智者的生命。

这就是知识的好处。

13你应当思想上帝的作为,

因为上帝弄弯的,

谁能使它变直呢?

14顺境时要快乐,

逆境时要思想:

两者都是上帝的安排,

好叫人不能预知将来。

15在我虚空的一生中,我见过义人行义,反而灭亡;恶人行恶,却享长寿。 16为人不要过分正直,也不要过于聪明,何必自取毁灭呢? 17不要过分邪恶,也不要做愚人,何必时候未到就死呢? 18最好是持守这个教训也不放松那个教训,因为敬畏上帝的人必避免两个极端。 19智慧使一个智者比城里十个官长更有能力。 20诚然,在地上无法找到一个一生行善、从未犯罪的义人。 21你不要斤斤计较别人所说的每一句话,免得听见你的仆人咒诅你, 22因为你心里知道自己也曾多次咒诅别人。 23我用智慧试验过这一切。我说:“我要做智者”,谁知智慧却离我甚远。 24智慧如此遥不可及、深不可测,谁能找得到呢? 25我用心去认识、探究、追寻智慧和事物的原委,并去认识邪恶带来的愚昧和无知带来的狂妄。 26我发现有的妇人比死亡更苦毒,她是个陷阱,心如网罗,手像锁链。敬畏上帝的人避开她,罪人却被她俘虏。 27-28传道者说:“看啊,我事事反复探索,要查明万事之理,却没有寻获。但我发现在一千个男子中还可以找到一位正直人,在众女子中却未找到一位。 29我只发现一件事,上帝造的人本来正直,人却找出各种诡计。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 7:1-29

Nzeru

1Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino,

ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.

2Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro

kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero:

Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense;

anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.

3Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka,

pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.

4Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa,

koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.

5Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru

kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.

6Kuseka kwa zitsiru kuli ngati

kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika,

izinso ndi zopandapake.

7Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru,

ndipo chiphuphu chimawononga mtima.

8Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake,

ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.

9Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako,

pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.

10Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?”

pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.

11Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino

ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.

12Nzeru ndi chitetezo,

monganso ndalama zili chitetezo,

koma phindu la chidziwitso ndi ili:

kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.

13Taganizirani zimene Mulungu wazichita:

ndani angathe kuwongola chinthu

chimene Iye anachipanga chokhota?

14Pamene zinthu zili bwino, sangalala;

koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino:

Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo,

ndiponso nthawi imene si yabwinoyo.

Choncho munthu sangathe kuzindikira

chilichonse cha mʼtsogolo mwake.

15Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi:

munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake,

ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.

16Usakhale wolungama kwambiri

kapena wanzeru kwambiri,

udziwonongerenji wekha?

17Usakhale woyipa kwambiri,

ndipo usakhale chitsiru,

uferenji nthawi yako isanakwane?

18Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi,

ndipo usataye njira inayo.

Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.

19Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru

kupambana olamulira khumi a mu mzinda.

20Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi

amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.

21Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula,

mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,

22pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako

kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.

23Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati,

“Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,”

koma nzeruyo inanditalikira.

24Nzeru zimene zilipo,

zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri,

ndani angathe kuzidziwa?

25Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe,

ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira

ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru

ndiponso kupusa kwake kwa misala.

26Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa,

mkazi amene ali ngati khoka,

amene mtima wake uli ngati khwekhwe,

ndipo manja ake ali ngati maunyolo.

Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo,

koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.

27Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi:

“Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,

28pamene ine ndinali kufufuzabe

koma osapeza kanthu,

ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000,

koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.

29Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi:

Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama,

koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”