生命之道
1太初,道已经存在,道与上帝同在,道就是上帝。 2太初,道就与上帝同在。 3万物都是借着祂造的1:3 “造的”或译“存在”。,受造之物没有一样不是借着祂造的。 4祂里面有生命,这生命是人类的光。 5光照进黑暗里,黑暗不能胜过1:5 “胜过”或译“接受”或“明白”。光。
6有一个人名叫约翰,是上帝差来的。 7他来是要为光做见证,叫世人可以借着他而相信。 8约翰不是那光,他来是为那光做见证。 9那照亮世人的真光来到了世上。 10祂来到自己所创造的世界,世界却不认识祂。 11祂来到自己的地方,自己的人却不接纳祂。 12但所有接纳祂的,就是那些信祂的人,祂就赐给他们权利成为上帝的儿女。 13这些人既不是从人的血缘关系生的,也不是从人的情欲或意愿生的,而是从上帝生的。
14道成为肉身,住在我们中间,充满了恩典和真理。我们见过祂的荣耀,正是父独一儿子的荣耀。
15约翰为祂做见证的时候,高声喊道:“这就是我以前所说的那位,‘祂在我以后来却比我位分高,因为祂在我之前已经存在了。’” 16从祂的丰盛里,我们一次又一次地领受了恩典。 17因为律法是借着摩西颁布的,恩典和真理是借着耶稣基督赐下来的。 18从来没有人见过上帝,只有父怀中的独一上帝1:18 “独一上帝”有古卷作“独一儿子”。把祂显明出来。
施洗者约翰的见证
19以下是约翰的见证。犹太人从耶路撒冷派祭司和利未人来找约翰,查问他是谁。 20约翰毫不隐瞒地说:“我不是基督。”
21他们问:“那么,你是谁?是以利亚吗?”
他说:“不是。”
他们又问:“你是那位先知吗?”
他说:“也不是。”
22他们又追问:“你到底是谁?我们好回复差我们来的人。你自己说你是谁?”
23他说:“我就是在旷野大声呼喊‘修直主的路’的那个人,正如以赛亚先知所言。”
24派来的人当中有几个法利赛人1:24 “派来的人当中有几个法利赛人”或译“法利赛人派来的那几个人”。,他们问他: 25“你既然不是基督,不是以利亚,也不是那位先知,那你为什么给人施洗呢?”
26约翰答道:“我是用水施洗,但在你们中间有一位你们不认识的, 27祂虽然是在我以后来的,我就是给祂解鞋带也不配。” 28这事发生在约旦河东岸的伯大尼,那里是约翰给人施洗的地方。
上帝的羔羊
29次日,约翰看见耶稣走过来,就说:“看啊!上帝的羔羊,除去世人罪恶的! 30这就是我以前所说的那位,‘有一个人在我以后来却比我位分高,因为祂在我之前已经存在了。’ 31我以前并不认识祂,现在我用水给人施洗,是要把祂显明给以色列人。”
32约翰又做见证说:“我看见圣灵好像鸽子一样从天降下,住在祂身上。 33我本来不认识祂,但那位差我来用水给人施洗的告诉我,‘你看见圣灵降下,住在谁身上,谁就是用圣灵给人施洗的。’ 34我看见了,便做见证,祂就是上帝的儿子。”
第一批门徒
35再次日,约翰和两个门徒站在那里, 36他看见耶稣经过,就说:“看啊!这是上帝的羔羊!” 37两个门徒听见他的话,便跟从了耶稣。 38耶稣转过身来,看见他们跟着,便问:“你们想要什么?”
他们说:“老师1:38 “老师”希腊文是“拉比”,特指犹太教的老师,下同。,你住在哪里?”
39耶稣说:“你们来看吧。”他们便跟着去看耶稣住的地方。到了那里大约下午四点了,他们就住在耶稣那里。 40听见约翰的话后跟从耶稣的两个人中,有一个是西门·彼得的弟弟安得烈。 41他首先去找他哥哥西门,说:“我们找到弥赛亚了!”弥赛亚的意思是基督1:41 希伯来文的“弥赛亚”和希腊文的“基督”都是“受膏者”的意思。。 42他带着西门去见耶稣。
耶稣看着西门,对他说:“约翰的儿子西门,你要改名为矶法。”矶法的意思是彼得。
43又过了一天,耶稣决定去加利利。祂遇见了腓力,就对他说:“跟从我!” 44腓力是伯赛大人,与彼得、安得烈是同乡。 45腓力去找拿但业,对他说:“我们遇见了摩西律法书和先知书记载的那位!祂是约瑟的儿子耶稣,从拿撒勒来的。”
46拿但业说:“拿撒勒还会出什么好东西?”
腓力说:“你来看看吧!”
47耶稣看见拿但业走过来,就指着他说:“看啊,这是个真正的以色列人!他心里毫无诡诈。”
48拿但业问耶稣:“你怎么会认识我?”
耶稣答道:“腓力还没有去找你之前,我就看见你在无花果树下了。”
49拿但业说:“老师,你是上帝的儿子!你是以色列的王!”
50耶稣说:“我说看见你在无花果树下,你就信我吗?将来你还要看见比这更大的事。 51我实实在在地告诉你们,你们会看见天门敞开,上帝的天使以人子1:51 “人子”是耶稣的自称,耶稣在这里自比天梯,背景请参见创世记28:12。为梯上上下下。”
Mawu Asandulika Thupi
1Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu. 2Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
3Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa. 4Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu. 5Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
6Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane. 7Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire. 8Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika. 9Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
10Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye. 11Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye. 12Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu; 13ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
14Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
15Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’ ” 16Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso. 17Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu. 18Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
Yohane Mʼbatizi Akana kuti Iye ndi Khristu
19Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani. 20Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”
21Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?”
Iye anati, “Sindine.”
“Kodi ndiwe Mneneri?”
Iye anayankha kuti, “Ayi.”
22Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”
23Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’ ”
24Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa 25anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”
26Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa. 27Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”
28Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.
Yesu Mwana Wankhosa wa Mulungu
29Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi! 30Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’ 31Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”
32Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye. 33Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’ 34Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”
Ophunzira Oyamba a Yesu
35Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake. 36Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”
37Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu. 38Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?”
Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”
39Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.”
Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.
40Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu. 41Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).
42Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).
Yesu Ayitana Filipo ndi Natanieli
43Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”
44Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida. 45Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”
46Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?”
Filipo anati, “Bwera udzaone.”
47Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
48Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?”
Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”
49Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”
50Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.” 51Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”