传道书 11 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

传道书 11:1-10

1当慷慨施舍11:1 当慷慨施舍”或译“当把你的资财投入海外贸易”。

因为日后必有收获。

2当把你的资财分给多人,

因为你不知道日后会有什么灾难临到世上。

3云中满了水,就会下雨。

树不论倒向南或倒向北,

倒在哪里就躺在哪里。

4你若等待完美的天气,

必无法撒种,无法收割。

5正如你不知道风的路线,不知道骨骼在母胎中如何形成,你也无法了解创造万物之上帝的作为。 6你要早晚不停地撒种,因为你不知道什么时候撒的种子会发芽生长,或许所撒的都会带来收获。 7光真美好,能够看见阳光真好! 8人一生不论活多久,都要活得快乐,但不要忘记死后有许多黑暗的日子。将来的一切都是虚空。 9年轻人啊,在年轻时要快乐,要在青春岁月里使自己的心欢畅。心里想做什么就去做,眼睛想看什么就去看。然而,要切记:上帝必照你所行的一切审判你。 10所以,你要抛开心中的烦恼和肉体的痛苦,因为青春年华转瞬即逝。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 11:1-10

Kuponya Chakudya pa Madzi

1Ponya chakudya chako pa madzi,

udzachipezanso patapita masiku ambiri.

2Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu,

pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.

3Ngati mitambo yadzaza ndi madzi,

imagwetsa mvula pa dziko lapansi.

Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto,

ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.

4Amene amayangʼana mphepo sadzadzala;

amene amayangʼana mitambo sadzakolola.

5Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo,

kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi,

momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu,

Mlengi wa zinthu zonse.

6Dzala mbewu zako mmawa

ndipo madzulo usamangoti manja lobodo,

pakuti sudziwa chimene chidzapindula,

mwina ichi kapena icho,

kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.

Kumbukira Mlengi Wako

7Kuwala nʼkwabwino,

ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.

8Munthu akakhala wa zaka zambiri,

mulekeni akondwerere zaka zonsezo,

koma iye azikumbukira masiku a mdima,

pakuti adzakhala ochuluka.

Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.

9Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono,

ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako.

Tsatira zimene mtima wako ukufuna,

ndiponso zimene maso ako akuona,

koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo

Mulungu adzakuweruza.

10Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako,

upewe zokupweteka mʼthupi mwako,

pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.