以赛亚书 8 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 8:1-22

预言灾难降临

1耶和华对我说:“你去拿块大的写字板,用通用的文字在上面写上‘玛黑珥·沙拉勒·哈施·罢斯8:1 玛黑珥·沙拉勒·哈施·罢斯”意思是“快速掳掠,迅速抢夺”。2我会吩咐忠信的祭司乌利亚耶比利迦的儿子撒迦利亚为这事做见证。” 3以赛亚与妻子同房,她就怀孕生了个儿子。耶和华对我说:“给他取名叫玛黑珥·沙拉勒·哈施·罢斯4因为这孩子会叫父亲母亲之前,亚述王必把大马士革的财富和撒玛利亚的战利品洗劫一空。” 5耶和华又对我说: 6“因为这些人拒绝接受我如西罗亚河缓缓流水般的温柔照顾,反倒因与利迅利玛利的儿子结盟而欢喜, 7我要差来亚述王的军队,使他们像幼发拉底河的洪流一样汹涌而来,淹没一切水道,漫过河岸, 8席卷犹大,使整个犹大几遭灭顶之灾。他必展开双翼横扫你的土地。”愿上帝与我们同在!

9列国啊,你们必被打垮、击溃!

远方的人啊,你们要听!

整装备战吧,但你们必被击垮!

整装备战吧,但你们必被击垮!

10你们设计谋吧,但休想得逞!

你们定策略吧,但休想成功!

因为上帝与我们同在。

当敬畏主

11耶和华大能的手按在我身上,警告我不可效法这些人。祂说: 12“他们认为是阴谋的,你们不要认为是阴谋。他们所怕的,你们不要怕,也不要畏惧。 13你们当尊万军之耶和华为圣,当敬畏祂,畏惧祂。 14祂必作人的圣所,也要作以色列犹大的绊脚石和使人跌倒的磐石,作耶路撒冷居民的陷阱和网罗。 15许多人必被绊倒,摔得粉身碎骨;他们必被网罗缠住、捕获。” 16我的门徒啊,你们要把上帝的训诲卷起来,用印封好。 17虽然耶和华掩面不顾雅各家,但我仍要等候祂,冀望于祂。 18看啊,我和祂所赐给我的儿女在以色列是征兆。这征兆来自住在锡安山的万军之耶和华。 19有人让你们去求问那些念念有词的巫师和术士,你们不要去。你们要去求问你们的上帝,活人的事怎能求问死人呢? 20人应该遵循耶和华的训诲和法度。人若不遵循祂的话,必看不到曙光。 21他们必困苦,饥饿,到处流浪,并在饥饿中怒气冲冲地咒骂他们的君王,亵渎上帝。 22他们抬头望天,低头看地,看到的尽是患难、痛苦和黑暗。他们必被扔进黑暗中。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 8:1-22

Asiriya, Chida cha Yehova

1Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira. 2Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”

3Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’ 4Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”

5Yehova anayankhulanso ndi Ine;

6“Popeza anthu a dziko ili akana

madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu,

ndipo akukondwerera Rezini

ndi mwana wa Remaliya,

7nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa

madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo;

mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo.

Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse

ndi mʼmagombe ake onse.

8Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira,

adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi.

Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse,

iwe Imanueli!”

9Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere!

Tamverani, inu mayiko onse akutali.

Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!

Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!

10Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu,

kambiranani zochita, koma zidzalephereka,

pakuti Mulungu ali nafe.

Yehova Achenjeza Mneneri

11Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:

12“Usamanene kuti ndi chiwembu,

chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu

usamaope zimene anthuwa amaziopa,

ndipo usamachite nazo mantha.

13Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera,

ndiye amene uyenera kumuopa,

ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,

14ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika;

koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala

mwala wopunthwitsa,

mwala umene umapunthwitsa anthu,

thanthwe limene limagwetsa anthu.

Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.

15Anthu ambiri adzapunthwapo

adzagwa ndi kuthyokathyoka,

adzakodwa ndi kugwidwa.”

16Manga umboniwu

ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.

17Ndidzayembekezera Yehova,

amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo.

Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.

18Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.

19Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo, 20kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala. 21Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo. 22Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.