以赛亚书 25 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 25:1-12

赞美之歌

1耶和华啊!你是我的上帝,我要尊崇你,赞美你的名。你信实无比,

按你古时定下的计划行了奇妙的事。

2你使城邑沦为废墟,

使坚垒沦为荒场。

外族人的宫殿不复存在,

永远不能重建。

3因此,强盛的国家必颂扬你,

残暴的民族必敬畏你。

4你是贫穷人的避难所,

是困苦之人患难中的避难所,

你是避风港,

是酷暑中的阴凉处。

残暴之徒的气息好像吹袭墙垣的暴风,

5又像沙漠中的热气。

但你平息外族人的喧哗,

止息残暴之徒的歌声,

好像云朵消去酷热。

6锡安山上,万军之耶和华必为天下万民摆设丰盛的宴席,有陈年佳酿和精选的美食。 7在这山上,祂必除去遮蔽万民的面纱和笼罩万国的幔子。 8祂必永远吞灭死亡。主耶和华必擦去各人脸上的眼泪,从世上除掉祂子民的羞辱。这是耶和华说的。 9到那日,人们必说:“看啊,这是我们的上帝,我们信靠祂,祂拯救了我们。这是耶和华,我们信靠祂,我们要因祂的拯救而欢喜快乐。” 10耶和华必伸手保护这山,但摩押人必被践踏,像干草被践踏在粪池中。 11他们必在里面张开手臂,好像张开手臂游泳的人一样。耶和华必摧毁他们的骄傲,挫败他们手中的诡计。 12祂必拆毁他们高大坚固的城墙,将其夷为平地、化为尘土。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 25:1-12

Nyimbo Yotamanda Yehova

1Yehova ndinu Mulungu wanga;

ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu,

pakuti mwachita zodabwitsa

zimene munakonzekeratu kalekale

mokhulupirika kwambiri.

2Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala.

Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja,

linga la anthu achilendo lero si mzindanso

ndipo sidzamangidwanso.

3Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani;

mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.

4Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka,

mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake.

Mwakhala ngati pobisalirapo

pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa.

Pakuti anthu ankhanza

ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,

5ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma.

Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo.

Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha,

inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.

6Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera

anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino.

Phwando la nyama yonona

ndi vinyo wabwino kwambiri.

7Iye adzachotsa kulira

kumene kwaphimba anthu ngati nsalu.

Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.

8Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya,

Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso

mwa munthu aliyense;

adzachotsa manyazi a anthu ake

pa dziko lonse lapansi,

Yehova wayankhula.

9Tsiku limenelo iwo adzati,

“Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu;

ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa.

Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira;

tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”

10Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake;

ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo,

ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.

11Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo,

ngati mmene amachitira munthu wosambira.

Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo

ngakhale luso la manja awo.

12Iye adzagumula malinga awo ataliatali

ndipo adzawagwetsa

ndi kuwaponya pansi,

pa fumbi penipeni.