传道书 6 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

传道书 6:1-12

1我看见日光之下有一件可悲的事,重重地压在人身上: 2上帝赐给人财富和尊荣,叫他拥有所渴望的一切,却使他无法享用,倒让别人享用。这是虚空,是极大的悲哀。 3人若有一百个儿子,并且长寿,但心中却从未得到满足,死后又不得安葬。唉!这样的人还不如流产的胎儿。 4这胎儿在虚空中来,在黑暗中去,名字隐没在黑暗中, 5没有见过天日,一无所知,然而这胎儿比那人更享安息。 6就算那人活了千年,又活千年,却不能享受福乐,又如何呢?世人最终岂不都同归一处吗? 7人人为口腹劳碌,却永不满足。 8那么,智者比愚人有什么优势呢?贫穷人即使懂得如何处世,又有什么益处呢? 9满足于眼前所有的,胜过心中贪想的。这也是虚空,如同捕风。 10一切存在的事物都已有了名字,人的本质也被识透了;人无法与比他更强的较量。 11其实话越多,越虚空,这对人又有什么益处? 12人生短暂虚空,如影飞逝,有谁知道什么对人有益?谁能告诉人死后日光之下会发生什么事?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 6:1-12

1Ine ndinaona choyipa china pansi pano, ndipo chimasautsa anthu kwambiri: 2Mulungu amapereka chuma, zinthu ndi ulemu kwa munthu, kotero kuti munthuyo sasowa kanthu kalikonse kamene akukalakalaka, koma Mulungu samulola kuti adyerere zinthuzo, ndipo mʼmalo mwake amadyerera ndi mlendo. Izi ndi zopandapake, ndi zoyipa kwambiri.

3Ngakhale munthu atabereka ana 100 ndi kukhala ndi moyo zaka zambiri; komatu ngakhale atakhala zaka zambiri chotani, ngati iye sangadyerere chuma chake ndi kuyikidwa mʼmanda mwaulemu, ine ndikuti mtayo umamuposa iyeyo. 4Mtayo umangopita pachabe ndipo umapita mu mdima, ndipo mu mdimamo dzina lake limayiwalika. 5Ngakhale kuti mtayowo sunaone dzuwa kapena kudziwa kanthu kalikonse, koma umapumula kuposa munthu uja, 6ngakhale munthuyo atakhala ndi moyo zaka 2,000, koma ndi kulephera kudyerera chuma chake. Kodi onsewa sapita malo amodzi?

7Ntchito yonse ya munthu imathera pakamwa pake,

komatu iye sakhutitsidwa ndi pangʼono pomwe.

8Kodi munthu wanzeru

amaposa motani chitsiru?

Kodi munthu wosauka amapindula chiyani

podziwa kukhala bwino pamaso pa anthu ena?

9Kuli bwino kumangoona zinthu ndi maso

kusiyana ndi kumangozilakalaka mu mtima.

Izinso ndi zopandapake,

nʼkungodzivuta chabe.

10Chilichonse chimene chilipo anachitchula kale dzina,

za mmene munthu alili nʼzodziwika;

sangathe kutsutsana ndi munthu

amene ali wamphamvu kupambana iyeyo.

11Mawu akachuluka

zopandapake zimachulukanso,

nanga munthu zimamupindulira chiyani?

12Pakuti ndani amene amadziwa chomwe ndi chabwino pa moyo wa munthu, pakuti moyo wake ndi wa masiku ochepa ndi opandapake, umangopitira ngati mthunzi. Ndani amene angamufotokozere zimene zidzachitika pansi pano iye atapita?