1我是耶稣基督的奴仆和使徒西门·彼得,写信给借着我们的上帝和救主耶稣基督的义,与我们得到同样宝贵信心的人。
2愿你们因认识上帝和我们主耶稣而得到丰富的恩典和平安!
追求长进
3因为我们认识了用自己的荣耀和美德呼召我们的上帝,上帝以祂神圣的能力将生命与敬虔所需要的一切赐给了我们。 4借此,祂已将既宝贵又伟大的应许赏给了我们,使我们脱离世上私欲带来的败坏,能够有份于上帝的性情。
5正因如此,你们要加倍努力,不仅要有信心,还要有好的德行;不仅要有好的德行,还要有知识; 6不仅要有知识,还要有节制;不仅要有节制,还要有忍耐;不仅要有忍耐,还要有敬虔; 7不仅要有敬虔,还要有爱弟兄姊妹的心;不仅要有爱弟兄姊妹的心,还要有爱众人的心。 8如果充分具备了这些品德,你们对我们主耶稣基督的认识就不会停滞不前,毫无收获。 9缺乏上述品德的人不是瞎眼就是目光短浅,忘记他从前的罪已经得到洁净。
10所以,弟兄姊妹,你们要更加努力,以确定自己蒙了呼召和拣选。这样,你们就绝不会失足犯罪, 11进入我们的主和救主耶稣基督永恒国度的大门必为你们敞开。
12虽然你们已经知道这些事,并且在所领受的真道上也很坚固,但我还是要常常提醒你们。 13我觉得应当趁着我还在世的时候1:13 “还在世的时候”希腊文是“还在这帐篷里的时候”,作者用帐篷代表自己的身体。提醒你们,激励你们, 14因我知道自己离世的日子已经不远了,正如我们的主耶稣基督指示我的。 15我要尽力使你们在我离世以后仍然常常记得这些事。
见证基督的荣耀
16我们从前告诉你们有关主耶稣基督的大能和祂降临的事,并非根据巧妙虚构的神话,而是我们亲眼见过祂的威荣。 17祂从父上帝那里得到了尊贵和荣耀,那时从极大的荣光中有声音对祂说:“这是我的爱子,我甚喜悦祂。” 18当时我们和祂一同在圣山上,亲耳听见了这来自天上的声音。
19这使我们更加确信先知的预言。你们要留意这些预言,把这些预言看作照耀在黑暗中的明灯,一直到天破晓、晨星在你们心中升起。 20你们首先该知道:圣经上的一切预言都不可随人的私意解释, 21因为预言绝非出于人的意思,都是人受了圣灵的感动,讲出上帝的信息。
1Ndine Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu.
Kwa anthu amene analandira chikhulupiriro cha mtengowapatali chomwe ifenso tinalandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.
2Chisomo ndi mtendere zochuluka zikhale nanu pomudziwa Mulungu ndi Yesu Ambuye athu.
Kudziwa za Mayitanidwe ndi za Kusankhidwa Kwathu
3Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ubwino wake. 4Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo, anatipatsa malonjezo opambana kwambiri ndi a mtengowapatali. Amenewa ndi malonjezo amene amakuthandizani kulandira nawo moyo wa Mulungu, titapulumuka ku chiwonongeko chimene chili mʼdziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoyipa.
5Choncho, chitani khama kuwonjezera moyo wabwino pa chikhulupiriro chanu, ndipo pa moyo wabwino muwonjezerepo nzeru. 6Pa nzeru muwonjezerepo kudziretsa, pa kudziretsa muwonjezerepo chipiriro, ndipo pa chipiriro muwonjezerepo khalidwe lolemekeza Mulungu. 7Pa khalidwe lolemekeza Mulungu muwonjezerepo chifundo cha ubale, pa chifundo cha ubale muwonjezerepo chikondi. 8Ngati zonsezi zikhala mwa inu nʼkumachuluka, zidzakuthandizani kuti musakhale aulesi ndi osapindula ndi chidziwitso chanu cha Ambuye athu Yesu Khristu. 9Koma ngati wina alibe zimenezi, ndi wakhungu sangathe kuona patali, ndipo wayiwala kuti anayeretsedwa machimo ake akale.
10Nʼchifukwa chake abale anga, funitsitsani kuti mayitanidwe ndi masankhidwe anu akhale otsimikizika. Pakuti ngati muchita zinthu izi, simudzagwa konse. 11Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.
Kukhala Oyera Mtima
12Tsono ine ndidzakukumbutsani nthawi zonse za zinthu zimenezi, ngakhale kuti mumazidziwa ndipo kuti munakhazikika mʼchoonadi chimene muli nacho tsopano. 13Ndikuganiza kuti nʼkoyenera ndikanali mu msasa uno, kuti ndikutsitsimutseni ndi kukukumbutsani, 14chifukwa ndikudziwa kuti posachedwapa ndikuchoka mu msasa uno, monga Ambuye athu Yesu Khristu anandidziwitsiratu. 15Ndipo ndidzayesetsa kuti nditachoka, mudzakumbukire nthawi zonse.
16Ife sitinatsate nkhani zongopeka titakuwuzani za mphamvu zake ndi zakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, koma tinaona ndi maso athu za ukulu wake. 17Pakuti Iye analandira ulemu ndi ulemerero kuchokera kwa Mulungu Atate atamufikira mawu ochokera ku ulemerero wa ukulu akuti, “Uyu ndi mwana wanga amene Ine ndimukonda, amene ndimakondwera naye kwambiri.” 18Ifeyo tinamva mawuwa akuchokera kumwamba pamene tinali naye pamodzi pa phiri lopatulika lija.
19Tsono ifenso tili ndi mawu a uneneri amene ndi odalirika kwambiri ndipo inu mudzachita bwino mukawasamalira mawuwa, monga kuwunika kumene kukuwala mu mdima, mpaka tsiku lidzayambe kucha, pamene nthanda idzayambe kuwala mʼmitima mwanu. 20Kuposa zonse, inu muyenera kuzindikira kuti palibe mawu a uneneri amene amatanthauzidwa pa okha. 21Pakuti mawu a uneneri sanadze mwa kufuna kwa anthu, koma anthu anayankhula zochokera kwa Mulungu, Mzimu Woyera atawayankhulitsa.