以赛亚书 39 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 39:1-8

巴比伦的使者

1那时,巴比伦王——巴拉但的儿子米罗达·巴拉但听说希西迦患病、后来痊愈,便派人送去书信和礼物。 2希西迦欣然接见使者,让他们观看国库里的金银、香料、珍贵膏油、所有兵器和一切宝物。希西迦把宫中及国内的一切都给他们看。

3以赛亚先知来见希西迦王,问他:“这些人说了些什么?他们从哪里来?”

希西迦答道:“他们从遥远的巴比伦来。”

4以赛亚问:“他们在你宫中看见了什么?”

希西迦答道:“他们看到了我宫中的一切。我把国库里的一切都给他们看了。”

5以赛亚希西迦说:“你听着,万军之耶和华说, 6‘终有一天,你王宫中的一切和你祖先积攒到现在的一切,必一件不留地被掳到巴比伦。这是耶和华说的。 7你的子孙当中必有人被掳去,在巴比伦王的宫中做太监。’” 8希西迦以赛亚说:“耶和华借你说的话很好。”因为他想:“我有生之年将平安稳妥。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 39:1-8

Nthumwi Zochokera ku Babuloni

1Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira. 2Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.

3Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?”

Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”

4Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?”

Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”

5Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse: 6Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe. 7Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”

8Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”