传道书 5 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

传道书 5:1-20

敬畏上帝

1你进入上帝的殿时要小心谨慎,近前倾听胜过愚人献祭,因为他们不知道自己是在作恶。 2在上帝面前不要冒失开口,不可急于发言,因为祂在天上,你在地上。所以,你要少言寡语。 3事务繁杂,夜里多梦;多言多语,显出愚昧。 4你向上帝许愿,不可迟迟不还,因为祂不喜欢这样的愚人。要还所许的愿。 5与其许了愿不还,倒不如不许。 6不要在言语上犯罪,也不要在祭司5:6 祭司”希伯来文是“使者”。面前说许错了愿。为什么用言语惹上帝发怒,以致祂摧毁你手中的工作呢? 7多梦多言都是虚空。你只要敬畏上帝!

财富虚空

8若你在某地看见穷人受欺压,公平正义被扭曲,不要震惊,因为官上有官,在众官之上还有更高的官。 9况且,地的出产滋养万物,就是君王也需要从田地得到供应。 10贪爱钱财的,金银不能使他满足;贪图富裕的,再多的利益也不能叫他称心。这也是虚空! 11财富增加,消费的人也增加,这对财富的主人有什么益处呢?只是过眼烟云罢了! 12劳力的人不管吃多吃少,总是睡得香甜;富人的万贯家财却害得他不能成眠。 13我看到日光之下有一件可悲的事:有人积攒财宝,反而害了自己。 14经营不善,便财富尽失,什么也不能留给儿子。 15人怎样从母腹空空而来,也必照样空空而去;劳碌一生,什么也不能带走。 16这是多么可悲啊!人怎样来,也要怎样去,为风劳碌有什么益处呢? 17他一生活在黑暗中,饱受烦恼、病痛和愤怒的困扰。 18我认为人生最美最善的是,在上帝所赐的短暂岁月中尽情吃喝,享受自己在日光之下劳苦得来的成果。因为这是人当得的。 19上帝不单给人财富,也叫他能吃能喝,享用自己所当得的,并在劳碌中得到快乐,这都是上帝的恩赐。 20他不用担忧自己寿命的长短,因为上帝使他心里充满喜乐。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 5:1-20

Lemekeza Mulungu

1Uzisamala mayendedwe ako pamene ukupita ku nyumba ya Mulungu. Upite pafupi kuti ukamvetsere mʼmalo mopereka nsembe ya zitsiru zimene sizizindikira kuti zikuchita zolakwa.

2Usamafulumire kuyankhula,

usafulumire mu mtima mwako

kunena chilichonse pamaso pa Mulungu.

Mulungu ali kumwamba

ndipo iwe uli pa dziko lapansi,

choncho mawu ako akhale ochepa.

3Kuchuluka kwa mavuto mu mtima kumabweretsa maloto oyipa,

ndipo kuchuluka kwa mawu kumadzetsa uchitsiru.

4Pamene ulumbira kwa Mulungu usachedwe kukwaniritsa chimene walumbiracho. Iye sakondweretsedwa ndi chitsiru; kwaniritsa lumbiro lako. 5Kuli bwino kusalumbira kusiyana ndi kulumbira koma osakwaniritsa lumbirolo. 6Pakamwa pako pasakuchimwitse. Ndipo usanene kwa mthenga wa mʼNyumba ya Mulungu kuti, “Ndinalakwitsa polumbira.” Chifukwa chiyani ukufuna Mulungu akwiye ndi mawu ako ndiponso ntchito ya manja ako? 7Maloto ochuluka ndi mawu ochuluka ndi zinthu zopandapake. Kotero lemekeza Mulungu.

Chuma Nʼchopandapake

8Ngati uwona anthu osauka akuzunzika mʼdziko, ndiponso anthu ena akupsinja anzawo ndi kuwalanda ufulu wawo, usadabwe ndi zinthu zimenezi; pakuti woyangʼanira ali naye wina womuyangʼanira wamkulu, ndipo pamwamba pa awiriwa pali ena akuluakulu owaposa. 9Anthu onse amatengako zokolola za mʼminda: koma ndi mfumu yokha imene imapeza phindu la mindayi.

10Aliyense amene amakonda ndalama sakhutitsidwa ndi ndalamazo;

aliyense amene amakonda chuma sakhutitsidwa ndi zimene amapeza.

Izinso ndi zopandapake.

11Chuma chikachuluka

akudya nawo chumacho amachulukanso.

Nanga mwini wake amapindulapo chiyani

kuposa kumangochiyangʼana ndi maso ake?

12Wantchito amagona tulo tabwino

ngakhale adye pangʼono kapena kudya kwambiri,

koma munthu wolemera, chuma

sichimulola kuti agone.

13Ine ndinaona choyipa chomvetsa chisoni pansi pano:

chuma chokundikidwa chikupweteka mwini wake yemwe,

14kapena chuma chowonongedwa pa nthawi yatsoka,

kotero kuti pamene wabereka mwana

alibe kanthu koti amusiyire.

15Munthu anabadwa wamaliseche kuchokera mʼmimba mwa amayi ake,

ndipo monga iye anabadwira, adzapitanso choncho.

Pa zonse zimene iye anakhetsera thukuta

palibe nʼchimodzi chomwe chimene adzatenge mʼmanja mwake.

16Izinso ndi zoyipa kwambiri:

munthu adzapita monga momwe anabwerera,

ndipo iye amapindula chiyani,

pakuti amagwira ntchito yolemetsa yopanda phindu?

17Masiku ake onse ndi odzaza ndi mdima,

kukhumudwa kwakukulu, masautso ndi nkhawa.

18Tsono ndinazindikira kuti nʼchabwino ndi choyenera kuti munthu azidya ndi kumwa, ndi kukhutitsidwa ndi ntchito yake yolemetsa imene amayigwira pansi pano pa nthawi yake yochepa imene Mulungu amamupatsa, poti ichi ndiye chake. 19Komatu pamene Mulungu apereka chuma kwa munthu aliyense ndi zinthu zina, ndi kulola kuti akondwere ndi chumacho, munthuyo alandire chumacho ndi kusangalala ndi ntchito yake, imene ndi mphatso yochokera kwa Mulungu. 20Munthu wotereyu saganizirapo za masiku a moyo wake, chifukwa Mulungu amamutanganidwitsa ndi chisangalalo cha mu mtima mwake.