Песнь 19
1Дирижёру хора. Песнь Давуда.
2Да ответит Вечный тебе в день печали;
да хранит тебя имя Бога Якуба.
3Да пошлёт Он помощь тебе из святилища
и поддержит тебя с Сиона.
4Да вспомнит Он все жертвы твои
и всесожжения твои примет. Пауза
5Да даст Он тебе то, чего ты желаешь,
и исполнит все твои намерения.
6Мы будем кричать от радости о твоей победе
и поднимем знамёна во имя нашего Бога.
Да исполнит Вечный все твои просьбы.
7Теперь я знаю: Вечный спасает Своего помазанника,
отвечает ему со святых небес Своих
спасающей силой Своей правой руки.
8Кто хвалится колесницами, а кто конями,
мы же хвалимся именем Вечного, нашего Бога.
9Они ослабели и падают,
а мы поднимаемся и стоим твёрдо.
10Вечный, даруй царю победу!
Ответь нам19:10 Или: «…даруй победу! Царь, ответь нам»., когда мы взываем!
Salimo 19
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
1Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu;
thambo limalalikira ntchito za manja ake.
2Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri,
usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
3Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse;
liwu lawo silimveka.
4Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi,
mawuwo amafika mpaka
kumalekezero a dziko lapansi.
5Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake,
ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
6Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo
ndi kuzungulira mpaka mbali inanso;
palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
7Lamulo la Yehova ndi langwiro,
kutsitsimutsa moyo.
Maumboni a Yehova ndi odalirika,
amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
8Malangizo a Yehova ndi olungama,
amapereka chimwemwe mu mtima.
Malamulo a Yehova ndi onyezimira,
amapereka kuwala.
9Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro,
chimakhala mpaka muyaya.
Maweruzo a Yehova ndi owona
ndipo onse ndi olungama;
10ndi a mtengowapatali kuposa golide,
kuposa golide weniweni;
ndi otsekemera kuposa uchi,
kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
11Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo;
powasunga pali mphotho yayikulu.
12Ndani angathe kudziwa zolakwa zake?
Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
13Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa;
iwo asandilamulire.
Kotero ndidzakhala wosalakwa,
wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
14Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga
zikhale zokondweretsa pamaso panu,
Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.