以西结书 25 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以西结书 25:1-17

预言审判外族人

1耶和华对我说: 2“人子啊,你要面向亚扪人,说预言斥责他们, 3告诉他们要听主耶和华的话。主耶和华说,‘当我的圣所被亵渎,以色列变得荒凉,犹大人被掳的时候,你们竟然哈哈而乐。 4所以我要使东方人侵占你们的地方。他们必在你们的土地上安营扎寨,吃你们出产的果子,喝你们牛羊的奶。 5我要使拉巴成为骆驼的草场,使亚扪人的土地变成羊群歇息之处,这样你们便知道我是耶和华。

6“主耶和华说,‘你们看到以色列的灾祸,便幸灾乐祸,手舞足蹈。 7因此,我要伸手攻击你们,使你们成为各国的俘虏。我必从万民中铲除你们,从万国中消灭你们,使你们灭绝。这样,你们就知道我是耶和华。’

斥责摩押

8“耶和华说,‘摩押西珥嘲笑犹大与其他各国没有两样。 9所以我要攻陷摩押边界的城邑,就是那地方引以为荣的伯·耶西末巴力·免基列亭10我要将它和亚扪人一起交给东方人统治,使亚扪人从此被列国遗忘。 11我必审判摩押人,这样他们就知道我是耶和华。’

斥责以东

12“耶和华说,‘因为以东报复犹大,犯了大罪。 13所以,我要伸手攻击以东,铲除那里的人和牲畜,使地荒废,从提幔直到底但以东人要倒在刀下。 14我要借我以色列子民的手向以东报仇。以色列人会照我的烈怒惩罚他们。那时,他们就会尝到我报应他们的滋味,这是主耶和华说的。’

斥责非利士

15“主耶和华说,‘非利士人心存仇恨,为了报世仇要毁灭犹大16所以我必伸手攻击他们,铲除基利提人,毁灭沿海残余的人。 17我要报应他们,发烈怒惩罚他们。我报应他们的时候,他们就知道我是耶和华。’”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 25:1-17

Za Chilango cha Aamoni

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, tembenukira anthu a ku Amoni ndipo unenere mowadzudzula. 3Awawuze kuti, ‘Inu anthu a ku Amoni, imvani zimene Ambuye Yehova akunena. Iye akuti: Inu munanena mawu onyoza pamene Nyumba yanga yopatulika inkayipitsidwa. Munanyozanso dziko la Israeli pamene linaguga ndiponso anthu a ku Yuda pamene anatengedwa ukapolo. 4Nʼchifukwa chake Ine ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu akummawa ngati cholowa chawo. Iwo adzamanga misasa yawo ndi kukhoma matenti awo pakati panu. Adzadya zipatso zanu ndi kumwa mkaka wanu. 5Ndidzasandutsa Raba kuti akhale busa la ngamira ndi mizinda ya Aamoni kuti ikhale makola a nkhosa. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 6Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu munawomba mʼmanja ndi kumalumphalumpha. Munkakondwa mu mtima mwanu pamene munkanyoza dziko la Israeli. 7Nʼchifukwa chake ndidzatambasula dzanja langa kuti ndikulangeni, ndipo ndidzakuperekani kuti mukhale chofunkha cha anthu a mitundu ina. Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukufafanizani mʼmayiko onse. Ndidzakuwonongani, ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova!’ ”

Za Chilango cha Mowabu

8“Ambuye Yehova akuti, ‘Anthu a ku Mowabu ndi a ku Seiri ananena kuti anthu a ku Yuda ali ngati mayiko ena onse.’ 9Nʼchifukwa chake ndidzagumula mbali ina ya Mowabu, kuyambira ku mizinda yake ya kumalire; mizinda yokongola ya Beti-Yesimoti, Baala-Meoni ndi Kiriataimu. 10Ndidzapereka Amowabu pamodzi ndi Aamoni mʼmanja mwa anthu akummawa kotero kuti Aamoni adzayiwalikiratu pakati pa anthu a mitundu ina. 11Ndidzawalangadi Amowabuwo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

Za Chilango cha Edomu

12“Ambuye Yehova akuti, ‘Pakuti Edomu analipsira Ayuda, ndiye kuti analakwa kwambiri pochita zimenezi. 13Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kulanga Edomu ndi kupha anthu ake ndiponso nyama zawo. Ndidzawonongeratu Edomu ndipo adzaphedwa ndi lupanga kuchokera ku Temani mpaka ku Dedani. 14Ndidzalanga Edomu ndi dzanja la anthu anga Aisraeli. Adzalanga anthu a ku Edomu molingana ndi mkwiyo ndi ukali wanga. Choncho adzaona kulipsira kwanga akutero Ambuye Yehova.’ ”

Za Chilango cha Filisitiya

15“Ambuye Yehova akuti, ‘Afilisti analanga anthu anga mwankhanza ndi kuwalipsira. 16Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kukantha Afilistiwo. Ndidzafafaniza Akereti ndi kuwononga iwo amene amakhala mʼmbali mwa nyanja. 17Ndidzawabwezera chilango choopsa ndipo ndidzawalanga mu mkwiyo wanga. Ndikadzawalipsira ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”