Песнь 112
Славьте Вечного!
1Воздайте хвалу, о рабы Вечного,
воздайте хвалу имени Вечного!
2Да будет прославлено имя Вечного
отныне и вовеки.
3От востока и до запада
да будет прославлено имя Вечного.
4Вечный превознесён над всеми народами,
и слава Его выше небес.
5Кто подобен Вечному, нашему Богу,
восседающему на высоте
6и склоняющемуся, чтобы видеть,
что происходит на небе и на земле?
7Он поднимает бедного из праха
и возвышает нищего из грязи,
8чтобы посадить их с вождями,
с вождями их народа.
9Бесплодную женщину делает
счастливой матерью в её доме.
Славьте Вечного!
Salimo 112
1Tamandani Yehova.
Wodala munthu amene amaopa Yehova,
amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;
mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,
ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;
wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,
amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6Ndithu sadzagwedezeka;
munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;
mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;
potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,
chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;
nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;
adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.
Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.