Песнь 124
Песнь восхождения.
1Те, кто надеется на Вечного, – как гора Сион:
не поколеблются, пребудут вовеки.
2Как горы окружают Иерусалим,
так Вечный окружает Свой народ
отныне и вовеки.
3Не вечно власти нечестивых
быть на земле, принадлежащей праведным,
иначе праведные, по их примеру,
сами станут творить беззаконие.
4Будь добр, Вечный, к добрым
и правым в сердцах своих.
5Но тех, кто следует кривыми путями,
да отвергнет Вечный вместе со злодеями.
Мир Исроилу!
Salimo 124
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
1Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
anene tsono Israeli,
2akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
potiwukira anthuwo,
3iwo atatipsera mtima,
akanatimeza amoyo;
4chigumula chikanatimiza,
mtsinje ukanatikokolola,
5madzi a mkokomo
akanatikokolola.
6Atamandike Yehova,
amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame
yokodwa mu msampha wa mlenje;
msampha wathyoka,
ndipo ife tapulumuka.
8Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.