以赛亚书 14 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 14:1-32

以色列人必重归故土

1耶和华必怜悯雅各,再次选择以色列人做祂的子民,把他们安置在他们自己的土地上。外族人必与他们联合,归入以色列2各国必帮助他们重返故乡。在耶和华赐给他们的土地上,外族人必做他们的仆婢。他们必掳掠以前掳掠他们的人,统治以前压制他们的人。

对巴比伦的讽刺

3耶和华使他们脱离痛苦、悲伤和残酷奴役的时候, 4他们必这样讥笑巴比伦王:

“暴君灭亡了!

暴政结束了!

5耶和华折断了邪恶君主的权杖。

6他曾狂怒地攻伐列邦,

无休无止,

怒气冲冲地征服列国,

大肆迫害。

7如今天下太平,

人人欢呼歌唱,

8连松树和黎巴嫩的香柏树都欢喜快乐地说,

‘自从他灭亡后,

再没有人上来砍伐我们。’

9巴比伦王啊,你下到阴间,

阴间兴奋地迎接你,

那些在世上做过君王和首领的阴魂都从座位上站起来迎接你,

10对你说,

‘你如今也跟我们一样软弱无能。’

11你的荣耀和琴声一同落入阴间,

虫成了你的床铺,

蛆成了你的被子。

12“明亮的晨星、黎明之子啊,

你怎么从天上坠落下来?

你这打败列国的怎么被砍倒在地上?

13你曾想,‘我要升到天上,

把自己的宝座设在上帝的众星之上;

我要坐在遥远的北方众神明聚会的山上;

14我要升到云天之上,

使自己与至高者一样。’

15可是,你必坠入阴间,

掉进死亡的深坑。

16看见你的都瞪大眼睛盯着你,

都在想,‘这就是那曾使大地震动、列国颤抖的人吗?

17这就是那曾使天下荒凉、城邑倾覆、不肯释放俘虏回家的人吗?’

18万国的君王都躺在自己华丽的陵墓中,

19只有你像一根毫无用处的树枝,

被抛弃在自己的坟墓外。

你就像一具遭人践踏的尸体,

与丧身刀下的人一同被扔进乱石坑里。

20你必得不到君王的葬礼,

因为你祸国殃民,

杀害自己的百姓。

“恶人的子孙必永远被遗忘。

21预备杀戮他的子孙吧,

因为他们的祖先罪恶深重,

免得他们兴起统治世界、到处建造城邑。”

22万军之耶和华说:

“我必攻击巴比伦

铲除巴比伦的名号、余民和后裔。

这是耶和华说的。

23我必用毁灭的扫帚清扫它,

使它成为沼泽之地和刺猬的住所。

这是万军之耶和华说的。”

关于亚述的预言

24万军之耶和华起誓说:

“我的计划必实现,

我的旨意必成就。

25我必在我的土地上击垮亚述人,

在我的山上践踏他们,

除去他们加在我子民身上的轭和重担。

26这是我对全世界所定的计划,

是向列国伸出的惩罚之手。”

27万军之耶和华定了计划,

谁能阻挠呢?

祂的手已经伸出,

谁能叫祂收回呢?

关于非利士的预言

28亚哈斯王驾崩那年,我得到以下预言:

29非利士人啊,

不要因击打你们的杖已经折断14:29 击打你们的杖已经折断”指攻击非利士的王已死。便高兴。

因为那杖就像一条蛇,

必生出一条更危险的蛇,

一条会飞的毒蛇。

30贫穷人必衣食无忧,

困苦人必安然度日,

但我必用饥荒除掉你们的子孙,

消灭你们残存的人。

31城门啊,哀号吧!

城邑啊,哭喊吧!

非利士人啊,战抖吧!

因为有阵容整齐的军队从北方如尘烟滚滚而来。

32该怎样回复外国的使者呢?

要告诉他们:“耶和华建立了锡安

祂困苦的子民必得到保护。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 14:1-32

1Yehova adzachitira chifundo Yakobo;

adzasankhanso Israeli

ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo.

Alendo adzabwera kudzakhala nawo

ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.

2Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli

ku dziko lawo.

Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja

kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova.

Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo.

Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.

3Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani, 4mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti,

Wopsinja uja watha!

Ukali wake uja watha!

5Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa,

Iye waphwanya ndodo ya olamulira.

6Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali

powamenya kosalekeza,

Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali

ndikuwazunza kosalekeza.

7Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere;

ndipo akuyimba mokondwa.

8Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni

ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti,

“Chigwetsedwere chako pansi,

palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”

9Ku manda kwatekeseka

kuti akulandire ukamabwera;

mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri

a dziko lapansi, yadzutsidwa.

Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu

ayimiritsidwa pa mipando yawo.

10Onse adzayankha;

adzanena kwa iwe kuti,

“Iwenso watheratu mphamvu ngati ife;

Iwe wafanana ndi ife.”

11Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda,

pamodzi ndi nyimbo za azeze ako;

mphutsi zayalana pogona pako

ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi.

12Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba,

iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha!

Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi,

Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!

13Mu mtima mwako unkanena kuti,

“Ndidzakwera mpaka kumwamba;

ndidzakhazika mpando wanga waufumu

pamwamba pa nyenyezi za Mulungu;

ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako,

pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.

14Ndidzakwera pamwamba pa mitambo;

ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”

15Koma watsitsidwa mʼmanda

pansi penipeni pa dzenje.

16Anthu akufa adzakupenyetsetsa

nadzamalingalira za iwe nʼkumati,

“Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi

ndi kunjenjemeretsa maufumu,

17munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu,

amene anagwetsa mizinda yake

ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”

18Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu

aliyense mʼmanda akeake.

19Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako,

ngati nthambi yowola ndi yonyansa.

Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa;

amene anabayidwa ndi lupanga,

anatsikira mʼdzenje lamiyala

ngati mtembo woponderezedwa.

20Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu,

chifukwa unawononga dziko lako

ndi kupha anthu ako.

Zidzukulu za anthu oyipa

sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.

21Konzani malo woti muphere ana ake aamuna

chifukwa cha machimo a makolo awo;

kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi

ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.

22Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni.

Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo.

Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,”

akutero Yehova.

23“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu

ndiponso dambo lamatope;

ndidzawusesa ndi tsache lowononga,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

Za Kulangidwa kwa Asiriya

24Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti,

“Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho,

ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.

25Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa;

ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga;

ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga,

ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”

26Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi,

ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.

27Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse?

Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?

Za Kulangidwa kwa Afilisti

28Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:

29Musakondwere inu Afilisti nonse

kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa;

chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri,

ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.

30Osaukitsitsa adzapeza chakudya

ndipo amphawi adzakhala mwamtendere.

Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala,

ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.

31Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda!

Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse!

Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto,

ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.

32Kodi tidzawayankha chiyani

amithenga a ku Filisitiya?

“Yehova wakhazikitsa Ziyoni,

ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”